< Nnwom 132 >
1 Ɔsoroforɔ dwom. Ao Awurade kae Dawid ne ɔhaw ahodoɔ a ɔgyinaa ano no.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Inu Yehova, kumbukirani Davide ndi mavuto onse anapirira.
2 Ɔkaa Awurade ntam na ɔhyɛɛ Yakob Otumfoɔ no bɔ sɛ,
Iye analumbira kwa Yehova ndi kulonjeza kwa Wamphamvu wa Yakobo kuti,
3 “Merenhyɛne me fie na merenkɔda me mpa so,
“Sindidzalowa mʼnyumba mwanga kapena kugona pa bedi langa:
4 meremma nna mfa me na meremma mʼani nkum,
sindidzalola kuti maso anga agone, kapena zikope zanga ziwodzere,
5 kɔsi sɛ menya baabi ama Awurade, baabi a Yakob Otumfoɔ no bɛtena.”
mpaka nditamupezera malo Yehova, malo okhala a Wamphamvu wa Yakobo.”
6 Yɛtee wɔ Efrata, yɛbɛtoo so wɔ Yaar mfuo so.
Zoonadi, tinamva za Bokosi la Chipangano ku Efurata, tinalipeza mʼminda ya ku Yaara:
7 “Momma yɛnkɔ nʼatenaeɛ; momma yɛnsom wɔ ne nan ntiasoɔ hɔ.
“Tiyeni tipite ku malo ake okhalamo; tiyeni tikamulambire pa mapazi ake.
8 ‘Ao Awurade, sɔre bra wʼahomegyebea, wo ne wo tumi Adaka no.
‘Dzukani Yehova, ndipo bwerani ku malo anu opumulira, Inuyo ndi Bokosi la Chipangano limene limafanizira mphamvu zanu.
9 Ma tenenee nyɛ sɛ ntadeɛ mma wʼasɔfoɔ; ma wʼahotefoɔ nto ahurisie dwom.’”
Ansembe anu avekedwe chilungamo; anthu anu oyera mtima ayimbe nyimbo mwachimwemwe.’”
10 Wo ɔsomfoɔ Dawid enti, nyi wʼani mfiri deɛ woasra no ngo no so.
Chifukwa cha Davide mtumiki wanu, musakane wodzozedwa wanu.
11 Awurade kaa ntam kyerɛɛ Dawid, nokorɛ ntam a ɔrentwe nsane sɛ, “Wʼasefoɔ no mu baako na mede no bɛtena wʼahennwa so.
Yehova analumbira kwa Davide, lumbiro lotsimikizika kuti Iye sadzasintha: “Mmodzi wa ana ako ndidzamuyika pa mpando waufumu;
12 Sɛ wo mmammarima di mʼapam so na wɔtie me nkyerɛkyerɛ a, ɛnneɛ wɔn mmammarima bɛtena wʼahennwa so afebɔɔ.”
ngati ana ako azisunga pangano langa ndi malamulo amene ndiwaphunzitsa, pamenepo ana awo adzakhala pa mpando wako waufumu kwamuyaya ndi muyaya.”
13 Awurade ayi Sion, ɔde hɔ ayɛ nʼatenaeɛ:
Pakuti Yehova wasankha Ziyoni, Iye wakhumba kuti akhale malo ake okhalamo:
14 “Ɛha ne mʼahomegyebea daa nyinaa; ɛha na mɛtena adi ɔhene, ɛfiri sɛ ɛha na mepɛ,
“Awa ndi malo anga opumapo ku nthawi za nthawi; ndidzakhala pano pa mpando waufumu, pakuti ndakhumba zimenezi.
15 mede nneɛma pa bebree bɛhyira no na mama nʼahiafoɔ adidi amee.
Ndidzadalitsa mzindawu ndi zinthu zambiri; anthu ake osauka ndidzawakhutitsa ndi chakudya.
16 Mede nkwagyeɛ bɛfira nʼasɔfoɔ na nʼahotefoɔ ato ahurisie dwom daa.
Ndidzaveka ansembe ake chipulumutso, ndipo anthu ake oyera mtima adzayimba nthawi zonse nyimbo zachimwemwe.
17 “Mɛma ɔberempɔn bi apue wɔ Dawid ahennie mu na mede kanea asi hɔ ama deɛ masra no ngo no.
“Pano ndidzachulukitsa mphamvu za Davide ndi kuyikapo nyale ya wodzozedwa wanga.
18 Mede aniwuo bɛfira nʼatamfoɔ, nanso nʼahenkyɛ bɛhyerɛn wɔ ne tiri so.”
Ndidzaveka adani ake manyazi, koma chipewa chaufumu pamutu pake chidzakhala chowala.”