< Sefania 3 >

1 Nnome nka nhyɛsofo kuropɔn atuatew kuropɔn a ho agu fi!
Tsoka kwa mzinda wa anthu opondereza, owukira ndi odetsedwa!
2 Ɔnyɛ osetie mma obiara onnye nteɛso biara nto mu. Ɔmfa ne ho nto Awurade so. Ontwiw mmɛn ne Nyankopɔn.
Sumvera aliyense, sulandira chidzudzulo. Sumadalira Yehova, suyandikira pafupi ndi Mulungu wake.
3 Nʼakannifo yɛ gyata a wɔbobɔ mu, ne sodifo yɛ mpataku a wɔnam anadwo, a wonnya biribiara mma adekyee.
Akuluakulu ake ali ngati mikango yobuma, olamulira ake ndi olusa ngati mimbulu ya nthawi ya madzulo, zimene pofika mmawa sizisiya chilichonse.
4 Ne nkɔmhyɛfo yɛ ahantan; wɔyɛ afatwafo. Nʼasɔfo gu kronkronbea ho fi. Wɔnam mmara no so di nsɛmmɔne.
Aneneri ake ndi odzikuza; anthu achinyengo. Ansembe ake amadetsa malo opatulika ndipo amaphwanya lamulo.
5 Awurade a ɔte ne mu no yɛ ɔtreneeni; ɔnyɛ mfomso biara. Adekyee biara, ɔda ne trenee adi, na onni huammɔ da, nanso amumɔyɛfo de, wonnim aniwu.
Yehova amene ali pakati pawo ndi wolungama; Iye salakwa. Tsiku ndi tsiku amaweruza molungama, ndipo tsiku lililonse salephera, komabe ochita zoyipa sachita manyazi nʼkomwe.
6 “Masɛe amanaman; madwiriw wɔn abandennen agu. Wɔn mmorɔn so adeda mpan, a obiara ntwa mu hɔ. Wɔasɛe wɔn nkuropɔn; a obiara renka.
“Ndachotseratu mitundu ya anthu; ndagwetsa malinga awo. Ndipo sindinasiye ndi mmodzi yemwe mʼmisewu mwawo, popanda aliyense wodutsa. Mizinda yawo yawonongedwa; palibe aliyense adzatsalemo.
7 Meka kyerɛɛ kuropɔn no se, ‘ampa ara wubesuro me na woagye nteɛso ato mu!’ Na afei ne tenabea rensɛe, na mʼasotwe biara nso remma no so. Nanso wɔn ho peree wɔn sɛ wɔbɛkɔ so ayɛ bɔne, wɔn nneyɛe nyinaa mu.
Ndinati, ‘Ndithudi, anthu a mu mzindawu adzandiopa ndi kumvera kudzudzula kwanga!’ Ndipo sindidzawononga nyumba zawo, kapena kuwalanganso. Koma iwo anali okonzeka kuchita mwachinyengo zinthu zonse zimene amachita.
8 Enti twɛn me,” sɛnea Awurade se ni, “na da no mɛsɔre adi adanse. Mayɛ mʼadwene sɛ mɛboaboa amanaman ne ahenni ano na mahwie mʼabufuw agu wɔn so mʼabufuwhyew nyinaa. Me ninkutwe abufuw gya mu no, asase nyinaa bɛhyew.
Choncho mundidikire,” akutero Yehova, “chifukwa cha tsiku limene ndidzaperekera umboni. Ndatsimikiza kusonkhanitsa pamodzi mitundu ya anthu, kusonkhanitsa maufumu ndi kutsanulira ukali wanga pa iwo; mkwiyo wanga wonse woopsa. Dziko lonse lidzatenthedwa ndi moto wa mkwiyo wa nsanje yanga.
9 “Afei medwira nnipa no ano, na wɔn nyinaa abɔ Awurade din na wɔaka abɔ mu asom no.
“Pamenepo ndidzayeretsa milomo ya anthu a mitundu yonse kuti anthu onsewo ayitane dzina la Yehova ndi kumutumikira Iye pamodzi.
10 Mʼasomfo, me nkurɔfo a wɔabɔ ahwete no befi nsubɔnten a ɛwɔ Kus nohɔ de wɔn afɔrebɔde abrɛ me.
Kuchokera kutsidya kwa mitsinje ya ku Kusi anthu anga ondipembedza, omwazikana, adzandibweretsera zopereka.
