< 1 Самуїлова 2 >
1 І молилася Анна та й проказала: „Звесели́лося Господом серце моє, мій ріг став високим у Го́споді! Розкри́лися у́ста мої на моїх ворогів, бо радію з спасіння Твого́!
Ndipo Hana anapemphera nati, “Moyo wanga ukukondwera mwa Yehova; Ndiyenda mwa tukumutukumu chifukwa cha Yehova. Pakamwa panga pakula ndi kuseka adani anga mowanyogodola. Ndikukondwa chifukwa mwandipulumutsa.
2 Немає святого, подібного Господу, немає ніко́го, крім Те́бе, і скелі немає, як Бог наш!
“Palibe wina woyera ngati Yehova, palibe wina koma inu nokha, palibe thanthwe lofanana ndi Mulungu wathu.
3 Більше не говоріть зарозумі́ло, нехай з ваших уст не виходить зухва́льство, бо Господь — Бог знання́, і Він упляно́вує вчинки!
“Musandiyankhulenso modzitama, pakamwa panu pasatuluke zonyada, pakuti Yehova ndi Mulungu wanzeru, ndipo ndiye amene amayesa ntchito za anthu onse.
4 Лук сильних пола́маний, а немічні опереза́лися силою!
“Mauta a anthu ankhondo athyoka koma anthu ofowoka avala dzilimbe.
5 Наймаються ситі за хліб, а голодні відпочивають, аж неплідна сімо́х породила, а многодітна — знеси́ліла.
Amene kale anali okhuta tsopano akukagula chakudya, koma iwo amene anali ndi njala sakumvanso njala. Amene anali wosabereka, wabereka ana aamuna asanu ndi awiri, koma iye wobereka ana ambiri watsala yekha.
6 Госпо́дь побиває й оживлює, до шео́лу знижає й підно́сить до неба. (Sheol )
“Yehova amabweretsa imfa ndipo amaperekanso moyo, amatsitsira ku manda ndipo amawatulutsakonso. (Sheol )
7 Господь зубо́жує та збагачує, понижує Він та звели́чує.
Yehova amasaukitsa ndipo amalemeretsa, amatsitsa ndipo amakweza.
8 Підіймає нужде́нного з по́роху, підно́сить убогого зо смітникі́в, щоб посадити з вельмо́жами й престол слави їм дать на спа́дщину, бо Госпо́дні основи землі, і на них Він поставив вселе́нну.
Iye amakweza osauka kuwachotsa pa fumbi, ndipo amachotsa anthu osowa pa dzala. Iye amawakhazika pamodzi ndi ana a mafumu, amawapatsa mpando waulemu. “Pakuti nsanamira za dziko lapansi ndi za Yehova, anakhazika dziko lapansi pa nsanamirazo.
9 Він ноги святих Своїх стереже, нечестиві ж погинуть у те́мряві, бо сильним не з сили стає чоловік.
Iye adzateteza moyo wa anthu okhulupirika koma anthu oyipa adzawonongedwa mu mdima. “Pakuti munthu sapambana ndi mphamvu zake.
10 Господь — хай поламані будуть Його супроти́вники! У небі Господь загримить, і розсудить Він кі́нці землі! І Він подасть силу Своєму царе́ві, і рога повищить Свого помаза́нця!“
Yehova adzaphwanya omutsutsa. Adzawaopsa ndi bingu kuchokera kumwamba; Yehova adzaweruza mathero a dziko lapansi. “Koma adzapereka mphamvu kwa mfumu yake, adzakuza mphamvu za odzozedwa wake.”
11 І пішов Елкана до Рами, до дому свого. А той отрок служив Господе́ві при священикові Ілі́ї.
Tsono Elikana anapita ku mudzi kwawo ku Rama, koma mnyamatayo amatumikira Yehova pansi pa ulamuliro wa wansembe Eli.
12 А сини Ілі́я були люди негідні, — вони не знали Господа,
Ana a Eli anali ana achabechabe pakuti samasamala za Yehova.
13 ані зви́чаю священичого з народом. Коли хто прино́сив жертву, то, як варилося м'ясо, прихо́див священиків слуга, а в його руці — тризубе виде́льце.
Ndipo chizolowezi cha ansembe pakati pa anthu chinali motere kuti pamene munthu aliyense ankapereka nsembe ndipo nyama ija ikuwira pa moto, mtumiki wa wansembe ankabwera ndi chifoloko cha mano atatu mʼdzanja lake.
14 І він із грюкотом стромляв до мідниці, або до кітла, або до горшка, або до горня́ти, — і все, що витягне видельце, священик собі брав. Так вони робили всьому Ізраїлеві, що прихо́див туди до Шіло́.
