< 2 царів 17 >

1 Дванадцятого року Ахаза, Юдиного царя, зацарював над Ізраїлем у Самарії Осі́я, син Елин, на дев'ять років.
Mʼchaka cha 12 cha Ahazi mfumu ya Yuda, Hoseya mwana wa Ela anakhala mfumu ya Israeli mu Samariya ndipo analamulira zaka zisanu ndi zinayi.
2 І робив він зле в Господніх оча́х, тільки не так, як ті Ізраїлеві царі, що були перед ним.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, koma osafanana ndi mafumu a Israeli amene ankalamulira iye asanalowe ufumuwo.
3 На нього вийшов Салманасар, цар асирійський, і Осі́я став йому за раба́, і давав йому дани́ну.
Salimenezeri mfumu ya ku Asiriya anabwera kudzathira nkhondo Hoseya amene anali pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho kwa iyeyo.
4 Та асирійський цар знайшов в Осі́ї змову, що він посилав послів до Со, єгипетського царя, та не прино́сив асирійському цареві данини, як рік-у-рік те робив був. І замкнув його асирійський цар, і зв'язав його в в'язни́чому домі.
Koma mfumu ya ku Asiriya inazindikira kuti Hoseya akuwukira, pakuti Hoseyayo anali atatumiza nthumwi kwa So mfumu ya Igupto ndiponso analeka kukhoma msonkho kwa mfumu ya ku Asiriya, monga ankachitira chaka ndi chaka. Choncho Salimenezeri anagwira Hoseya ndi kumuyika mʼndende.
5 І вийшов асирійський цар на ввесь Край, і прийшов до Самарії, й обляга́в її три роки.
Mfumu ya ku Asiriya inapita kukathira nkhondo dziko lonse la Israeli ndipo inapita mpaka ku Samariya ndipo inazinga mzindawo kwa zaka zitatu.
6 Дев'ятого року Осі́ї асирійський цар здобув Самарію, та й вигнав Ізраїля до Асирії, і осадив їх у Халаху, і в Хаворі над річкою Ґозан, і в містах Мідії.
Mʼchaka chachisanu ndi chinayi cha Hoseya, mfumu ya ku Asiriya inalanda Samariya ndipo inatenga Aisraeli ndi kupita nawo ku Asiriya. Anakawakhazika ku Hala ndi Habori mʼmbali mwa mtsinje wa Gozani ndi mʼmizinda ya Amedi.
7 І сталося, коли Ізраїлеві сини грішили проти Господа, Бога свого, що ви́провадив їх з єгипетського кра́ю з руки фараона, єгипетського царя, і боя́лися інших богів,
Zonsezi zinachitika chifukwa Aisraeli anachimwira Yehova Mulungu wawo, amene anawatulutsa mʼdziko la Igupto pansi pa ulamuliro wa Farao mfumu ya Igupto. Iwo ankapembedza milungu ina,
8 і ходили уставами тих народів, що Госпо́дь повиганяв їх перед Ізраїлевими синами, та Ізраїлевих царів, які вони встановили,
ndiponso ankatsatira miyambo ya anthu a mitundu imene Yehova anayichotsa pamene iwo ankafika mʼdzikomo pamodzinso ndi miyambo yonse imene mafumu a Israeli anayambitsa.
9 а Ізраїлеві сини вимишляли на Господа, Бога свого, слова́, що не були слушні, і будували собі па́гірки по всіх своїх містах, від вартово́ї башти аж до тверди́нного міста,
Ndipo Aisraeli ankachita zoyipa mwamseri kutsutsana ndi Yehova Mulungu wawo. Kuchokera ku nsanja ya alonda mpaka ku mzinda wotetezedwa, mʼmizinda yawo yonse anamangamo malo opembedzeramo mafano.
10 і ставили собі стовпи для богів та Астарти на кожному високому взгі́р'ї та під усяким зеленим деревом,
Anayimika miyala ya chipembedzo ndi mitengo ya mafano a Asera pa phiri lililonse lalitali ndi pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
11 і кадили там на всіх па́гірках, як ті люди, що Господь повиганяв перед ними, і робили злі речі, щоб гніви́ти Господа,
Pa malo aliwonse opembedzera mafano, anthuwa ankafukiza lubani monga momwe ankachitira anthu a mitundu imene Yehova anayichotsa pamene iwo ankafika. Iwo anachita zinthu zoyipa zomwe zinaputa mkwiyo wa Yehova.
