< Mmebusɛm 11 >

1 Awurade kyi asisi nsania, na nʼani gye nokware nkaribo ho.
Muyeso wachinyengo Yehova umamunyansa, koma amakondwera ndi muyeso woyenera.
2 Ahantan ba a, animguase na edi so, nanso ahobrɛase de nyansa ba.
Kunyada kukalowa, pamafikanso manyazi, koma pamene pali kudzichepetsa pameneponso pali nzeru.
3 Teefo nokwaredi kyerɛ wɔn kwan; nanso nkontompofo ano ntanta sɛe wɔn.
Ungwiro wa anthu olungama umawatsogolera, koma anthu osakhulupirika amawonongeka ndi chinyengo chawo.
4 Ahonya nka hwee wɔ abufuwhyew da no, nanso trenee gye nkwa fi owu mu.
Chuma sichithandiza pa tsiku lawukali wa Mulungu, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
5 Wɔn a wonni bɔne no trenee bɔ kwan tee ma wɔn, nanso amumɔyɛfo amumɔyɛsɛm brɛ wɔn ase.
Chilungamo cha anthu angwiro chimawongolera moyo wawo, koma ntchito zoyipa zimagwetsa mwini wake yemweyo.
6 Pɛyɛfo treneeyɛ gye wɔn, nanso akɔnnɔ bɔne afiri yi nkontompofo.
Chilungamo cha anthu oyera mtima chimawapulumutsa, koma anthu onyenga adzagwidwa ndi zilakolako zawo zomwe.
7 Sɛ omumɔyɛfo wu a, nʼanidaso yera; nea osusuw sɛ obenya afi ne tumi mu nyinaa no yɛ ɔkwa.
Pamene munthu woyipa wafa, chiyembekezo chake chimathanso. Chiyembekezo cha munthu wosalungama chimawonongeka.
8 Wogye ɔtreneeni fi amane mu, na ɛba omumɔyɛfo so mmom.
Munthu wolungama amapulumutsidwa ku mavuto, koma mʼmalo mwake amagwa mʼmavutomo ndi anthu oyipa.
9 Nea onsuro Onyame de nʼano sɛe ne yɔnko, nanso ɔtreneeni nam nimdeɛ so fi mu.
Munthu wosapembedza amawononga mnansi wake ndi pakamwa pake, koma munthu wolungama amapulumuka chifukwa cha kudziwa zinthu.
10 Sɛ atreneefo di yiye a, kuropɔn no di ahurusi; nanso amumɔyɛfo wu a, wɔbɔ ose.
Anthu olungama zinthu zikamawayendera bwino, mzinda wonse umakondwera, ndipo oyipa akamawonongeka anthu amafuwula mwachimwemwe.
11 Pɛyɛfo nhyira ma kuropɔn no kɔ so, nanso amumɔyɛfo ano ma ɛbɔ.
Mzinda umakwezeka chifukwa cha madalitso a anthu oyera mtima, koma umawonongedwa chifukwa cha pakamwa pa anthu oyipa.
12 Onipa a onni adwene no bu ne yɔnko animtiaa, nanso nea ɔwɔ nhumu no to ne tɛkrɛma nnareka.
Munthu wonyoza mnzake ndi wopanda nzeru, koma munthu wanzeru zomvetsa zinthu amakhala chete.
13 Nsekudi sɛe ahotoso, nanso nea wɔwɔ ne mu ahotoso no kora ahintasɛm.
Amene amanka nachita ukazitape amawulula zinsinsi; koma munthu wokhulupirika amasunga pakamwa pake.
14 Ɔman a enni akwankyerɛ no bɔ, nanso afotufo dodow ma nkonimdi ba.
Pakasoweka uphungu mtundu wa anthu umagwa; koma pakakhala aphungu ambiri pamakhalanso chipulumutso.
15 Nea odi akagyinamu ma ɔfoforo no behu amane, na nea ɔmmfa ne nsa nhyɛ awowasi ase no aso mu dwo no.
Woperekera mlendo chikole adzapeza mavuto, koma wodana ndi za chikole amakhala pa mtendere.
16 Ɔbea a ne yam ye no, wɔde obu ma no, nanso mmarima atirimɔdenfo nya ahode nkutoo.
