< Atemmufo 5 >
1 Da no, Debora ne Abinoam babarima Barak too saa dwom yi:
“Tsiku limenelo Debora ndi Baraki mwana wa Abinoamu anayimba nyimbo iyi:
2 “Israel mpanyimfo sɔre dii anim, na nnipa no de anigye dii wɔn akyi. Nhyira nka Awurade!
“Popeza kuti atsogoleri anatsogoleradi mʼdziko la Israeli; ndipo anthu anadzipereka okha mwa ufulu, tamandani Yehova:
3 “Mo ahemfo, muntie! Monyɛ aso, mo abirɛmpɔn! Na mɛto dwom ama Awurade. Mɛma me nne so ama Awurade, Israel Nyankopɔn.
“Imvani inu mafumu! Tcherani khutu, atsogoleri inu! Ndidzayimba nyimbo, ndidzayimbira Yehova, Mulungu wa Israeli nyimbo yokoma.
4 “Awurade, bere a wufii Seir, na wobɔɔ nsra faa Edom mfuw so no, asase wosowee na ɔsoro omununkum tuee nsu.
“Inu Yehova, pamene munkatuluka mu Seiri, pamene mumayenda kuchokera mʼdziko la Edomu, dziko linagwedezeka, mitambo inasungunuka nigwetsa madzi.
5 Awurade ba no maa mmepɔw wosowee. Sinai Bepɔw mpo wosowee wɔ Awurade, Israel Nyankopɔn anim.
Mapiri anagwedezeka pamaso pa Yehova, Mulungu wa Israeli.
6 “Anat ba Samgar ne Yael bere so, nnipa amfa atempɔn so, na akwantufo faa anammɔnkwan kɔntɔnkye so.
“Pa nthawi ya Samugara mwana wa Anati, pa nthawi ya Yaeli, misewu inasiyidwa; alendo ankangoyenda mʼtinjira takumbali.
7 Nnipa kakra na wɔkaa Israel nkuraa kosii sɛ Debora sɔree sɛ ɛna maa Israel.
Anthu a ku midzi anathawa; mu Israeli munalibe midzi mpaka pamene iwe Debora unafika; unafika ngati mayi ku Israeli.
8 Bere a Israel som anyame foforo no, ɔko sɔree kuropɔn no apon ano. Nanso wɔanhu nkatabo anaa peaw wɔ akofo mpem aduanan a wɔwɔ Israel mu!
Pamene anasankha milungu ina, nkhondo inabwera ku zipata za mzinda, ndipo chishango kapena mkondo sizinapezeke pakati pa anthu 40,000 mu Israeli.
9 Mewɔ Israel ntuanofo afa ne wɔn a wɔde anigye dii wɔn akyi. Hyira Awurade!
Mtima wanga uli ndi atsogoleri a Israeli, uli ndi anthu amene anadzipereka okha mwaufulu pakati pa anthu. Tamandani Yehova!
10 “Mo a motete afurum a wɔte apɔw so, tete nsaa a ɛyɛ fɛ so, muntie! Ne mo a ɛsɛ sɛ monantew fam nso, muntie!
“Inu okwera pa abulu oyera, okhala pa zishalo, ndi inu oyenda pa msewu, yankhulani.
11 Muntie nkuraa nnwontofo a wɔaboa wɔn ho ano wɔ anomee. Wɔkeka Awurade trenee nkonimdi, ne ne nkuraasefo nkonimdi wɔ Israel ho asɛm. “Afei Awurade nkurɔfo bɔɔ nsra kɔɔ kuropɔn no apon ano.
Ku zitsime, kutali ndi phokoso la a mauta; kumeneko akusimba za kuti Yehova wapambana; akusimba kuti Yehova walipsira anthu ake mu Israeli. “Choncho anthu a Yehova anasonkhana ku zipata za mzinda.
12 ‘Sɔre! Debora, sɔre! Sɔre, sɔre na to dwom! Sɔre, Barak! Di wo nneduafo anim kɔ, Abinoam ba!’