12 і служили бовва́нам, про яких Господь говорив їм: „Не бу́дете робити цієї речі“,
Ndipo iwowo ankapembedza mafano ngakhale Yehova ananena kuti, “Musadzachite zimenezi.”
13 то Господь засві́дчив в Ізраїлі та в Юді через усіх Своїх пророків та всіх прозорли́вців, говорячи: „Верніться з ваших злих доріг, і додержуйте Моїх заповідей, уставів Моїх, згідно зо всім Зако́ном, якого Я наказав був вашим батькам, і якого послав до вас через Моїх рабів пророків“.
Yehova anachenjeza Israeli ndi Yuda kudzera mwa aneneri ake onse ndi alosi kuti, “Lekani mchitidwe wanu woyipawo. Mverani malamulo anga ndi malangizo anga potsatira zonse zolembedwa mʼmalamulo a Mose, zimene ndinalamulira makolo anu kuti azimvere, kudzera mwa aneneri, atumiki anga.”
14 Та не слухали вони, і робили твердо́ю свою шию, як шия їхніх батькі́в, що не вірили в Господа, Бога свого.
Koma anthuwa sanamvere ndipo anawumitsa khosi ngati momwe analili makolo awo, amene sanadalire Yehova Mulungu wawo.
15 І не́хтували вони постанови Його, і заповіта Його, що склав з їхніми батька́ми, і свідо́цтва Його, що засві́дчив на них, і пішли за гидо́тою й марно́тами, та за наро́дами, що були навколо них, про яких Господь наказав був їм не робити, як вони.
Anakana malangizo ake ndi pangano anachita ndi makolo awo ndipo ananyoza zochenjeza za Yehova. Iwo anatsatira mafano achabechabe nasanduka achabechabe. Anthuwa anatsanzira mitundu ya anthu owazungulira ngakhale kuti Yehova anawalamula kuti, “Musamachite zomwe iwo amachita,” koma iwo anachita zomwe Yehova anawaletsa.
16 І полишили вони всі заповіді Господа, Бога свого, і зробили собі литого бовва́на, двох телят, і зробили Астарту, і вклонялися всьому небесному ві́йськові та служили Ваалові.
Iwowo anasiya malamulo onse a Yehova Mulungu wawo, nadzipangira mafano awiri osungunula a ana angʼombe ndiponso fano la Asera, napembedza zonse zamlengalenga ndi kutumikira Baala.
17 І вони перево́дили через огонь своїх синів та дочо́к своїх, і чарува́ли ча́рами, і ворожили, і віддавалися робити зло в Господніх оча́х, щоб гнівити Його.
Ndipo anadutsitsa mʼmoto ana awo aamuna ndi aakazi. Iwo ankawombeza mawula, namachitanso zanyanga ndipo anadzipereka kuchita zoyipa pamaso pa Yehova namukwiyitsa.
18 І сильно розгнівався Господь на Ізраїля, і відкинув їх від Свого лиця, — не позостало ніко́го, тільки саме Юдине пле́м'я.
Choncho Yehova anakwiya nawo kwambiri Aisraeli ndipo anawachotsa pamaso pake. Palibe amene anatsala kupatula fuko la Yuda lokha.
19 Та й Юда не додержував заповідей Господа, Бога свого, — і ходили вони Ізраїлевими постановами, які вони встанови́ли.
Yuda nayenso sanasunge malamulo a Yehova Mulungu wawo. Iwo ankatsatira machitidwe amene Israeli anayambitsa.
20 І відвернувся Господь від усього Ізраїлевого насіння, і впокоря́в їх, і давав їх у руку грабі́жників, аж поки не кинув їх від лиця Свого,
Motero Yehova anakana Aisraeli onse. Iye anawazunza nawapereka mʼmanja mwa anthu ofunkha mpaka Iye atawachotseratu pamaso pake.