Iye ankachipisa mu mʼphikamo, ndipo wansembeyo amatenga chilichonse chimene folokoyo yabaya. Umu ndi mmene ansembewo amachitira ndi Aisraeli onse amene amabwera ku Silo.
15 Також поки пали́ли лій, то прихо́див священиків слуга, та й говорив до чоловіка, що приносив жертву: „Дай м'яса на печеню для священика, бо він не ві́зьме від тебе м'яса варе́ного, а тільки сире!“
Ndipo ngakhale mafuta asanatenthedwe, mtumiki wansembe amabwera ndi kunena kwa munthu amene akupereka nsembeyo kuti, “Ndipatse nyama kuti ndiwotche, pakuti Yehova salandira nyama yophika koma yayiwisi.”
16 А як той чоловік відповідав йому: „Нехай перше спалять і той лій, а ти потім візьми собі, скільки буде жадати душа твоя!“А той говорив: „Ні, таки зараз давай! А коли ні, візьму́ силою!“
Ngati munthuyo anena kuti, “Apseretu mafuta poyamba, ndipo kenaka mutenge mmene mufunira,” mtumikiyo amayankha kuti, “Ayi ndipatse tsopano lino. Ngati sutero, ine nditenga molanda.”
17 І був гріх тих юнакі́в дуже великий перед Господнім лицем, бо ті люди безче́стили Господню жертву
Tchimo la ana a Eli linali lalikulu kwambiri pamaso pa Yehova pakuti iwo amanyoza nsembe za Yehova.
18 А Самуїл служив перед Господнім лицем. Отрок був оперезаний лляни́м ефо́дом.
Koma Samueli amatumikira pamaso pa Yehova atavala efodi ya nsalu yofewa yosalala.
19 А малу верхню одежину робила йому його мати, і прино́сила йому з року на рік, коли прихо́дила з своїм мужем прино́сити річну жертву.
Chaka chilichonse amayi ake ankamusokera kamkanjo ndi kukamupatsa akamapita ndi mwamuna wake kukapereka nsembe za pa chaka.
20 А Ілій поблагословив Елкану й його жінку та й сказав: „Нехай Господь дасть тобі наща́дків від цієї жінки, за ві́дданого, що Господь узяв“. І пішли вони на місце своє.
Tsono Eli amadalitsa Elikana ndi mkazi wake ndi mawu akuti “Yehova akupatseni ana mwa mkazi uyu kulowa mʼmalo mwa amene anapempha ndi kumupereka kwa Yehova.”
21 І Господь згадав про Анну, і вона завагітні́ла, та й породила трьох синів та дві до́чки. А о́трок Самуїл ріс із Господом.
Ndipo Yehova anamukomera mtima Hana. Anakhala ndi pathupi ndi kubereka ana aamuna atatu ndi ana aakazi awiri. Ndipo Samueli ankakula pamaso pa Yehova.
22 А Ілі́й був дуже стари́й. І почув він усе, що́ сини його роблять усьому Ізраїлеві, і що вони злягаються з жінками, які відбувають службу при вході скинії заповіту.
Tsono Eli anakalamba kwambiri. Iye ankamva zonse zimene ana ake aamuna ankachitira Aisraeli onse, ndiponso kuti ankagona ndi akazi pa chipata cha tenti ya msonkhano.
23 І він сказав їм: „Нащо ви робите такі речі, про які я чую? Про ваші злі вчинки я чую від усього цього народу.
Choncho anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukuchita zinthu zotere? Ine ndikumva kuchokera kwa anthu onse za zoyipa zanuzo.
24 Ні, сини мої, — недобра та чутка, що я чую, — ви відхиляєте Господній наро́д від Закону!
Ayi, ana anga si mbiri yabwino imene ndikumva anthu a Mulungu akufalitsa.
25 Якщо хто згрішить супроти люди́ни, то помо́ляться за неї перед Богом. А якщо люди́на згрішить супроти Господа, — хто заступиться за неї?“Та вони не слухали голосу батька свого, бо Господь постановив погубити їх.
Ngati munthu alakwira munthu mnzake, mwina Mulungu adzamupepesera, koma ngati munthu achimwira Yehova adzamupepesera ndani?” Koma ana ake sanamvere kudzudzula kwa abambo awo, pakuti chinali cholinga cha Yehova kuti awaphe.
26 А о́трок Самуїл усе ріс, та здобува́в ла́ску як у Господа, так і в людей.
Ndipo mnyamata Samueli anapitirira kukula mu msinkhu, ndipo ankapeza kuyanja pamaso pa Yehova ndi anthu.
27 І прийшов Божий чоловік до Ілія, та й сказав йому: „Так сказав Господь: Чи ж Я справді не об'явився до́мові твого батька, як були вони в Єгипті, у фараоновім домі?
