< 2 хроніки 25 >
1 У віці двадцяти й п'яти літ зацарював Амація, і двадцять і п'ять літ царював він в Єрусалимі. А ім'я́ його матері — Єгоаддан, з Єрусалиму.
Amaziya anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 29. Dzina la amayi ake linali Yehoyadini wa ku Yerusalemu.
2 І робив він угодне в Господніх оча́х, тільки не з ці́лим серцем.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, koma osati ndi mtima wonse.
3 І сталося, як зміцнилося царство за ним, то він повбивав своїх рабів, що забили царя свого, його батька.
Pamene mphamvu zonse zaufumu zinali mʼmanja mwake, iye anapha akuluakulu amene anapha abambo ake, mfumu ija.
4 А синів їх він не позабивав, як написано в книзі Мойсеєвого Зако́ну, що наказав був Господь, говорячи: „Не помруть батьки за синів, а сини не помруть за батьків, бо кожен за гріх свій помре́“.
Komabe iye sanaphe ana awo koma anatsatira zolembedwa mʼbuku la Mose, mʼmene Yehova analamula kuti, “Makolo sadzaphedwa chifukwa cha ana awo kapena ana kuphedwa chifukwa cha makolo awo. Aliyense adzafera machimo ake.”
5 І зібрав Амація Юду, і поставив їх за домом їхніх батькі́в, за тисячниками та за сотниками для всього Юди та Веніямина; і він перелічив їх від віку двадцяти́ років і вище, і знайшов їх три сотні тисяч ви́браного, здатного до війська, хто тримає ра́тище та великого щита́.
Amaziya anasonkhanitsa anthu a ku Yuda ndipo anawapatsa zochita molingana ndi mabanja awo kukhala anthu olamulira 1,000, ndi olamulira 100 pa Ayuda onse ndi Benjamini. Ndipo iye anawerenga amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo napeza kuti analipo amuna 300,000 okonzeka kugwira ntchito ya usilikali, okhoza kugwiritsa ntchito mkondo ndi chishango.
6 І найняв він із Ізраїля сотню тисяч хоробрих воякі́в за сотню талантів срібла.
Iye analembanso ntchito anthu odziwa nkhondo 100,000 ochokera ku Israeli pa mtengo wa makilogalamu 3,400 a siliva.
7 І прийшов до нього Божий чоловік, говорячи: „О ца́рю, нехай не вихо́дить з тобою Ізраїлеве ві́йсько, бо Господь не з Ізраїлем, ні з жодним із синів Єфрема.
Koma munthu wa Mulungu anabwera kwa iye ndipo anati, “Inu mfumu, asilikali awa ochokera ku Israeli asapite ndi inu, pakuti Yehova sali ndi Israeli kapena ndi aliyense wa anthu a Efereimu.
8 Але йди тільки ти, роби, будь відважний на війні! Інакше вчи́нить Бог, що ти спіткне́шся перед ворогом, бо в Бога є сила допомагати, або робити, щоб спіткну́тися“.
Ngakhale mupite ndi kuchita nkhondo molimba mtima, Mulungu adzakugonjetsani pamaso pa adani anu, pakuti Mulungu ali ndi mphamvu yothandiza kapena kugonjetsa.”
9 І сказав Амація до Божого чоловіка: „А що́ робити з тією сотнею талантів, що я дав Ізраїлевому ві́йську?“А Божий чоловік відказав: „Господь може дати тобі більше від цьо́го!“
Amaziya anafunsa munthu wa Mulungu kuti, “Koma nanga za makilogalamu aja a siliva amene ndapereka kwa asilikali a Israeli?” Munthu wa Mulungu anayankha kuti, “Yehova atha kukupatsani zambiri kuposa zimenezo.”
10 І відділив Амація їх, те ві́йсько, що прийшло з краю Єфремового, щоб ішло на своє місце. І дуже запали́вся їхній гнів на Юду, і вони вернулися на своє місце в запа́леному гніві.
