< Nnwom 48 >

1 Koramma dwom. Awurade yɛ ɔkɛse na ɔsɛ nkamfo, wɔ yɛn Nyankopɔn kuropɔn mu, ne bepɔw kronkron so.
Nyimbo. Salimo la ana a Kora. Wamkulu ndi Yehova, ndi woyenera kwambiri matamando mu mzinda wa Mulungu wathu, phiri lake loyera.
2 Ne sorokɔ ma ɛyɛ fɛ, ɛyɛ wiase nyinaa anigyede. Bepɔw Sion te sɛ Safon sorɔnsorɔmmea, Ɔhenkɛse no kuropɔn.
Lokongola mu utali mwake, chimwemwe cha dziko lonse lapansi. Malo aatali kwambiri a Zafoni ndiye Phiri la Ziyoni, mzinda wa Mfumu yayikulu.
3 Onyankopɔn te nʼabankɛse mu wada ne ho adi sɛ ɔyɛ nʼabandennen.
Mulungu ali mu malinga ake; Iye wadzionetsa yekha kuti ndiye malinga akewo.
4 Bere a ahemfo yi boaa wɔn ho ano, na wotuu ɔsa bɔɔ mu no,
Pamene mafumu anasonkhana pamodzi, pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,
5 wohuu no ma ɛyɛɛ wɔn ahodwiriw, na wɔde ehu guanee.
iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri; anathawa ndi mantha aakulu.
6 Wɔbɔɔ huboa wɔ hɔ, ɔyaw a ɛte sɛ ɔbea a awo aka no.
Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera, ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.
7 Wosɛe wɔn sɛ Tarsis ahyɛn a apuei mframa abɔ adwira wɔn.
Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.
8 Sɛnea yɛate no, saa ara na yɛahu wɔ Asafo Awurade kuropɔn no mu, yɛn Nyankopɔn kuropɔn mu; Onyankopɔn ma etim hɔ afebɔɔ.
Monga momwe tinamvera, kotero ife tinaona mu mzinda wa Yehova Wamphamvuzonse, mu mzinda wa Mulungu wathu. Mulungu adzawuteteza kwamuyaya.
9 Wʼasɔredan no mu; Ao, Onyankopɔn, na yɛdwene wo dɔ a enni huammɔ da no ho,
Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu, ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.
10 Ao, Onyankopɔn, wʼayeyi du asase ano te sɛ wo din te; trenee ayɛ wo nsa nifa mu ma.
Monga dzina lanu, Inu Mulungu, matamando anu amafika ku malekezero a dziko lapansi dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.
11 Sion bepɔw di ahurusi, Yuda nkuraase no ani gye esiane wʼatemmu no nti.
Phiri la Ziyoni likukondwera, midzi ya Yuda ndi yosangalala chifukwa cha maweruzo anu.
12 Nantew Sion na twa ho hyia, kan nʼabantenten dodow,
Yendayendani mu Ziyoni, uzungulireni mzindawo, werengani nsanja zake.
13 dwene nʼafasu ho yiye, hwɛ nʼabankɛse no, na woaka ho asɛm akyerɛ nkyirimma.
Yangʼanitsitsani bwino mipanda yake, penyetsetsani malinga ake, kuti mudzafotokoze za izo ku mʼbado wotsatira.
14 Saa Onyankopɔn yi yɛ yɛn Nyankopɔn daa daa; ɔbɛyɛ yɛn kwankyerɛfo akosi awiei mpo. Wɔde ma dwonkyerɛfo.
Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu ku nthawi zosatha; Iye adzakhala mtsogoleri wathu mpaka ku mapeto.

< Nnwom 48 >