21 бо Ізраїль розірвав з Давидовим домом, і вони зробили царем Єровоама, Неватового сина, а Єровоам відвернув Ізраїля від Господа, і вводив їх у великий гріх.
Yehova atangʼamba Israeli kumuchotsa ku nyumba ya Davide, Aisraeliwo anasankha Yeroboamu mwana wa Nebati kukhala mfumu yawo. Yeroboamu ananyengerera Aisraeli kuti asatsatire Yehova ndipo anawachimwitsa tchimo lalikulu.
22 І ходили Ізраїлеві сини в усіх Єровоамових гріхах, які він робив, не відсту́палися з того,
Aisraeli anakakamira machimo onse amene Yeroboamu anachita ndipo sanawasiye
23 аж поки Господь не відкинув Ізраїля від лиця Свого, як говорив був через усіх Своїх рабів пророків. І пішов Ізраїль на вигна́ння з своєї землі до Асирії, і він там аж до цього дня.
mpaka pamene Yehova anawachotsa pamaso pake monga anawachenjezera kudzera mwa atumiki ake onse, aneneri. Choncho Aisraeli anachotsedwa mʼdziko lawo kupita ku ukapolo ku Asiriya ndipo ali komweko mpaka lero lino.
24 І спрова́див асирійський цар людей з Вавилону, і з Кути, і з Авви, і з Гамоту, і з Сефарваїму, й осели́в по містах Самарії замість Ізраїлевих синів. І посіли вони Самарію, й осілися по містах її.
Mfumu ya ku Asiriya inabweretsa anthu a ku Babuloni, Kuta, Awa, Hamati ndi a ku Sefaravaimu kudzawakhazika mʼmizinda ya Samariya kulowa mʼmalo mwa Aisraeli. Iwo anatenga Samariya ndi kukhala mʼmizinda yake.
25 І сталося, на поча́тку пробува́ння їх там не боялися вони Господа, — і Господь послав на них левів, і вони нищили їх.
Iwo atayamba kukhala kumeneko, sanapembedze Yehova choncho Yehova anatumiza mikango pakati pawo ndipo inapha ena mwa iwo.
26 І сказали вони до асирійського царя, говорячи: „Ті люди, яких ти вигнав та осели́в по містах Самарії, не знають прав Бога цього Кра́ю, і Він послав на них оцих левів, і ось вони нищать їх, бо вони не знають права Бога цього Кра́ю“.
Tsono mfumu ya ku Asiriya inawuzidwa za nkhaniyi kuti, “Anthu amene munawatumiza ndi kuwakhazika mʼmizinda ya Samariya sakudziwa chimene Mulungu wa dzikolo amafuna. Choncho Iye watumiza mikango pakati pawo imene ikuwapha chifukwa anthuwo sadziwa chimene Mulungu wa dzikolo amafuna.”
27 І наказав асирійський цар, говорячи: „Відведіть туди одно́го зо священиків, яких вигнали звідти, і пі́дуть, і осядуть там, і він навчатиме їх пра́ва Бога цього кра́ю“.
Tsono mfumu ya ku Asiriya inalamula kuti, “Tengani wansembe mmodzi mwa amene munawagwira ukapolo, mupite naye kumeneko ndipo akakhale komweko nakaphunzitse anthu zimene Mulungu wa dzikolo amafuna.”
28 І прибув один із священиків, яких вигнали з Самарії, й осівся в Бет-Елі, і він навчав їх, як мають боятися Господа.
Choncho mmodzi mwa ansembe amene anawatenga ku Samariya anabwera kudzakhala ku Beteli ndipo ankaphunzitsa anthuwo kupembedza Yehova.
29 Та крім того кожен народ робив свого бога, і ставили їх у па́гірковому місці, що робили попередні самаряни, кожен народ по своїх містах, де вони сиділи.
Koma mtundu uliwonse wa anthu unkapangabe mafano a milungu yawoyawo mʼmizinda yambiri imene anthuwo ankakhala, ndipo anayika milunguyo mʼnyumba za milungu zimene anthu a ku Samariya anamanga ku malo opembedzera mafano.
