< Hosea 12 >

1 Efraim de mframa ayɛ aduane; ɔdi apueeɛ mframa akyi daa na ɔdi atorɔ yɛ akakabensɛm bebree. Ɔne Asiria yɛ apam na ɔde ngo kɔ Misraim.
Efereimu amadya mpweya; tsiku lonse amasaka mphepo ya kummawa ndipo amachulukitsa mabodza ndi chiwawa. Amachita mgwirizano ndi Asiriya ndipo amatumiza mphatso za mafuta a olivi ku Igupto.
2 Awurade wɔ soboɔ de bɔ Yuda; ɔbɛtwe Yakob aso, wɔ nʼakwan ho na watua no ne nneyɛeɛ so ka.
Yehova akuyimba mlandu Yuda; Iye adzalanga Yakobo molingana ndi makhalidwe ake, adzamulanga molingana ndi ntchito zake.
3 Ɔyafunu mu na ɔsɔɔ ne nua nantin; ɔnyiniiɛ no, ɔne Onyankopɔn pepree so.
Akali mʼmimba mwa amayi ake, Yakobo anagwira chidendene cha mʼbale wake; iye atakula analimbana ndi Mulungu.
4 Ɔne ɔbɔfoɔ tentameeɛ dii ne so nkonim; ɔde nisuo srɛɛ ne nkyɛn adom. Ɔhunuu no wɔ Bet-El ne no kasaa wɔ hɔ.
Yakobo analimbana ndi mngelo ndipo anapambana; analira napempha kuti amukomere mtima. Mulungu anakumana naye ku Beteli ndipo anayankhula naye kumeneko,
5 Asafo Awurade Onyankopɔn, Awurade ne ne din a ahyeta!
Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Yehova ndiye dzina lake lotchuka!
6 Ɛsɛ sɛ wo sane kɔ wo Onyankopɔn nkyɛn. Tena ɔdɔ ne tenenee mu, na twɛn wo Onyankopɔn daa.
Koma inu muyenera kubwerera kwa Mulungu wanu; pitirizani chikondi ndi chiweruzo cholungama, ndipo muzidikira Mulungu wanu nthawi zonse.
7 Ɔdwadini de nsisie nsania yɛ nʼadwuma; nʼani gye nsisie ho.
Munthu wamalonda amagwiritsa ntchito masikelo achinyengo; iyeyo amakonda kubera anthu.
8 Efraim hoahoa ne ho sɛ, “Meyɛ ɔdefoɔ; manya me ho. Mʼahonya nyinaa mu wɔrenhunu amumuyɛ biara wɔ me ho.”
Efereimu amadzitama ponena kuti, “Ndine wolemera kwambiri; ndili ndi chuma chambiri. Palibe amene angandiloze chala chifukwa cha kulemera kwanga.”
9 “Mene Awurade wo Onyankopɔn, a meyii wo firii Misraim. Mɛma woakɔtena ntomadan mu bio sɛdeɛ na woyɛ wɔ wʼapontoɔ afahyɛ nna mu no.
“Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa mu Igupto. Ndidzakukhazikaninso mʼmatenti, monga munkachitira masiku aja pa nthawi ya zikondwerero zanu.
10 Mekasa kyerɛɛ adiyifoɔ, memaa wɔn anisoadehunu bebree na mefaa wɔn so kaa mmɛbusɛm.”
Ndinayankhula ndi aneneri, ndinawaonetsa masomphenya ambiri, ndipo ndinawawuza mafanizo kudzera mwa iwo.”
11 Gilead yɛ otirimuɔdenfoɔ anaa? Emu nnipa no yɛ ahuhufoɔ! Wɔde anantwie bɔ afɔdeɛ wɔ Gilgal anaa? Wɔn afɔrebukyia bɛyɛ te sɛ aboɔ a wɔahɔre no sie wɔ asase a wɔafuntum soɔ.
Kodi Giliyadi ndi woyipa? Anthu ake ndi achabechabe! Kodi amapereka nsembe za ngʼombe zazimuna ku Giligala? Maguwa awo ansembe adzakhala ngati milu ya miyala mʼmunda molimidwa.
12 Yakob dwane kɔɔ Aramfoɔ asase so; Israel someeɛ de nyaa yere, ɔhwɛɛ nnwan de tua etiri nsa.
Yakobo anathawira ku dziko la Aramu, Israeli anagwira ntchito kuti apeze mkazi, ndipo anaweta nkhosa kuti akwatire mkaziyo.
13 Awurade nam odiyifoɔ so yii Israel firii Misraim, ɔnam odiyifoɔ so hwɛɛ no.
Yehova anagwiritsa ntchito mneneri kuti atulutse Israeli mu Igupto; kudzera mwa mneneriyo Iye anawasamalira.
14 Nanso, Efraim ahyɛ no abufuo yaayaaya; nʼAwurade bɛma ne mogyahwiegu ho afɔdie ada ne so na ɔbɛtua nʼanimtiabuo no so ka.
Koma Efereimu wamukwiyitsa kwambiri. Nʼchifukwa chake Yehova adzawalanga ndi imfa. Adzawalanga chifukwa anamuchititsa manyazi kwambiri.

< Hosea 12 >