< 2 царів 19 >

1 І сталося, як почув це цар Єзекі́я, то розде́р свої шати та накрився вере́тою, і ввійшов до Господнього дому.
Mfumu Hezekiya atamva zimenezi, anangʼamba zovala zake navala chiguduli ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova.
2 І послав він Еліякима, начальника палати, і писаря Шевну, та старши́х із священиків, покритих вере́тами, до пророка Ісаї, Амосового сина.
Iye anatuma Eliyakimu, woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi ansembe akuluakulu, onse atavala ziguduli, kwa mneneri Yesaya mwana wa Amozi.
3 І сказали вони до нього: „Так сказав Єзекія: Цей день — це день горя й карта́ння та нару́ги! Бо підійшли діти аж до виходу утро́би, та немає сили породити!
Iwo anamuwuza kuti, “Hezekiya akunena kuti, ‘Lero ndi tsiku lamavuto, lachilango ndi lamanyazi. Ife lero tili ngati mayi woyembekezera amene pofika nthawi yoti achire akupezeka kuti alibe mphamvu zoberekera.
4 Може почує Господь, Бог твій, всі слова́ великого чашника, що його послав асирійський цар, пан його, на обра́зу Живого Бога, і Господь, Бог твій, покарає за слова́, які чув, а ти принесе́ш молитву за рештку, що ще знахо́диться“.
Mwina Yehova Mulungu wanu adzamva mawu onse a Rabusake amene mbuye wake, mfumu ya ku Asiriya anamutuma kudzanyoza Mulungu wamoyo, ndipo Mulunguyo adzamulanga chifukwa cha mawu amene Yehova Mulungu wanu wamva. Choncho pemphererani anthu otsala amene akanali ndi moyo.’”
5 І прийшли раби царя Єзекії до Ісаї.
Akuluakulu a Mfumu Hezekiya atafika kwa Yesaya,
6 І сказав їм Іса́я: „Так скажете вашому панові: Так сказав Господь: Не бійся тих слів, що почув ти, якими ображали Мене слуги асирійського царя!
Yesaya anawawuza kuti, “Kawuzeni mbuye wanu kuti, ‘Yehova akunena kuti: Usachite mantha ndi zimene wamva, mawu amene nthumwi za mfumu ya ku Asiriya zandinyoza nawo Ine.
7 Ось Я дам в нього духа, і він почує звістку, — і ве́рнеться до свого краю. І Я вражу́ його мече́м у його кра́ї“.
Tamverani! Ine ndidzayika mwa mfumuyo mzimu wina kotero kuti akadzamva mphekesera ya nkhondo, adzabwerera ku dziko lake ndipo Ine ndidzachititsa kuti aphedwe ndi lupanga kwawo komweko.’”
8 І вернувся великий чашник, і знайшов асирійського царя, що воював проти Лівни, бо почув, що той рушив із Лахішу.
Rabusake atamva kuti mfumu ya ku Asiriya yachoka ku Lakisi, iye anabwerera mʼmbuyo ndipo anakapeza mfumu ikuchita nkhondo ndi mzinda wa Libina.
9 А коли він почув про Тіргаку, царя етіопського, таке: „Ось він вийшов воювати з тобою!“то вернувся, і послав послів до Єзекії, говорячи:
Nthawi imeneyi Senakeribu analandira uthenga wakuti Tirihaka, mfumu ya ku Kusi, akubwera kudzachita naye nkhondo. Choncho iye anatumanso amithenga kwa Hezekiya ndi mawu awa:
10 „Так скажете до Єзекії, Юдиного царя, говорячи: „Нехай не зво́дить тебе Бог твій, що ти наді́єшся на Нього, кажучи: Не буде да́ний Єрусалим у руку асирійського царя.
“Kawuzeni Hezekiya mfumu ya Yuda kuti: Usalole kuti Mulungu amene ukumudalira akupusitse ponena kuti, ‘Yerusalemu sadzaperekedwa mʼmanja mwa mfumu ya ku Asiriya.’
11 Ось ти чув, що́ зроби́ли асирійські царі всім края́м, щоб учинити їх закляттям, а ти будеш урято́ваний?
Ndithu iwe unamva chimene mafumu a Asiriya anachita ku mayiko ena onse, kuti anawawononga kotheratu. Ndipo kodi iwe nʼkupulumuka?
12 Чи врятували їх боги тих народів, яких понищили батьки мої: Гозана, і Харана, і Рецефа, і синів Едена, що в Телассарі?
Kodi milungu ya mitundu imene makolo anga anayigonjetsa, milungu ya anthu a ku Gozani, Harani, Rezefi ndi Aedeni amene anali ku Teli Asara, inawapulumutsa?
13 Де він, цар Гамату, і цар Арпаду, і цар міста Сефарваїму, Гени та Івви?“
Kodi mafumu a Hamati, Aripadi ndi mafumu a mizinda ya Sefaravaimu, Hena ndi Iva, ali kuti?”