30 А вавилоняни зробили Суккот-Бенота, а кутяни зробили Нереґала, а гаматяни зробили Ашіму,
Anthu a ku Babuloni anapanga Sukoti-Benoti, anthu a ku Kuti anapanga Nerigali, ndipo anthu a ku Hamati anapanga Asima;
31 а авв'яни зробили Нівхаза та Тартака, а ме́шканці Сефарваїму палили синів своїх ув огні Адраммелехові й Анаммелехові, сефарваїмським богам.
Aava anapanga Nibihazi ndi Taritaki, ndipo Asefaravaimu ankawotcha ana awo pa moto ngati nsembe kwa Adirameleki ndi Anameleki, milungu ya Asefaravaimu.
32 І при тому вони боялися Господа, і настанови́ли собі з-серед себе священиків па́гірків, і вони прино́сили їм жертви в пагірковому місці.
Iwo ankapembedza Yehova, koma ankadzisankhira okha pakati pawo anthu wamba kuti akhale ansembe awo ku nyumba za milungu za ku malo opembedzera mafano.
33 Вони боялися Господа, і богам своїм служили за правом тих народів, звідки повиганя́ли їх.
Iwowo ankapembedza Yehova, komanso ankatumikira milungu yawo molingana ndi miyambo ya mitundu ya kumene ankachokera.
34 Аж до цього дня вони роблять за колишнім правом, — вони не бояться Господа, і не роблять за уставами своїми та за правом своїм, ані за Зако́ном, ані за заповіддю, як наказав був Господь синам Якова, якому дав ім'я́ Ізраїля.
Mpaka lero lino iwo akupitirizabe kuchita zimene ankachita poyamba. Sapembedza Yehova kapenanso kutsata malangizo ake ndi malamulo ake, chiphunzitso chake monga mwa malamulo amene Yehova anawapereka kwa zidzukulu za Yakobo, amene anamutcha Israeli.
35 І склав Господь із ними заповіта, і наказав їм, говорячи: „Не будете боятися інших богів, і не будете вклонятися їм, і не будете служити їм, і не будете прино́сити жертов їм,
Pamene Yehova anachita pangano ndi Aisraeli, Iye anawalamula kuti, “Musapembedze milungu ina kapena kuyigwadira iyo, kuyitumikira kapena kupereka nsembe kwa iyoyo.
36 а тільки Господа, що вивів вас із єгипетського кра́ю великою силою та ви́тягненим раме́ном, Його будете боятися, і Йому будете вклонятися, і Йому будете прино́сити жертви.
Koma Yehova amene anakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi dzanja lake lamphamvu ndiye amene muyenera kumupembedza.
37 І устави, і права́, і Зако́на, і заповідь, які написав вам, бу́дете доде́ржувати, щоб вико́нувати по всі дні, а богів інших не будете боятися.
Muyenera kusamalitsa nthawi zonse kusunga malangizo anga ndi malemba anga, chiphunzitso ndi malamulo amene anakulemberani. Musapembedze milungu ina.
38 А заповіта, що Я склав із вами, не забудете, і не будете боятися інших богів,
Musayiwale pangano limene ndinapangana nanu ndipo musamapembedze milungu ina.
39 а тільки Господа, Бога вашого, будете боятися, і Він вирятує вас із руки всіх ваших ворогів“.
Mʼmalo mwake muzipembedza Yehova Mulungu wanu pakuti ndiye amene adzakulanditsani mʼdzanja la adani anu onse.”
40 Та не послухали вони, бо все робили за своїм попереднім зви́чаєм.
Komabe iwo sanamvere ndipo anapitiriza kuchita zomwe ankachita kale.
41 І ті народи все боялися Господа, але служили бовва́нам своїм. Так само сини їхні та сини їхніх синів, — як робили батьки їхні, так роблять вони аж до цього дня.
Ngakhale anthuwo ankapembedza Yehova, ankatumikiranso mafano awo. Mpaka lero lino ana awo ndi zidzukulu zawo zikupitiriza kuchita zomwe ankachita makolo awo.

< 2 царів 17 >