< Mmebusɛm 15 >

1 Mmuae pa sianka abufuwhyew, nanso asɛm a ano yɛ den hwanyan abufuw mu.
Kuyankha kofatsa kumathetsa mkwiyo, koma mawu ozaza amautsa ukali.
2 Onyansafo tɛkrɛma yi nimdeɛ ayɛ, nanso ɔkwasea ano woro agyimisɛm.
Munthu wanzeru amayankhula zinthu za nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamatulutsa za uchitsiru.
3 Awurade ani hu baabiara, na ɛhwɛ amumɔyɛfo ne apapafo.
Maso a Yehova ali ponseponse, amayangʼana pa oyipa ndi abwino omwe.
4 Tɛkrɛma a ɛde abodwo ba yɛ nkwadua, nanso nnaadaa tɛkrɛma dwerɛw honhom.
Kuyankhula kodekha kuli ngati mtengo wopatsa moyo, koma kuyankhula kopotoka kumapweteka mtima.
5 Ɔkwasea mfa nʼagya nteɛso nyɛ hwee, na nea otie nteɛso no kyerɛ sɛ ɔyɛ onitefo.
Chitsiru chimanyoza mwambo wa abambo ake, koma wochenjera amasamala chidzudzulo.
6 Ahonya bebree wɔ ɔtreneeni fi, nanso amumɔyɛfo adenya de ɔhaw brɛ wɔn.
Munthu wolungama amakhala ndi chuma chambiri, zimene woyipa amapindula nazo zimamugwetsa mʼmavuto.
7 Anyansafo ano trɛtrɛw nimdeɛ mu, nanso ɛnyɛ saa na nkwaseafo koma te.
Pakamwa pa anthu anzeru pamafalitsa nzeru; koma mitima ya zitsiru sitero.
8 Awurade kyi amumɔyɛfo afɔrebɔ, nanso teefo mpaebɔ sɔ nʼani.
Nsembe za anthu oyipa zimamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi pemphero la anthu owona mtima.
9 Awurade kyi amumɔyɛfo akwan, nanso ɔdɔ wɔn a wotiw trenee.
Ntchito za anthu oyipa zimamunyansa Yehova koma amakonda amene amafunafuna chilungamo.
10 Asotwe dennen wɔ hɔ ma nea ɔman fi ɔkwan no so, nea ɔtan nteɛso no bewu.
Amene amasiya njira yabwino adzalangidwa koopsa. Odana ndi chidzudzulo adzafa.
11 Owu ne Ɔsɛe da Awurade anim, na nnipa koma mu de, onim ma ɛboro so. (Sheol h7585)
Manda ndi chiwonongeko ndi zosabisika pamaso pa Yehova, nanji mitima ya anthu! (Sheol h7585)
12 Ɔfɛwdifo mpɛ nteɛso; onkobisa anyansafo hwee.
Wonyoza sakonda kudzudzulidwa; iye sapita kwa anthu anzeru.
13 Anigye koma ma anim yɛ sereserew, na koma a abotow dwerɛw honhom.
Mtima wokondwa umachititsa nkhope kukhala yachimwemwe, koma mtima wosweka umawawitsa moyo.
14 Nhumufo koma hwehwɛ nimdeɛ, nanso ɔkwasea ano ka agyimisɛm.
Mtima wa munthu wozindikira zinthu umafunafuna nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamadya uchitsiru wawo.
15 Wɔn a wɔhyɛ wɔn so nna nyinaa yɛ mmɔbɔmmɔbɔ, nanso anigye koma wɔ daa ahosɛpɛw mu.
Munthu woponderezedwa masiku ake onse amakhala oyipa, koma mtima wachimwemwe umakhala pa chisangalalo nthawi zonse.
16 Ketewa bi a yenya a Awurade suro ka ho no ye sen ahonyade bebree a ɔhaw bata ho.
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono nʼkumaopa Yehova, kusiyana ndi kukhala ndi chuma chambiri uli pamavuto.