14 І взяв Єзекія ті листи з руки послів, і прочитав їх, і ввійшов у Господній дім. І Єзекія розгорну́в одного листа перед Господнім лицем.
Hezekiya analandira kalata kwa amithenga aja nayiwerenga. Pomwepo anapita ku Nyumba ya Yehova nayika kalatayo pamaso pa Yehova.
15 І Єзекія молився перед Господнім лицем і сказав: „Господи, Боже Ізраїлів, що сидиш на херуви́мах! Ти Той єдиний Бог для всіх царств землі, Ти створив небеса́ та землю!
Ndipo Hezekiya anapemphera kwa Yehova nati, “Inu Yehova Mulungu wa Israeli, Inu amene mumakhala pa Akerubi, Inu nokha ndinu Mulungu wolamulira maufumu onse a dziko lapansi. Inu munalenga kumwamba ndi dziko lapansi.
16 Нахили́, Господи, ухо Своє та й почуй! Відкрий, Господи, очі Свої та й побач, і почуй слова Санхеріва, що прислав ображати Живого Бога!
Inu Yehova, tcherani khutu lanu ndipo mumve Yehova tsekulani maso anu ndipo muone, imvani mawu onse amene Senakeribu watumiza kunyoza Inu Mulungu wamoyo.
17 Справді, Господи, асирійські царі попусто́шили ті народи та їхній край.
“Inu Yehova, nʼzoonadi kuti mafumu a Asiriya anawononga mitundu iyi ndi mayiko awo.
18 І кинули вони їхніх богів на огонь, бо не боги вони, а тільки чин лю́дських рук, дерево та камінь, і понищили їх.
Iwo anaponya milungu yawo pa moto ndi kuyiwononga pakuti sinali milungu koma mitengo ndi miyala chabe, yopangidwa ndi anthu.
19 А тепер, Господи, Боже наш, спаси нас від руки його, і нехай знають усі царства землі, що Ти Господь, Бог єдиний!“
Ndipo tsopano Inu Yehova Mulungu wathu, tipulumutseni ndithu mʼdzanja lake, kuti maufumu onse a dziko lapansi adziwe kuti Inu nokha, Inu Yehova, ndinu Mulungu.”
20 І послав Ісая, Амосів син, до Єзекії, говорячи: „Так сказав Госпо́дь, Бог Ізраїлів: Я почув те, про що ти молився до Мене, про Санхеріва, царя асирійського.
Ndipo Yesaya mwana wa Amozi anatumiza uthenga kwa Hezekiya wakuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndamva pemphero lako lonena za Senakeribu mfumu ya ku Asiriya.’”
21 Ось те слово, яке Господь говорив про нього: Горду́є тобою, сміється із тебе діви́ця, сіонська дочка́, вслід тобі головою хитає дочка́ Єрусалиму!
Mawu amene Yehova wayankhula wotsutsana naye ndi awa: “Namwali wa Ziyoni akukunyoza ndi kukuseka iwe. Mwana wamkazi wa Yerusalemu akupukusa mutu wake kumbuyo kwako.
22 Кого лаяв ти та ображав, і на ко́го пови́щив ти голос та вго́ру підніс свої очі? — На Святого Ізраїлевого!
Kodi iweyo wanyoza ndi kuchitira chipongwe yani? Kodi ndani amene wamufuwulira mawu ako ndi kumuyangʼana monyada? Wachitiratu izi Woyera wa Israeli!
23 Через послів своїх Господа ти ображав та казав: Із бе́зліччю своїх колесни́ць я вийшов на го́ри високі, на боки Ливану, і позру́бую ке́дри високі його, добі́рні його кипари́си, і ви́йду аж на вершо́к його на нічліг, — у гущину́ його саду.
Kudzera mwa amithenga ako wonyoza Ambuye. Ndipo wanena kuti, ‘Ndi magaleta ochuluka ndinakwera mapiri ataliatali, pa msonga za mapiri a Lebanoni. Ndigwetsa mitengo yake ya mkungudza yayitali kwambiri, mitengo yake ya payini yabwino kwambiri. Ndalowanso mʼkati mwake mwenimweni, mwa nkhalango yake yowirira kwambiri.
24 Я копаю та п'ю чужу воду, і стопо́ю своєї ноги повису́шую я всі єгипетські рі́ки!
Ndakumba zitsime ku mayiko achilendo ndipo ndinamwa madzi a kumeneko. Ndi mapazi anga ndawumitsa mitsinje yonse ya ku Igupto.’”
25 Хіба ти не чув, що віддавна зробив Я оце, що за днів стародавніх Я це був створи́в? Тепер же спровадив Я це, що ти нищиш міста поукріплювані, на купу румо́вищ обертаєш їх...