Choncho Amaziya anachotsa asilikali amene anabwera kwa iye kuchokera ku Efereimu ndipo anawatumiza kwawo. Iwo anakwiyira anthu a ku Yuda ndipo anapita kwawo atapsa mtima kwambiri.
11 А Амація зміцни́вся, і попровадив свій наро́д, і пішов до Соляної долини, і побив десять тисяч Сеїрових синів,
Ndipo Amaziya analimba mtima ndipo anatsogolera gulu lake lankhondo ku Chigwa cha Mchere, kumene anapha anthu 10,000 a ku Seiri.
12 а десять тисяч живих узяли́ Юдині сини до неволі. І привели́ їх на верхі́в'я скелі, і поскида́ли їх з верхі́в'я тієї скелі, — і всі вони позабивалися.
Gulu la ankhondo la Yuda linagwiranso anthu amoyo 10,000, napita nawo pamwamba pa thanthwe ndipo anawaponya pansi kotero kuti onse ananyenyeka.
13 А люди того ві́йська, що Амація вернув, щоб не йшли з ним на війну, розси́палися по Юдиних містах від Самарії й аж до Бет-Хорону, і повбива́ли з них три тисячі, і пограбували велику здо́бич.
Pa nthawi imeneyi asilikali amene Amaziya anawabweza ndipo sanawalole kuti achite nawo nkhondo, anakathira nkhondo mizinda ya Yuda kuyambira ku Samariya mpaka ku Beti-Horoni. Iwo anapha anthu 3,000 ndipo anafunkha katundu wambiri.
14 І сталося по то́му, як прийшов Амація, побивши едо́млян, то він приніс богів Сеїрових синів, і поставив їх собі за богів, і перед ними вклоня́вся, і їм кадив.
Amaziya atabwerera kuja anakapha Aedomu, anabweretsa milungu ya anthu a ku Seiri. Ndipo anayika kuti ikhale milungu yake, ankayipembedza ndi kupereka nsembe zopsereza.
15 І запали́вся Господній гнів на Амацію, і Він послав до нього пророка, а той сказав йому́: „На́що ти звертався до богі́в цього народу, богів, що не врятували народу свого від твоєї руки?“
Yehova anakwiyira Amaziya, ndipo anamutumizira mneneri amene anati, “Nʼchifukwa chiyani mukupembedza milungu ya anthu awa, imene sinathe kupulumutsa anthu ake mʼdzanja lanu?”
16 І сталося, як він говорив це до нього, сказав йому цар: „Чи я поставив тебе за царевого дора́дника? Перестань собі, нащо вбивати тебе?“І перестав той пророк, але сказав: „Я знаю, що Бог постановив погубити тебе, бо зробив ти це, і не слухав моєї поради“.
Iye ali kuyankhula, mfumu inati, “Kodi ife takusankha iwe kuti ukhale mlangizi wa mfumu? Khala chete! Ufuna kuphedweranji?” Choncho mneneriyo analeka koma anati, “Ine ndikudziwa kuti Mulungu watsimikiza kukuwonongani chifukwa mwachita izi ndipo simunamvere uphungu wanga.”
17 І радився Амація, цар Юдин, і послав до Йоаша, сина Єгоахаза, сина Єгу, Ізраїлевого царя, говорячи: „Іди но, поміряємось!“
Amaziya mfumu ya ku Yuda, atafunsa alangizi ake, anatumiza mawu awa kwa Yowasi mwana wa Yehowahazi mwana wa Yehu, mfumu ya Israeli: “Bwera udzakumane nane maso ndi maso.”
18 І послав Йоаш, Ізраїлів цар, до Амації, Юдиного царя, говорячи: „Терни́на, що на Лива́ні, послала до кедри́ни, що на Ливані, кажучи: Дай но дочку́ свою́ моєму синові за жінку! Та перейшла польова́ звірина́, що на Ливані, і витоптала ту терни́ну.
