< Nnwom 85 >

1 Wɔde ma dwonkyerɛfo. Koramma dwom. Wo Awurade, wodom wʼasase; wode Yakob ahonyade san maa no.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Yehova munakomera mtima dziko lanu; munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo.
2 Wode wo nkurɔfo bɔne kyɛɛ wɔn na wokataa wɔn nnebɔne nyinaa so.
Munakhululukira mphulupulu za anthu anu ndi kuphimba machimo awo onse. (Sela)
3 Wode wʼabufuw nyinaa too nkyɛn na wodan fii wʼabufuwhyew ho.
Munayika pambali ukali wanu wonse ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa.
4 San gye yɛn bio, Onyankopɔn, yɛn Gyefo, na ma wʼani nnye yɛn ho.
Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, ndipo mutichotsere mkwiyo wanu.
5 Wo bo befuw yɛn akosi daa ana? Wʼabufuw bɛtoa so akɔ awo ntoantoaso nyinaa so ana?
Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse?
6 Worenhyɛ yɛn den bio, na ama wo nkurɔfo asɛpɛw wɔn ho wɔ wo mu ana?
Kodi simudzatitsitsimutsanso, kuti anthu anu asangalale mwa Inu?
7 Awurade, kyerɛ yɛn wo dɔ a ɛnsa da no, na ma yɛn wo nkwagye no.
Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova, ndipo tipatseni chipulumutso chanu.
8 Metie nea Awurade Nyankopɔn bɛka; ɔde asomdwoe hyɛ ne nkurɔfo, ahotefo no bɔ, enti ɛnsɛ sɛ wɔsan kɔ agyimisɛm ho.
Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena; Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake, koma musawalole kuti abwerere ku zopusa.
9 Ampa ara, ne nkwagye bɛn wɔn a wosuro no, na nʼanuonyam bɛtena yɛn asase so.
Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye, kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu.
10 Ɔdɔ ne nokwaredi behyia, na trenee ne asomdwoe befew wɔn ho wɔn ho ano.
Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi; chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana.
11 Nokwaredi bepue afi asase no so, na trenee ahwɛ afi ɔsoro.
Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi, ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba.
12 Awurade bɛma yɛn nea eye ampa ara na yɛn asase bɛma ne nnɔbae.
Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino, ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.
13 Trenee di nʼanim siesie ɔkwan ma nʼanammɔntu.
Wolungama amapita patsogolo pake ndi kukonza njira za mapazi ake.

< Nnwom 85 >