Tsiku lina munthu wa Mulungu anabwera kwa Eli ndipo anamuwuza kuti, “Yehova akuti, ‘Kodi Ine sindinadziwulule ndekha kwa banja la kholo lako pamene iwo anali akapolo a Farao ku Igupto?
28 Я вибрав його Собі зо всіх Ізраїлевих племен за священика, щоб він входив до Мого жертівника, щоб кадив кадило, щоб носив ефо́да перед Моїм лицем. І дав Я до́мові твого батька всі жертви Ізраїлевих синів.
Ndipo ndinamusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti akhale wansembe wanga ndi kuti azipita pa guwa langa la nsembe, kufukiza Lubani ndi kuvala efodi pamaso panga. Ndinapatsa banja la abambo ako gawo la nsembe zonse zopsereza zimene Aisraeli amapereka.
29 Чого ж ви бере́те під ноги Мою жертву та Мою жертву хлібну, що Я заповів для скинії? І ти вшанував синів своїх більш, як Мене, щоб ви потовстіли від найкращих частин усякого Ізраїлевого да́ру перед лицем Моїм.
Nʼchifukwa chiyani ukunyoza nsembe ndi zopereka zanga zimene ndinalamula? Nʼchifukwa chiyani ukupereka ulemu kwa ana ako kuposa Ine podzinenepetsa nokha ndi zopereka zabwino kwambiri za nsembe zimene Aisraeli amapereka?’”
30 Тому́ то слово Господа, Бога Ізраїлевого, таке: Говорячи, сказав Я: Дім твій та дім батька твого будуть ходити перед Моїм лицем аж навіки. А тепер слово Господнє: Не буде в Мене такого, бо Я шаную тих, хто шанує Мене, а ті, хто зневажає Мене, будуть знева́жені!
“Paja Ine Yehova Mulungu wa Israeli ‘Ndinalonjeza kuti anthu a pa banja lako ndi a pa banja la abambo ako azidzanditumikira nthawi zonse.’ Koma tsopano ndikuti, ‘Zonsezi zithe!’ Tsopano anthu amene amandilemekeza Inenso ndidzawalemekeza koma iwo amene amandinyoza Ine ndidzawanyoza.
31 Ось приходять дні, і Я відітну́ раме́но твоє та раме́но дому батька твого, щоб не було старо́го в домі твоєму.
Nthawi ikubwera imene ndidzachotsa anyamata ako ndi anyamata a pa banja la abambo ako, kotero kuti sipadzakhala munthu wokalamba pa banja lako.
32 І побачиш біду Мого ме́шкання, хоч у всьому Я добре чинив Ізра́їлеві, і не буде старого в домі твоїм по всі дні.
Pa mavuto ako udzayangʼana ndi maso ansanje zabwino zimene ndidzachitira Aisraeli ena. Mʼbanja lako simudzapezeka munthu wokalamba.
33 Я не витну в тебе всіх від Мого жертівника, щоб вибрати очі твої, і щоб зробити біль душі твоїй, — та ввесь до́ріст твого дому повмирає в силі віку.
Komabe pa banja lako mmodzi yekha ndidzamuleka wosamuchotsa kuti azidzanditumikira. Iyeyu azidzakuliritsa ndi kukumvetsa chisoni. Koma ena onse pa banja lako adzafa akanali aangʼono.”
34 А оце тобі озна́ка, що при́йде на обох синів твоїх, на Хофні та Пінхаса, — оби́два вони помруть одно́го дня.
“‘Ndipo chimene chidzachitike kwa ana ako awiriwa, Hofini ndi Finehasi, chidzakhala chizindikiro kwa iwe. Onse awiri adzafa pa tsiku limodzi.
35 А Я поставлю Собі священика вірного, — він буде робити згідно з серцем Моїм та з Моєю душею. І Я збудую йому тривалий дім, і він буде ходити перед Моїм пома́занцем по всі дні.
Pambuyo pake ndidzasankha wansembe wokhulupirika, amene adzachita zimene zili mu mtima ndi mʼmaganizo mwanga. Ndidzakhazikitsa banja lako kolimba ndipo adzatumikira pamaso pa wodzozedwa wanga nthawi zonse.
36 І станеться, — кожен, хто полишиться в домі твоїм, при́йде вклонятися йому за аґору срібла та за бухане́ць хліба, і скаже: Долучи мене до одного з священицтв, щоб їсти кавалок хліба“.
Ndipo aliyense wotsala wa banja lako adzabwera ndi kugwada pamaso pake kupempha ndalama kapena chakudya.’ Adzati, ‘Chonde ndiloleni kuti ndizithandizako pa ntchito iliyonse ya unsembe kuti ndipeze chakudya.’”