< Mmɛbusɛm 7 >
1 Me ba, fa me nsɛm sie na kora mʼahyɛdeɛ wɔ wo mu.
Mwana wanga, mvera mawu anga; usunge bwino malamulo angawa.
2 Di mʼahyɛdeɛ so na wobɛnya nkwa; bɔ me nkyerɛkyerɛ ho ban sɛ deɛ wodɔ noɔ.
Utsate malamulo anga ndipo udzakhala ndi moyo; samala malangizo angawa monga uchitira ndi maso ako.
3 Kyekyere bɔ wo nsateaa ho; twerɛ no yie gu wʼakoma ɛpono so.
Uchite ngati wawamangirira pa zala zako, ndiponso ngati kuti wawalemba pa mtima pako.
4 Ka kyerɛ nyansa sɛ, “Wo yɛ me nuabaa,” na frɛ nteaseɛ wo busuani;
Nzeru uyiwuze kuti, “Iwe ndiwe mlongo wanga,” ndipo khalidwe lomvetsa bwino zinthu ulitchule kuti, “Bwenzi langa lapamtima.”
5 Wɔbɛtwe wo afiri ɔbaawaresɛefoɔ ho, afiri ɔbaawarefoɔ sansani nsɛmmɔdɛ ho.
Zidzakuteteza kwa mkazi wachigololo ndiponso zidzakuthandiza kusamvera mawu oshashalika a mkazi wachilendo.
6 Me fie mpomma ano mede mʼani faa ntokua mu.
Tsiku lina pa zenera la nyumba yanga ndinasuzumira pa zenera.
7 Mehunuu wɔ ntetekwaafoɔ mu, mehyɛɛ mmeranteɛ no mu baako nso, ɔbabunu a ɔnni adwene.
Ndinaona pakati pa anthu opusa, pakati pa anyamata, mnyamata wina wopanda nzeru.
8 Na ɔnam borɔno a ɛbɛn ɔbaa no fie so a nʼani kyerɛ ɔbaa no fie
Iye ankayenda njira yodutsa pafupi ndi nyumba ya mkaziyo, kuyenda molunjika nyumba ya mkaziyo.
9 ɛberɛ a ɔnwunu redwoɔ, na animu rebiribiri no.
Inali nthawi yachisisira madzulo, nthawi ya usiku, kuli mdima.
10 Afei ɔbaa bi firi bɛhyiaa no a wasiesie ne ho sɛ odwamanfoɔ a nnaadaa wɔ nʼakomam.
Ndipo mkaziyo anadzakumana naye, atavala ngati munthu wachiwerewere wa mtima wonyenga.
11 (Ɔyɛ hyirenn na hwee mfa ne ho, ɔntena efie koraa;
(Mkaziyo ndi wolongolola ndiponso nkhutukumve, iye ndi wosakhazikika pa khomo.
12 ɛnnɛ wɔhunu no mmɔntene so, ɔkyena na ɔte adwaberem, ɔtetɛ wɔ mmantwea mmantwea.)
Mwina umupeza pa msewu, mwina umupeza pa msika, ndipo amadikirira munthu pa mphambano iliyonse).
13 Ɔsɔɔ ne mu fee nʼano wamfɛre, na ɔkaa sɛ,
Tsono amagwira mnyamatayo ndi kupsompsona ndi nkhope yake yopanda manyazi amamuwuza kuti,
14 “Mewɔ ayɔnkofa ayɛyɛdeɛ wɔ efie; ɛnnɛ madi me bɔhyɛ so.
“Ndinayenera kupereka nsembe zachiyanjano. Lero ndakwaniritsa malumbiro anga.
15 Enti mebaeɛ sɛ merebɛhyia wo; mehwehwɛɛ wo na mahunu wo!
Choncho ndinabwera kudzakumana nawe; ndinkakufunafuna ndipo ndakupeza!
16 Mato me mpa mede nwera a wɔahyɛ no aduro a ɛfiri Misraim.
Pa bedi panga ndayalapo nsalu zosalala zokongola zochokera ku Igupto.
17 Mede nnuhwam apete me mpa so: kurobo, pɛperɛ ne sinamon.
Pa bedi panga ndawazapo zonunkhira za mure, mafuta onunkhira a aloe ndi sinamoni.
18 Bra, ma yɛmfa ɔdɔ mmɔ ɔdɔ mu nkɔsi anɔpa;
Bwera, tiye tikhale malo amodzi kukondwerera chikondi mpaka mmawa; tiye tisangalatsane mwachikondi!
19 Me kunu nni efie; watu kwan na ɔbɛkyɛre.
Mwamuna wanga kulibe ku nyumbako; wapita ulendo wautali:
20 Ɔde sika a ɛdɔɔso hyɛɛ ne sikabɔtɔ ma na ɔremma kɔsi ɔsrane no korokumatwa berɛ mu.”
Anatenga thumba la ndalama ndipo adzabwera ku nyumba mwezi ukakhwima.”
21 Ɔde akorɔkorɔ bɔɔ no asɔn; ɔde nnaadaa nyaa no ne no daeɛ.
Ndi mawu ake onyengerera amamukakamiza mnyamatayo; amukopa ndi mawu ake oshashalika.
22 Ɔdii nʼakyi prɛko pɛ te sɛ nantwie a ɔrekɔ akumiiɛ, anaa ɔwansane a ɔde ne tiri rekɔhyɛ hankrafidie mu
Nthawi yomweyo chitsiru chimamutsatira mkaziyo ngati ngʼombe yopita kukaphedwa, monga momwe mbawala ikodwera mu msampha,
23 kɔsi sɛ bɛmma bɛhwire ne brɛboɔ mu, te sɛ anomaa a ɔrekɔtɔ anomaa afidie mu na ɔnnim sɛ ɔbɛhwere ne nkwa.
mpaka muvi utalasa chiwindi chake, chimakhala ngati mbalame yothamangira mʼkhwekhwe, osadziwa kuti moyo wake uwonongeka.
24 Na afei, me mma, montie me; monyɛ aso mma deɛ meka.
Tsono ana inu, ndimvereni; mvetsetsani zimene ndikunena.
25 Mommma mo akoma mpatere nkɔ ne so na mommane mfa nʼakwan so.
Musatengeke mtima ndi njira za mkazi ameneyu; musasochere potsata njira zake.
26 Bebree na wɔnam ne so ahwehwe ase; wɔn a wakum wɔn dɔɔso pa ara.
Paja iye anagwetsa anthu ambiri; wapha gulu lalikulu la anthu.
27 Ne fie yɛ ɛda kwantempɔn a ɛkɔ owuo mpia mu. (Sheol )
Nyumba yake ndi njira yopita ku manda, yotsikira ku malo a anthu akufa. (Sheol )