< 1 хроніки 13 >
1 І ра́дився Давид із тисячниками та з сотниками, зо всіма́ значни́ми.
Davide anakambirana ndi akuluakulu ake, atsogoleri a anthu 1,000 ndi atsogoleri a anthu 100.
2 І сказав Давид до всієї Ізраїлевої грома́ди: „Якщо вам це добре, а від Господа, Бога нашого вподо́бане, пошлі́мо до наших братів, позосталих по всіх Ізраїлевих края́х, а з ними до священиків та Левитів, по містах та по їхніх пасовиськах, і нехай зберу́ться до нас.
Ndipo anati kwa gulu lonse la Israeli, “Ngati kukukomerani komanso ngati chili chifuniro cha Yehova Mulungu wathu, tiyeni titumize uthenga kulikonse kumene kuli abale athu ena onse ku dziko lonse la Israeli ndiponso kwa ansembe ndi Alevi amene ali nawo mʼmidzi yawo ndi madera odyetsera ziweto, kuti abwere adzakhale nafe.
3 І вернімо ковчега нашого Бога до нас, бо не зверта́лися ми до нього за Саулових днів“.
Tiyeni tibweretsenso Bokosi la Mulungu wathu kuno kwathu, pakuti nthawi ya Sauli sitinafunse za bokosili.”
4 І сказала вся громада, щоб зробити так, бо слу́шна була та річ в оча́х усього народу.
Gulu lonse linavomereza izi, pakuti anthu onse anaona kuti kunali kofunika kutero.
5 І зібрав Давид усього Ізраїля від єгипетського Шіхору й аж туди, де йде́ться до Хамату, щоб спрова́дити Божого ковчега з Кір'ят-Єаріму.
Kotero Davide anasonkhanitsa Aisraeli onse, kuchokera ku mtsinje wa Sihori ku Igupto mpaka ku Lebo Hamati, kuti abweretse Bokosi la Mulungu kuchokera ku Kiriati-Yearimu.
6 І пішов Давид та ввесь Ізра́їль у Баалу, в Юдин Кір'ят-Єарім, щоб ви́нести звідти ковчега Бога, Господа, що сидить на херувимах, що ім'я́ Його приклика́ється.
Davide pamodzi ndi Aisraeli onse anapita ku Baalahi (Kiriati-Yearimu) ku Yuda kukatenga Bokosi la Yehova Mulungu, amene amakhala pakati pa akerubi. Limeneli ndiye Bokosi la Chipangano lomwe limadziwika ndi Dzina lake.
7 І пове́зли Божого ковчега на ново́му возі з Авінадавового дому, а Узза та Ахйо прова́дили того воза.
Iwo anachotsa Bokosi la Mulungu ku nyumba ya Abinadabu pa ngolo yatsopano. Uza ndi Ahiyo ndiwo ankayendetsa ngoloyo.
8 А Давид та ввесь Ізраїль грали перед Божим лицем з усієї сили, — із пісня́ми, і на ци́трах, і на а́рфах, і на бу́бнах, і на цимба́лах, і на су́рмах.
Davide pamodzi ndi Aisraeli onse ankakondwerera ndi mphamvu zawo zonse pamaso pa Mulungu, poyimba nyimbo pogwiritsa ntchito azeze, apangwe, matambolini, maseche ndi malipenga.
9 І прийшли вони аж до Кідонового то́ку, і простяг Узза свою руку, щоб підхопи́ти ковчега, бо воли нахили́ли його.
Atafika pa malo opunthira tirigu ku Kidoni, Uza anatambalitsa dzanja lake kuti agwire bokosilo, chifukwa ngʼombe zinkafuna kugwa.
10 І запалився на Уззу гнів Господній, і Він убив його за те, що простяг руку свою до ковчега. І помер він там перед Господнім лицем...
Yehova anapsera mtima Uza ndipo anamukantha chifukwa chogwira bokosilo. Choncho iyeyo anafera pomwepo pamaso pa Mulungu.
11 І зажури́вся Давид тим, що Господь убив Уззу, і він назвав ім'я тому місцю: Перец-Узза, і так воно зветься аж до цього дня.
Ndipo Davide anakhumudwa chifukwa Yehova anakantha Uza ndipo mpaka lero malowo amatchedwa Perezi Uza.
12 І того дня Давид злякався Бога, говорячи: „Як я внесу́ до се́бе Божого ковчега?“
Tsiku limenelo Davide anachita mantha ndi Mulungu ndipo anafunsa kuti, “Kodi Bokosi la Mulungu lingafike bwanji kwathu?”
13 І не повіз Давид ковчега до се́бе, до Давидового Міста, а напра́вив його до дому гатянина Овед-Едома.
Iye sanapitenso nalo Bokosi la Mulungu ku Mzinda wa Davide. Mʼmalo mwake anapita nalo ku nyumba ya Obedi-Edomu Mgiti.
14 І пробува́в Божий ковчег із домом Овед-Едома в його домі три місяці. А Господь поблагослови́в дім Овед-Едома, та все, що було його́.
Ndipo Bokosi la Mulungu linakhala mʼbanja la Obedi-Edomu mʼnyumba mwake kwa miyezi itatu ndipo Yehova anadalitsa nyumba yake ndi chilichonse chimene anali nacho.