< Nnwom 92 >

1 Dwom a wɔto no Homeda. Ɛyɛ sɛ wɔkamfo wo Awurade na wɔto dwom de hyɛ wo animuonyam, Ao Ɔsorosoroni,
Salimo. Nyimbo ya pa tsiku la Sabata. Nʼkwabwino kutamanda Yehova ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,
2 na wɔpae mu ka wʼadɔeɛ anɔpa ne wo nokorɛ anadwo,
Kulengeza chikondi chanu mmawa, ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,
3 wɔ ahoma edu sankuo so ne sankuten nnwom mu.
kuyimbira nyimbo choyimbira cha zingwe khumi ndi mayimbidwe abwino a zeze.
4 Ao Awurade, wo nneyɛɛ ma mʼani gye; mede anigyeɛ bɛto dwom, wo nsa ano nnwuma enti.
Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova; Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu.
5 Ao Awurade, wo nnwuma yɛ akɛseɛ, na wo nyansa mu dɔ!
Ndi yayikuludi ntchito yanu Yehova, maganizo anu ndi ozamadi!
6 Ogyimifoɔ nnim na nkwaseafoɔ nte aseɛ,
Munthu wopanda nzeru sadziwa, zitsiru sizizindikira,
7 amumuyɛfoɔ bɛnyini sɛ ɛserɛ na abɔnefoɔ bɛyɛ frɔmfrɔm deɛ, nanso wɔbɛsɛe wɔn pasaa.
kuti ngakhale anthu oyipa aphuka ngati udzu ndipo anthu onse ochita zoyipa apindula, adzawonongedwa kwamuyaya.
8 Na wo Awurade, woyɛ kɛseɛ afebɔɔ.
Koma Inu Yehova, ndinu wokwezedwa kwamuyaya.
9 Ao Awurade ampa ara, wʼatamfoɔ bɛyera; na wobɛhwete abɔnefoɔ nyinaa.
Zoonadi adani anu Yehova, zoonadi adani anu adzawonongeka; onse ochita zoyipa adzabalalitsidwa.
10 Woama me ahoɔden te sɛ ɛkoɔ; woahwie ngohwam papa agu me so.
Inu mwakweza nyanga yanga ngati nyanga ya njati; mafuta abwino akhuthulidwa pamutu wanga.
11 Mahunu mʼatamfoɔ nkoguo a wɔadi, mate sɛdeɛ mʼatamfoɔ atirimuɔdenfoɔ adwane afiri akono.
Maso anga aona kugonjetsedwa kwa olimbana nane, makutu anga amva za kugwa kwa amaliwongo anga oyipa.
12 Ateneneefoɔ bɛyɛ frɔmm te sɛ abedua, wɔbɛnyini sɛ Lebanon ntweneduro;
Anthu olungama adzaphuka ngati mtengo wa mgwalangwa, adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
13 deɛ wɔadua wɔ Awurade fie, wɔbɛnyini frɔmfrɔm wɔ yɛn Onyankopɔn adihɔ hɔ.
odzalidwa mʼnyumba ya Yehova, adzakula bwino mʼmabwalo a Mulungu wathu.
14 Wɔbɛkɔ so aso aba, onyinkyerɛ mu mpo, wɔbɛyɛ frɔmm sɛ ahahammono,
Iwo adzaberekabe zipatso mu ukalamba wawo, adzakhala anthete ndi obiriwira,
15 de akyerɛ sɛ, “Awurade yɛ ɔteneneeni; ɔyɛ me botan, na atirimuɔdensɛm biara nni ne mu.”
kulengeza kuti, “Yehova ndi wolungama; Iye ndiye Thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe choyipa.”

< Nnwom 92 >