11 Saa da no, wo Yerusalem, wɔrengu wʼanim ase wɔ nneyɛe bɔne a woayɛ atia me ho, efisɛ meyi afi saa kuropɔn yi mu, wɔn a wodi ahantan mu ahurusi, na worenyɛ ahantan bio wɔ me bepɔw kronkron no so.
Tsiku limenelo simudzachita manyazi chifukwa cha zoyipa zonse munandichitira, popeza ndidzachotsa onse mu mzinda uwu amene amakondwera chifukwa cha kunyada kwawo. Simudzakhalanso odzikuza mʼphiri langa lopatulika.
12 Nanso megyaw wɔ wo mu wɔn a wodwo na wɔbrɛ wɔn ho ase, na wɔde wɔn ho to Awurade so no.
Koma ndidzasiya pakati panu anthu ofatsa ndi odzichepetsa, amene amadalira dzina la Yehova.
13 Wɔrenyɛ bɔne biara; wɔrenka nkontomposɛm, na wɔn ano renka nnaadaasɛm wobedidi na wɔada, na obiara renyi wɔn hu.”
Aisraeli otsala sadzachitanso zolakwika; sadzayankhulanso zonama, ngakhale chinyengo sichidzatuluka mʼkamwa mwawo. Adzadya ndi kugona ndipo palibe amene adzawachititse mantha.”
14 To dwom, Ɔbabea Sion; teɛ mu dennen, Israel! Ma wʼani nnye, na di ahurusi wɔ wo koma nyinaa mu, Ɔbabea Yerusalem!
Imba, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni; fuwula mokweza, iwe Israeli! Sangalala ndi kukondwera ndi mtima wako wonse, iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!
15 Efisɛ Awurade ayi wʼasotwe afi wo so, wama wo tamfo asan nʼakyi. Awurade, Israelhene ka wo ho; worensuro ɔhaw biara bio.
Yehova wachotsa chilango chako, wabweza mdani wako. Yehova, Mfumu ya Israeli, ali pakati pako; sudzaopanso chilichonse.
16 Saa da no, wɔbɛka akyerɛ Yerusalem se, “Nsuro, Sion! Mma wo nsa mu ngow.
Pa tsiku limenelo adzanena kwa Yerusalemu kuti, “Usaope, iwe Ziyoni; usafowoke.
17 Awurade wo Nyankopɔn ne wo wɔ hɔ, Ɔyɛ ogyefo ɔhoɔdenfo. Nʼani begye wo ho ne dɔ mu, ɔrenka wʼanim bio, ɔde nnwonto bedi wo ho anigye.”
Yehova Mulungu wako ali pakati pako, ali ndi mphamvu yopulumutsa. Adzakondwera kwambiri mwa iwe, adzakukhalitsa chete ndi chikondi chake, adzayimba mokondwera chifukwa cha iwe.”
18 “Meyi wɔn a wodi awerɛhow wɔ wʼafahyɛnna ahorow a woahwere; a ayɛ adesoa ne animguase ama wo no ho.
“Ndidzakuchotserani zowawa za pa zikondwerero zoyikika; nʼzolemetsa ndi zochititsa manyazi.
19 Saa bere no me ne wɔn a wɔhyɛɛ wo so nyinaa bedi. Megye mmerɛwyɛfo na mɛboaboa wɔn a wɔabɔ wɔn ahwete no ano. Mɛkamfo wɔn ahyɛ wɔn anuonyam asase biara a woguu wɔn anim ase wɔ so no so.
Taonani, nthawi imeneyo ndidzathana ndi onse amene anakuponderezani; ndidzapulumutsa olumala ndi kusonkhanitsa amene anamwazika. Ndidzawayamikira ndi kuwachitira ulemu mʼdziko lililonse mmene anachititsidwa manyazi.
20 Saa bere no, mɛboaboa mo ano; saa bere no, mede mo bɛba fie. Mɛhyɛ wo anuonyam na makamfo mo wɔ asase so nnipa nyinaa mu bere a mede mo ahonyade bɛsan ama wo na mode mo ani behu no,” sɛnea Awurade se ni.
Pa nthawi imeneyo ndidzakusonkhanitsani; pa nthawi imeneyo ndidzakubweretsani ku mudzi kwanu. Ndidzakuyamikirani ndi kukuchitirani ulemu pakati pa mitundu ya anthu a dziko lapansi pamene ndidzabwezeretsa mtendere wanu inu mukuona,” akutero Yehova.

< Sefania 3 >