17 Nhabamma aduan a ɔdɔ wɔ mu no ye sen nantwi sradenam a ɔtan bata ho.
Kuli bwino kudyera ndiwo zamasamba pamene pali chikondi, kusiyana ndi kudyera nyama yangʼombe yonenepa pamene pali udani.
18 Nea ne bo fuw ntɛm no de mpaapaemu ba, nanso nea ɔwɔ ntoboase pata ntɔkwaw.
Munthu wopsa mtima msanga amayambitsa mikangano, koma munthu woleza mtima amathetsa ndewu.
19 Nsɔe ama onihawfo kwan asiw, nanso teefo kwan yɛ ɔtempɔn.
Njira ya munthu waulesi ndi yowirira ndi mtengo waminga, koma njira ya munthu wolungama ili ngati msewu waukulu.
20 Ɔba nyansafo ma nʼagya ani gye, nanso ɔba kwasea bu ne na animtiaa.
Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amanyoza amayi ake.
21 Agyimisɛm ma nea onni adwene ani gye, nanso nea ɔwɔ ntease no fa ɔkwan a ɛteɛ so.
Uchitsiru umakondweretsa munthu wopanda nzeru, koma munthu womvetsa zinthu amayenda mowongoka.
22 Nhyehyɛe a enni afotu no sɛe, nanso afotufo bebree ma ɛyɛ yiye.
Popanda uphungu zolinga zako munthu zimalephereka, koma pakakhala aphungu ambiri zolinga zimatheka.
23 Onipa a ɔma mmuae a ɛfata no ani gye, asɛm a ɛba bere pa mu no nso ye.
Munthu amakondwera ndi kuyankha koyenera, ndipo mawu onena pa nthawi yake ndi okoma.
24 Onyansafo asetena mu kwan ma no nkɔso, esiw ne da mukɔ ho kwan. (Sheol h7585)
Munthu wanzeru amatsata njira yopita ku moyo kuti apewe malo okhala anthu akufa. (Sheol h7585)
25 Awurade sɛe ɔhantanni fi, na ɔma akunafo ahye yɛ pɛpɛɛpɛ.
Yehova amapasula nyumba ya munthu wonyada koma amasamalira malo a mkazi wamasiye.
26 Awurade kyi amumɔyɛfo nsusuwii, nanso nʼani sɔ wɔn a wɔyɛ kronkron no de.
Maganizo a anthu oyipa amamunyansa Yehova, koma mawu a anthu oyera mtima amamusangalatsa.
27 Odifudepɛfo de ɔhaw brɛ nʼabusua, nanso nea okyi kɛtɛasehyɛ no benya nkwa.
Munthu wofuna phindu mwachinyengo amavutitsa banja lake, koma wodana ndi ziphuphu adzakhala ndi moyo.
28 Ɔtreneeni koma kari ne mmuae, nanso omumɔyɛfo ano woro bɔne.
Munthu wolungama amaganizira za mmene ayankhire, koma pakamwa pa munthu woyipa pamatulutsa mawu oyipa.
29 Awurade mmɛn amumɔyɛfo koraa, nanso ɔte ɔtreneeni mpaebɔ.
Yehova amakhala kutali ndi anthu oyipa, koma amamva pemphero la anthu olungama.
30 Anim a ɛtew ma koma nya ahomeka, na asɛm pa ma nnompe ahoɔden.
Kuwala kwa maso kumasangalatsa mtima ndipo uthenga wabwino umalimbitsa munthu.
31 Nea otie animka a ɛma nkwa no ne anyansafo bɛbɔ mu atena ase.
Womvera mawu a chidzudzulo amene apatsa moyo adzakhala pakati pa anthu anzeru.
32 Nea ɔmfa ahohyɛso no bu ne ho animtiaa, na nea otie nteɛso no nya nhumu.
Amene amanyoza mwambo amadzinyoza yekha, koma womvera mawu a chidzudzulo amapeza nzeru zomvetsa zinthu.
33 Awurade suro kyerɛ onipa nyansa, ahobrɛase di anuonyam anim.
Kuopa Yehova kumaphunzitsa munthu nzeru, ndipo kudzichepetsa ndi ulemu chili patsogolo ndi kudzichepetsa.

< Mmebusɛm 15 >