< Hiob 33 >

1 “Na afei, Hiob, tie me nsɛm; yɛ aso ma biribiara a mɛka.
“Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga; mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
2 Merebɛbue mʼano; me nsɛm aba me tɛkrɛma so.
Tsopano ndiyamba kuyankhula; mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
3 Me nsɛm firi akoma a ɛtene mu; na mʼano de ahonim pa ka deɛ menim.
Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama; pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
4 Onyankopɔn Honhom na abɔ me; Otumfoɔ no ahome ma me nkwa.
Mzimu wa Mulungu wandiwumba, mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
5 Sɛ wobɛtumi a, ma me mmuaeɛ; siesie wo ho, na ka si mʼanim.
Mundiyankhe ngati mungathe; konzekani tsopano kuti munditsutse.
6 Wo ne me nyinaa yɛ pɛ wɔ Onyankopɔn anim; me nso wɔbɔɔ me firii dɔteɛ mu.
Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu; nanenso ndinachokera ku dothi.
7 Ɛnsɛ sɛ wosuro me, na ɛnsɛ sɛ me nsa yɛ den wɔ wo so.
Musachite mantha ndipo musandiope ayi, Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.
8 “Nanso woaka ama mate, metee saa nsɛm no, na wokaa sɛ,
“Koma inu mwayankhula ine ndikumva, ndamva mawu anuwo onena kuti,
9 ‘Meyɛ kronn na menni bɔne; me ho te na afɔdie biara nni me ho.
‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo; ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
10 Nanso Onyankopɔn anya me ho mfomsoɔ; wafa me sɛ ne ɔtamfoɔ.
Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo; Iye akundiyesa ngati mdani wake.
11 Ɔde me nan ahyɛ mpɔkyerɛ mu; na nʼani wɔ mʼakwan nyinaa so.’
Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo, akulonda mayendedwe anga onse.’
12 “Nanso meka mekyerɛ wo sɛ, yei mu deɛ, woayɛ mfomsoɔ, ɛfiri sɛ Onyankopɔn so sene ɔdasani.
“Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi, pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
13 Na adɛn enti na wonwiinwii hyɛ no sɛ ɔmmua onipa nsɛm biara anaa?
Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
14 Nanso, Onyankopɔn kasa wɔ akwan ahodoɔ so, na ebia nnipa nte.
Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana, ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
15 Ɔkasa wɔ daeɛso ne anadwo anisoadehunu mu, ɛberɛ a nna afa nnipa na wɔretu nkorɔmo wɔ wɔn mpa so,
Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku, pamene anthu ali mʼtulo tofa nato pamene akungosinza chabe pa bedi,
16 ɔtumi kasa gu wɔn asom na ɔde kɔkɔbɔ yi wɔn hu,
amawanongʼoneza mʼmakutu ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
17 sɛ ɔbɛdane onipa afiri nneyɛɛ bɔne ho na watwe no afiri ahantan ho,
kumuchotsa munthu ku zoyipa, ndi kuthetseratu kunyada kwake,
18 sɛ ɔmma ne ɔkra nnkɔ amena mu na ɔnhwere ne nkwa wɔ akofena ano.
kumulanditsa munthu ku manda, kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.
19 Onyankopɔn tumi de yea twe onipa aso ɛberɛ a ɔda mpa so na ne nnompe mu yea nnyae da,
“Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake, nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
20 kɔsi sɛ ne kɔn nnɔ aduane na ne ɔkra nso po aduane a ɛyɛ akɔnnɔ pa ara;
kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya, ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
21 ɔfɔn yɛ basaa, na ne nnompe a anka ɛho akata no ho da hɔ.
Thupi lake limawonda ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
22 Ne ɔkra bɛn damena, na ne nkwa bɛn owuo abɔfoɔ.
Munthuyo amayandikira ku manda, moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.
23 “Nanso sɛ abɔfoɔ apem no mu baako wɔ nʼafa sɛ ɔdimafoɔ a ɔbɛkyerɛ no deɛ ɛyɛ ma no a,
“Koma patakhala mngelo ngati mthandizi, mmodzi mwa ambirimbiri oterewa, adzafotokoza zimene zili zoyenera,
24 ɔbɛhunu no mmɔbɔ na waka sɛ, ‘Monnyaa no na wankɔ damena mu; na manya mpatadeɛ ama no,’
kudzamukomera mtima ndi kunena kuti, ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda; ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
25 afei ne wedeɛ bɛyɛ foforɔ sɛ abɔfra deɛ, na asi ne dada mu sɛ mmeranteberɛ mu deɛ.
pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana; ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
26 Sɛ ɔbɔ Onyankopɔn mpaeɛ a, ɔbɛnya adom afiri ne hɔ, ɔbɛhunu Onyankopɔn anim na ɔde ahosɛpɛ ateam na Onyankopɔn agye no bio sɛ ɔteneneeni.
Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa. Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
27 Afei ɔbɛba nnipa mu abɛka sɛ, ‘Meyɛɛ bɔne na mekyeaa deɛ ɛtene, nanso wantwe mʼaso sɛdeɛ ɛfata me.
Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti, ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama, koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
28 Ɔgyee me ɔkra na wamma no ankɔ damena mu, enti mɛtena ase na madi hann no mu dɛ.’
Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda, ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’
29 “Onyankopɔn yɛ yeinom nyinaa ma onipa, mprɛnu ne ne mprɛnsa so,
“Mulungu amachita zonsezi kwa munthu kawirikawiri,
30 sɛdeɛ onipa kra renkɔ damena mu, na nkwa hann no ahyerɛn ne so.
kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda, kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.
31 “Yɛ aso, Hiob, na tie me; yɛ dinn na menkasa.
“Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere; khalani chete kuti ndiyankhule.
32 Na sɛ wowɔ biribi ka a, bua me; kasa, na mepɛ sɛ wɔbu wo bem.
Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni; yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
33 Sɛ ɛnte saa nso a, ɛnneɛ tie me. Yɛ dinn na mɛkyerɛ wo nyansa.”
Koma ngati sichoncho, mundimvere; khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”

< Hiob 33 >