< Mika 5 >

1 Mommoaboa mo asraafo ano, akofo kuropɔn, efisɛ atamfo atwa yɛn ho ahyia. Wɔde abaa bɛbɔ nea odi Israel so no wɔ nʼafono so.
Iwe mzinda wa anthu ankhondo, sonkhanitsa anthu ako ankhondo, pakuti anthu atizungulira kuti alimbane nafe. Adzakantha ndi ndodo pa chibwano cha wolamulira wa Israeli.
2 “Nanso wo, Betlehem Efrata, ɛwɔ mu sɛ woyɛ ketewa wɔ Yuda mmusua mu de, nanso wo mu na obi befi ama me a obedi Israel so, na nʼase fi teteete.”
“Koma iwe Betelehemu Efurata, ngakhale uli wonyozeka pakati pa mafuko a Yuda, mwa iwe mudzatuluka munthu amene adzalamulira Israeli, amene chiyambi chake nʼchakalekale, nʼchamasiku amakedzana.”
3 Enti wobɛto Israelfo paahwii, kosi sɛ ɔbea a awo aka no no bɛwo na ne nuanom mmarima nkae bɛsan akɔka Israelfo ho.
Nʼchifukwa chake Israeli adzasiyidwa mpaka pa nthawi imene mayi amene ali woyembekezera adzachire. Ndipo abale ake onse otsalira adzabwerera kudzakhala pamodzi ndi Aisraeli.
4 Ɔbɛsɔre ahwɛ ne nguankuw wɔ Awurade ahoɔden mu, wɔ Awurade ne Nyankopɔn din kɛseyɛ mu. Na wɔbɛtena asomdwoe mu, na afei ne kɛseyɛ bedu asase awiei.
Iye adzalimbika, ndipo adzaweta nkhosa zake mwa mphamvu ya Yehova, mu ulemerero wa dzina la Yehova Mulungu wake. Ndipo iwo adzakhala mu mtendere, pakuti ukulu wake udzakhala ponseponse pa dziko lapansi.
5 Na ɔbɛyɛ wɔn asomdwoe. Sɛ Asiriafo bɛtow ahyɛ yɛn asase so, na wɔbɔ nsra fa yɛn aban mu a, yɛde nguanhwɛfo baason, mpo asahene baawɔtwe behyia wɔn.
Ndipo Iye adzakhala mtendere wawo. Asiriya akadzalowa mʼdziko lathu ndi kuyamba kuthira nkhondo malo athu otetezedwa, tidzawadzutsira abusa asanu ndi awiri, ngakhalenso atsogoleri asanu ndi atatu.
6 Wɔde afoa bedi Asiria asase so, wɔbɛtwe afoa de adi Nimrod asase so. Sɛ Asiriafo tow hyɛ yɛn so, bɔ nsra fa yɛn ahye so a, obegye yɛn afi wɔn nsam.
Iwo adzagonjetsa dziko la Asiriya ndi lupanga, dziko la Nimurodi adzalilamulira mwankhondo. Adzatipulumutsa kwa Asiriya akadzafika mʼmalire a mʼdziko lathu kudzatithira nkhondo.
7 Yakob asefo nkae no bɛfrafra nnipa bebree mu te sɛ obosu a efi Awurade, te sɛ osu a ɛpete gu sare so a ɛntwɛn ɔdesani, na ɔdesani biara rentumi nsiw ho kwan.
Otsalira a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu yambiri ya anthu ngati mame ochokera kwa Yehova, ngati mvumbi pa udzu, omwe sulamulidwa ndi munthu kapena kudikira lamulo la anthu.
8 Wɔbɛkan Yakob asefo nkae no afra aman no mu, wɔbɛfrafra nnipa bebree mu te sɛ gyata a ɔfra mmoa mu wɔ kwae mu, te sɛ gyata ba a ɔfra nguankuw mu a ɔbobɔ wɔn tetew wɔn mu na obiara ntumi nnye wɔn.
Otsala a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu ya anthu, mʼgulu la anthu a mitundu yambiri, ngati mkango pakati pa nyama za mʼnkhalango. Ngati mwana wa mkango pakati pa gulu la nkhosa, amene pozidutsa amazidya ndi kuzikhadzula, ndipo palibe angathe kuzilanditsa.
9 Wɔbɛma wo nsa so sɛ woadi wʼatamfo so nkonim, na wɔbɛsɛe wʼatamfo nyinaa.
Mudzagonjetsa adani anu, ndipo adani anu onse adzawonongeka.
10 “Saa da no,” sɛnea Awurade se ni, “Mɛsɛe apɔnkɔ a wowɔ na mabubu wo nteaseɛnam.
Yehova akuti, “Tsiku limenelo ndidzawononga akavalo anu onse ndi kuphwasula magaleta anu.
11 Mɛsɛe nkuropɔn a ɛwɔ wʼasase so na madwiriw wo bammɔ dennen nyinaa agu.
Ndidzawononga mizinda ya mʼdziko mwanu ndi kugwetsa malinga anu onse.
12 Mɛsɛe wʼabayisɛm na wo ntafowayi to betwa.
Ndidzawononga ufiti wanu ndipo sikudzakhalanso anthu owombeza mawula.
13 Mɛsɛe nsɛsode a wode wo nsa ayɛ ne abo ahoni a wowɔ no, na worenkotow nsɔre wo nsa ano adwuma bio.
Ndidzawononga mafano anu osema pamodzi ndi miyala yanu yopatulika imene ili pakati panu; simudzagwadiranso zinthu zopanga ndi manja anu.
14 Metutu Asera abosomnnua no afi wo mu na masɛe wo nkuropɔn.
Ndidzazula mitengo ya mafano a Asera imene ili pakati panu, ndipo ndidzawononga mizinda yanu.
15 Aman a wɔantie mʼasɛm no nyinaa, mede abufuw ne abufuwhyew bɛtɔ wɔn so were.”
Ndidzayilanga mwaukali ndi mokwiya mitundu imene sinandimvere Ine.”

< Mika 5 >