< Mmebusɛm 5 >

1 Me ba, yɛ aso ma me nyansa; tie me nhumu nsɛm no yiye,
Mwana wanga, mvetsera bwino za nzeru zimene ndikukuwuzazi, tchera khutu ku mawu odziwitsa bwino zinthu ndikukupatsa,
2 sɛnea ɛbɛma woahwɛ yiye, na wʼano akora nimdeɛ.
kuti uthe kuchita zinthu mochenjera ndi mwanzeru ndiponso kuti utetezedwe ku mayankhulidwe a mkazi wachilendo.
3 Efisɛ ɔbea aguaman ano sosɔ ɛwo, na ne kasa yɛ fɔmm sen ngo;
Pakuti mkazi wachigololo ali ndi mawu okoma ngati uchi. Zoyankhula zake ndi zosalala ngati mafuta,
4 nanso awiei no, ɛyɛ nwen sen bɔnwoma, ɛyɛ nam sɛ afoa anofanu.
koma kotsirizira kwake ngowawa ngati ndulu; ngakuthwa ngati lupanga lakuthwa konsekonse.
5 Nʼanan kɔ owu mu; nʼanammɔntutu kɔ ɔda mu tee. (Sheol h7585)
Mapazi ake amatsikira ku imfa; akamayenda ndiye kuti akupita ku manda. (Sheol h7585)
6 Onsusuw ɔkwan a ɛkɔ nkwa mu ho; nʼakwan yɛ kɔntɔnkye, nanso onnim.
Iye saganizirapo za njira ya moyo; njira zake ndi zokhotakhota koma iye sadziwa izi.
7 Enti afei, me mma, muntie me; Monntwe mo ho mmfi nea meka ho.
Tsopano ana inu, mundimvere; musawasiye mawu anga.
8 Ɔkwan a ɛmmɛn no no na momfa so; mommmɛn ne fi pon ano,
Uziyenda kutali ndi mkazi wotereyo, usayandikire khomo la nyumba yake,
9 anyɛ saa a, mode mo ahoɔden bɛma afoforo na mode mo mfe ama otirimɔdenfo,
kuopa kuti ungadzalanditse ulemerero wako kwa anthu ena; ndi zaka zako kwa anthu ankhanza,
10 anyɛ saa a, ahɔho bɛfom mo ahonyade na mo brɛ de ahonya akɔ afoforo fi.
kapenanso alendo angadyerere chuma chako ndi phindu la ntchito yako kulemeretsa anthu ena.
11 Mo nkwanna akyi, mubesi apini, bere a mo honam ne mo nipadua asa no.
Potsiriza pa moyo wako udzabuwula, thupi lako lonse litatheratu.
12 Na moaka se, “Na mikyi ahohyɛso! Me koma ampɛ nteɛso!
Ndipo udzati, “Mayo ine, ndinkadana ndi kusunga mwambo! Mtima wanga unkanyoza chidzudzulo!
13 Manyɛ osetie amma mʼakyerɛkyerɛfo na mantie me kwankyerɛfo asɛm.
Sindinamvere aphunzitsi anga kapena alangizi anga.
14 Madu ɔsɛe ano wɔ asafo no nyinaa mu.”
Ine ndatsala pangʼono kuti ndiwonongeke pakati pa msonkhano wonse.”
15 Nom nsu fi wʼankasa ahina mu, nsu a ɛteɛ fi wʼankasa abura mu.
Imwa madzi a mʼchitsime chakochako, madzi abwino ochokera mʼchitsime chako.
16 So ɛsɛ sɛ wʼasuti yiri fa mmɔnten so na wo nsuwa kokɔ ɔman aguabɔbea ana?
Kodi akasupe ako azingosefukira mʼmisewu? Kodi mitsinje yako izingoyendayenda mʼzipata za mzinda?
17 Ma ɛnyɛ wo nko ara de, a wo ne ahɔho nkyɛ da.
Mitsinjeyo ikhale ya iwe wekha, osati uyigawireko alendo.
18 Nhyira nka wʼasubura na wʼani nnye wo mmrantebere mu yere ho.
Yehova adalitse kasupe wako, ndipo usangalale ndi mkazi wa unyamata wako.
19 Ɔte sɛ ɔtwe bere dɔfo, ɔwansan nuonyamfo; ma ne nufu nsɔ wʼani daa na ne dɔ nkyekyere wo.
Iye uja ali ngati mbalale yayikazi yokongola ndiponso ngati gwape wa maonekedwe abwino. Ukhutitsidwe ndi mawere ake nthawi zonse, ndipo utengeke ndi chikondi chake nthawi zonse.
20 Me ba, adɛn nti na woma ɔbea aguaman kyekyere wo? Adɛn nti na woda ɔbarima foforo bi yere kokom?
Mwana wanga, nʼchifukwa chiyani ukukopeka ndi mkazi wachigololo? Bwanji ukukumbatira mkazi wachilendo?
21 Awurade hu onipa akwan nyinaa, na ɔhwehwɛ ne nyinaa mu.
Pakuti mayendedwe onse a munthu Yehova amawaona, ndipo Iye amapenyetsetsa njira zake zonse.
22 Omumɔyɛfo nnebɔne sum no afiri; na ne bɔne ahama kyekyere no papee.
Ntchito zoyipa za munthu woyipa zimamukola yekha; zingwe za tchimo lake zimamumanga yekha.
23 Wobewu, esiane ahohyɛso a wonni nti, na wɔayera, esiane wɔn agyennyentwisɛm nti.
Iye adzafa chifukwa chosowa mwambo, adzasocheretsedwa chifukwa cha uchitsiru wake waukulu.

< Mmebusɛm 5 >