Mkazi wodekha amalandira ulemu, koma amuna ankhanza amangopata chuma.
17 Ɔyamyefo ye ma ne ho, na otirimɔdenfo de ɔhaw ba nʼankasa so.
Munthu wachifundo amadzipindulira zabwino koma munthu wankhanza amadzibweretsera mavuto.
18 Omumɔyɛfo nya akatua a ennyina, nanso nea ogu trenee aba no twa aba a edi mu.
Munthu woyipa amalandira malipiro wopanda phindu, koma wochita chilungamo amakolola mphotho yeniyeni.
19 Nea ɔyɛ nokware treneeni no nya nkwa, nanso nea ɔkɔ so yɛ bɔne no kɔ owu mu.
Munthu wochita za chilungamo amapeza moyo, koma wothamangira zoyipa adzafa.
20 Awurade kyi nnipa a wɔn koma akyea, na nʼani gye wɔn a wɔn akwan ho nni asɛm no ho.
Yehova amanyansidwa ndi anthu a mtima wokhotakhota koma amakondwera ndi anthu a makhalidwe angwiro.
21 Gye to mu sɛ, amumɔyɛfo benya wɔn akatua, na atreneefo benya wɔn ti adidi mu.
Zoonadi, anthu oyipa adzalangidwa, koma anthu olungama adzapulumuka.
22 Ɔbea hoɔfɛfo a ontumi nsi gyinae no te sɛ sika kaa a ɛhyɛ prako hwene mu.
Monga imaonekera mphete yagolide ikakhala pa mphuno ya nkhumba, ndi momwenso amaonekera mkazi wokongola wamʼkamwa.
23 Atreneefo apɛde wie yiye, nanso amumɔyɛfo anidaso wie abufuwhyew.
Zokhumba za anthu olungama zimathera pa zabwino zokhazokha, koma chiyembekezo cha anthu oyipa chimathera mu ukali wa Mulungu.
24 Obi yɛ adɔe, na onya ne ho bebree; obi nso yɛ pɛpɛe, nanso ehia no.
Munthu wina amapatsako anzake zinthu mwaufulu nʼkumangolemererabe; wina amamana chomwe akanatha kupereka, koma kumanka nasawukabe.
25 Ɔyamyefo bɛkɔ so anya ne ho; na nea ɔma ebinom mee no nso bɛmee.
Munthu wopereka mowolowamanja adzalemera; iye amene amathandiza ena iyenso adzathandizidwa.
26 Nnipa dome nea ɔde atoko sie, na nhyira ba nea ɔtɔn ne de so.
Anthu amatemberera womana anzake chakudya, koma madalitso amakhala pamutu pa munthu amene amagulitsa chakudyacho.
27 Nea ɔhwehwɛ papa akyi kwan no nya anisɔ, na nea ɔhwehwɛ bɔne no, bɔne ba ne so.
Iye amene amafunafuna zabwino mwakhama amapeza zabwinozo, koma wofunafuna zoyipa zidzamupeza.
28 Nea ɔde ne ho to nʼahonyade so no bɛhwe ase, na ɔtreneeni bɛyɛ frɔmfrɔm sɛ ahabammono.
Aliyense amene amadalira chuma chake adzafota, koma wolungama adzaphukira ngati tsamba lobiriwira.
29 Nea ɔde ɔhaw bɛto nʼabusua so no bedi mframa ade, na ɔkwasea bɛyɛ onyansafo somfo.
Wovutitsa a mʼnyumba mwake adzalowa mʼmavuto, ndipo chitsiru chidzakhala kapolo wa munthu wa nzeru.
30 Ɔtreneeni aba yɛ nkwadua, na nea ogye akra no yɛ onyansafo.
Chipatso cha ntchito zabwino ndi moyo, ndipo kusatsata malamulo kumawonongetsa moyo.
31 Kyerɛwsɛm no ka se, “Ɛyɛ den sɛ wobegye onipa pa nkwa; na wɔn a wonnye asɛm no nni ne nnebɔneyɛfo no de, dɛn na ɛbɛba wɔn so?”
Ngati anthu olungama amalandira mphotho zawo pa dziko lapansi, kuli bwanji anthu osapembedza ndi ochimwa!

< Mmebusɛm 11 >