Anati, ‘Tsogolera ndiwe, Debora, tsogolera; tsogolera ndiwe, tsogolera, imba nyimbo. Iwe Baraki! nyamuka Tsogolera akapolo ako, iwe mwana wa Abinoamu.’
13 “Nkaefo no bɔɔ nsra fi Tabor kɔɔ ahoɔdenfo so. Awurade nkurɔfo bɔɔ nsra kɔɔ akofo ahoɔdenfo so.
“Kenaka anthu okhulupirika anatsatira atsogoleri awo; anthu a Yehova anapita kukamenyera Yehova nkhondo kulimbana ndi adani amphamvu.
14 Wofi Efraim bae, asase a na kan no na ɛyɛ Amalekfo dea, na Benyamin nso dii wʼakyi. Asahene no bɔɔ nsra fii Makir; ɔsahene pemakurafo fi Sebulon bae.
Anakalowa mʼchigwa kuchokera ku Efereimu; akutsatira iwe Benjamini ndi abale ako. Akulu a ankhondo anachokera ku Makiri, ndipo onyamula ndodo ya udindo anachokera ku Zebuloni.
15 Na Isakar mu atitiriw ka Debora ne Barak ho. Wodii Barak akyi, bɔ wuraa obon no mu. Nanso Ruben abusuakuw mu de, wɔansi wɔn adwene pi.
Olamulira a Isakara anali pamodzi ndi Debora; inde, anthu ochokera ku Isakara anatsatanso Baraki, ndipo anathamangira ku chigwa akumutsatira. Koma pakati pa mafuko a Rubeni panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuchita.
16 Adɛn nti na wotenaa fie wɔ nguanhwɛfo mu, tie nguanhwɛfo a wɔde hwirema frɛ wɔn nguan? Ruben abusuakuw mu, wɔansi wɔn adwene pi.
Chifukwa chiyani munangokhala ku makola a nkhosa nʼkumangomvetsera zitoliro zoyitanira nkhosa? Pakati pa anthu a fuko la Rubeni panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuti achite.
17 Gilead kaa Yordan apuei hɔ. Na Dan de, adɛn nti na ɔtenaa fie? Aser tenaa mpoano a wanka ne ho, ɔkaa nʼahyɛn gyinabea ahorow hɔ.
Agiliyadi anatsala pa tsidya la Yorodani. Ndipo nʼchifukwa chiyani anthu afuko la Dani anatsarira mʼsitima za pa madzi? Aseri anali pa gombe la Nyanja; anangokhala mʼmadooko mwawo.
18 Nanso Sebulon too ne nkwa apemafo sɛnea Naftali yɛɛ wɔ akono no.
Azebuloni ndi anthu amene anayika moyo wawo mʼzoopsa. Nawonso anthu a fuko la Nafutali anayika miyoyo yawo pa chiswe pomenya nkhondo pamwamba pa mapiri.
19 “Kanaan ahemfo koo wɔ Taanak a ɛbɛn Megido asu ho, nanso wɔannya dwetɛ asade biara ankɔ.
“Mafumu anabwera, anachita nkhondo; mafumu Akanaani anachita nkhondo ku Tanaki pafupi ndi madzi a ku Megido, koma sanatengeko zofunkha zasiliva.
20 Nsoromma fi soro koe. Nsoromma nam wɔn akwan so ko tiaa Sisera.
Ngakhalenso nyenyezi zakumwamba zinachita nkhondo, zinathira nkhondo Sisera, zikuyenda mʼnjira zake.
21 Asubɔnten Kison twee wɔn kɔe, tete asu, Kison. Me kra, fa akokoduru bɔ nsra kɔ wʼanim!
Mtsinje wa Kisoni unawakokolola, chigumula cha mtsinje wa Kisoni chinawakokolola. Mtima wanga, yenda mwamphamvu, limbika!
22 Afei, apɔnkɔ no tɔte pempem fam, wɔde mmirikatɛntɛ, Sisera apɔnkɔ ahoɔdenfo no mmirikatɛntɛ.
Ndipo ziboda za ngