< Hiob 21 >

1 Na Hiob buaa sɛ,
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 “Montie me nsɛm no yie. Momma yei nyɛ awerɛkyekyerɛ a mode ma me.
“Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
3 Monnya ntoboaseɛ mma me ɛberɛ a merekasa, na sɛ mekasa wie a, monkɔso nni fɛ.
Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.
4 “Me nwiinwii hyɛ onipa anaa? Adɛn enti na ɛsɛ sɛ menya ntoboaseɛ?
“Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
5 Monhwɛ me, na mo ho nnwiri mo; momfa mo nsa nkata mo ano.
Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa.
6 Sɛ medwene yei ho a, mebɔ hu; na me ho popo.
Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera.
7 Adɛn enti na amumuyɛfoɔ tena nkwa mu? Wɔnyini kyɛ na wɔkɔ so di tumi.
Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
8 Wɔhunu wɔn mma a atwa wɔn ho ahyia no nkɔsoɔ, wɔhunu wɔn nananom.
Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
9 Ɔhaw nni wɔn afie na ehu nni hɔ; Onyankopɔn asotwe mma wɔn so.
Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
10 Wɔn anantwinini nyɛ akrawa; na wɔn anantwibereɛ wo a, wɔmpɔn.
Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
11 Wɔka wɔn mma bɔ mu te sɛ nnwankuo; na emu mmotafowa no hurihuri.
Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo.
12 Wɔto nnwom wɔ akasaeɛ ne sankuo so; na wɔde atɛntɛbɛn nnyegyeeɛ gye wɔn ani.
Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
13 Wɔdi yie wɔn nkwanna mu na wɔkɔ damena mu asomdwoeɛ mu. (Sheol h7585)
Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
14 Nanso wɔka kyerɛ Onyankopɔn sɛ, ‘Firi yɛn so! Yɛmpɛ sɛ yɛhunu wʼakwan.
Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
15 Hwan ne otumfoɔ no a ɛsɛ sɛ yɛsom no? Sɛ yɛbɔ no mpaeɛ a mfasoɔ bɛn na yɛbɛnya?’
Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
16 Nanso, wɔn nkɔsoɔ no nni wɔn nsam, enti metwe me ho firi amumuyɛfoɔ afutuo ho.
Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.
17 “Nanso mpɛn ahe na wɔdum amumuyɛfoɔ kanea? Mpɛn ahe na amanehunu ba wɔn so, deɛ Onyankopɔn firi nʼabufuo mu de ba no?
“Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
18 Mpɛn ahe na wɔyɛ sɛ ɛserɛ wɔ mframa ano, te sɛ ntɛtɛ a mframa den bi apra wɔn?
Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
19 Wɔka sɛ, ‘Onyankopɔn kora onipa asotwe so de twɛn ne mma.’ Ɛsɛ sɛ ɔtwe ɔnipa no ankasa aso ma ɔhunu.
Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
20 Ma wɔn ankasa ani nhunu wɔn sɛeɛ; ma Otumfoɔ abufuhyeɛ no nka wɔn ani.
Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
21 Wɔn abusuafoɔ a wɔagya wɔn akyire no renya hwee nʼagyapadeɛ nyinaa bɛsɛe.
Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?
22 “Obi bɛtumi akyerɛ Onyankopɔn nyansa, wɔ ɛberɛ a ɔbu atitire mpo atɛn?
“Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
23 Obi wu wɔ ɛberɛ a ɔwɔ ahoɔden; ne ho tɔ no na nʼaso mu adwo no,
Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
24 na ne onipadua yɛ frɔmm, na ɛhon ahyɛ ne nnompe ma.
thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
25 Ɔfoforɔ nso de ɔkra mu yeadie wu, a wanka asetena pa anhwɛ da.
Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
26 Wɔsie wɔn nyinaa wɔ mfuturo korɔ mu, ma asonson korɔ no ara nuka wɔn.
Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi.
27 “Mahunu mo adwene, ɛkwan a mopɛ sɛ mobu me fɔ.
“Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
28 Mopɛ sɛ moka kyerɛ me sɛdeɛ asikafoɔ ne amumuyɛfoɔ, wɔn bɔne enti, wɔhwere wɔn agyapadeɛ nyinaa.
Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
29 Nanso mommisa wɔn a wɔtu kwan; wɔbɛka akyerɛ mo sɛ
Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
30 onipa bɔne nya ne ti didi mu amanehunu da, na wɔgyaa no ma no dwane abufuhyeɛ da.
Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
31 Hwan na ɔtumi kasa nʼanim? Hwan na ɔtua no deɛ wayɛ so ka?
Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
32 Wɔsoa no kɔ damena mu, na wɔwɛn nʼaboda.
Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake.
33 Bɔnhwa mu dɔteɛ yɛ no dɛ; nnipa nyinaa di nʼakyi, na ɛdɔm a wɔntumi nkan wɔn di nʼanim.
Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.
34 “Enti ɛbɛyɛ dɛn na mode mo nsɛnhunu akyekyere me werɛ? Mo mmuaeɛ nyɛ hwee sɛ atorɔ!”
“Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”

< Hiob 21 >