Koma Yowasi mfumu ya Israeli inayankha Amaziya mfumu ya Yuda kuti, “Nthawi ina kamtengo kaminga ka ku Lebanoni kanatumiza mawu kwa mkungudza wa ku Lebanoni kuti, ‘Pereka mwana wako wamkazi kwa mwana wanga kuti amukwatire!’ Koma chirombo cha ku Lebanoni chinabwera ndi kupondaponda mtengo wa minga uja.
19 Ти сказав: Ось побив ти Едома, і підне́сло тебе серце твоє, щоб пиша́тися. Тепер сиди ж у своєму домі. На́що будеш дрочи́тися зо злом, і впадеш ти та Юда з тобою?“
Iwe ukuti wagonjetsa Edomu, ndipo tsopano ukudzikuza ndi kudzitamandira, koma khala kwanu komweko! Nʼchifukwa chiyani ukufuna mavuto ndi kudzichititsa kuti ugwe pamodzinso ndi Yuda?”
20 Та не послухався Амація, бо від Бога було це, щоб віддати їх у руку ворога, бо зверта́лися вони до едо́мських богів.
Komabe Amaziya sanamvere pakuti ndi Mulungu amene anakonzeratu kuti awapereke kwa Yehowasi, chifukwa iwo amapembedza milungu ya ku Edomu.
21 І вийшов Йоаш, Ізраїлів цар, і зустрі́лися він та Амація, цар Юдин, у Юдиному Бет-Шемеші.
Kotero Yowasi mfumu ya Israeli inakamuthira nkhondo. Iye ndi Amaziya anayangʼanana maso ndi maso ku Beti-Semesi ku Yuda.
22 І був побитий Юда перед Ізраїлем, і повтікали кожен до намету свого́.
Yuda anagonjetsedwa ndi Israeli ndipo munthu aliyense anathawira kwawo.
23 А Йоаш, цар Ізраїлів, схопи́в Амацію, Юдиного царя, сина Йоаша, сина Єгоахаза, у Бет-Шемеші, і привів його до Єрусалиму, і зробив пролі́м в єрусалиському мурі, від Єфремової брами аж до брами Нарі́жної, чотири сотні ліктів.
Yehowahazi mfumu ya Israeli inagwira Amaziya mfumu ya Yuda, mwana wa Yowasi, mwana wa Ahaziya ku Beti-Semesi. Yehowasi anabwera naye ku Yerusalemu ndipo anagwetsa khoma la Yerusalemu kuyambira pa Chipata cha Efereimu mpaka ku Chipata Chapangodya, khoma lotalika mamita 180.
24 І забрав він усе золото й срібло, та ввесь по́суд, що знахо́дився в Божому домі в Овед-Едома, та ска́рби царевого дому, та закла́дників, і вернувся в Самарію.
Iye anatenga golide ndi siliva yense ndi zida zonse zimene zimapezeka mʼNyumba ya Mulungu zimene ankazisamalira Obedi-Edomu, pamodzinso ndi chuma cha mʼnyumba yaufumu ndipo anatenga anthu ngati chikole.
25 І жив Амація, Йоашів син, цар Юдин, по смерті Йоаша, Єгоахазового сина, Ізраїлевого царя, п'ятнадцять літ.
Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anakhala ndi moyo kwa zaka khumi ndi zisanu atamwalira Yehowasi mwana wa Yehowahazi mfumu ya Israeli.
26 А решта діл Амації, перші та останні, ото вони написані в Книзі Царів Юдиних та Ізраїлевих.
Ntchito zina za mfumu Amaziya, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli?
27 А від ча́су, коли Амація відступив від Господа, то склали на нього змову в Єрусалимі, та він утік до Лахішу. І послали за ним до Лахішу, — і вбили його там.
Kuyambira nthawi imene Amaziya analeka kutsatira Yehova anthu anamukonzera chiwembu mu Yerusalemu ndipo anathawira ku Lakisi, koma adaniwo anatumiza anthu ku Lakisiko ndipo anamupha komweko.
28 І пове́зли його на ко́нях, і поховали його з батька́ми його в Давидовому Місті.
Iwo anabwera naye ali pa kavalo ndipo anayikidwa mʼmanda ndi makolo ake mu mzinda wa Yuda.