“‘Kodi sunamvepo? Zimenezi ndinazikhazikitsa kalekale. Ndinazikonzeratu masiku amakedzana; tsopano ndachita kuti zichitikedi, iwe kwako kunali kungosandutsa mizinda yotetezedwa kukhala milu ya miyala.
26 А ме́шканці їхні безсилі, настрашені та побенте́жені. Вони стали, як зілля оте польове́, мов трава зеленіюча, як трава на даха́х, як попа́лене збіжжя, яке не доспіло...
Anthu a kumeneko ndi opanda mphamvu, athedwa nzeru ndipo ali ndi manyazi. Ali ngati mbewu za mʼmunda, ngati udzu wanthete, ali ngati udzu womera pa denga, umene umawuma usanakule nʼkomwe.’”
27 І сидіння твоє, і твій вихід та вхід твій Я знаю, і твоє проти Мене обу́рення.
“‘Koma Ine ndimadziwa kukhala kwako, kutuluka kwako ndi kulowa kwako, ndi mkwiyo wako pa Ine.
28 За твоє проти Мене обу́рення, що горди́ня твоя надійшла до ушей Моїх, то на ні́здрі твої Я сережку привішу, а вуди́ло Моє — в твої у́ста, і тебе поверну́ Я тією дорогою, якою прийшов ти!
Chifukwa chakuti wandikwiyira ndipo ndamva za mwano wako, ndidzakola mphuno yako ndi mbedza ndi kuyika chitsulo changa mʼkamwa mwako, ndipo ndidzakubweza pokudzeretsa njira yomwe unadzera pobwera.’
29 А оце тобі знак: їжте цього року збіжжя самосі́йне, а другого року — саморо́сле, а третього року — сійте та жніть, і садіть виноградники, та й їжте їх плід.
“Koma iwe Hezekiya, chizindikiro chako chidzakhala ichi: “Chaka chino mudzadya tirigu wamphulumukwa, ndipo chaka chamawa mudzadya tirigu wongodzimerera. Koma chaka chachitatu mudzadzala ndi kukolola, mudzawoka mphesa ndipo mudzadya zipatso zake.
30 А врятоване Юдиного дому, що лишилося, пустить корі́ння додолу, і свого плода́ дасть уго́ру.
Anthu a nyumba ya Yuda amene adzatsale adzazika mizu ndi kubereka zipatso.
31 Бо з Єрусалиму вийде позоста́ле, а рештки — від гори Сіону. Ревність Господа Саваота зробить це!
Pakuti ku Yerusalemu kudzachokera anthu otsala, ndi ku phiri la Ziyoni kudzachokera gulu la anthu opulumuka.” “Changu cha Yehova Wamphamvuzonse chidzachita zimenezi.
32 Тому́ так сказав Господь про асирійського царя: Він не вві́йде до міста оцього, і туди він не кине стріли́, і щито́м її не попере́дить, і ва́ла на нього не ви́сипле!
“Choncho chimene Yehova akunena za mfumu ya ku Asiriya ndi ichi: “‘Iye sadzalowa mu mzinda umenewu kapena kuponyamo muvi. Sadzayandikira mzindawu ndi zishango zake kapena kumanga nthumbira ya nkhondo.
33 Якою дорогою при́йде, то нею пове́рнеться, у місто ж оце він не вві́йде, говорить Господь!
Adzabwerera potsata njira imene anadzera pobwera; sadzalowa mu mzinda umenewu, akutero Yehova.
34 І це місто Я обороню́ на спасі́ння його ради Себе та ради Давида, Мойого раба“!
Ndidzateteza mzinda umenewu kuwupulumutsa, chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha Davide mtumiki wanga.’”
35 І сталося тієї ночі, і вийшов Ангол Господній, і забив в асирійському табо́рі сто й вісімдеся́т і п'ять тисяч. І повставали вони рано вранці, аж ось — усі мертві тру́пи!
Usiku umenewo mngelo wa Yehova anapita ku misasa ya ku Asiriya ndi kupha ankhondo 185,000. Ndipo pamene anthu anadzuka mmawa, taonani, mitembo inali ngundangunda!
36 А Санхерів, асирійський цар, рушив та й пішов, і вернувся й осівся в Ніневі́ї.
Choncho Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anapasula misasa ndi kuchoka. Anabwerera ku Ninive nakakhala kumeneko.
37 І сталося, коли він молився в домі Нісроха, свого бога, то Адраммелех та Шар'ецер убили його мече́м, а самі втекли́ до кра́ю Арара́т. А замість нього зацарював син його Есар-Хаддон.
Tsiku lina, pamene Senakeribu ankapembedza mʼnyumba ya Nisiroki mulungu wake, ana ake Adirameleki ndi Sarezeri anamupha ndi lupanga ndipo anathawira ku dziko la Ararati. Tsono Esrahadoni, mwana wake, analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 царів 19 >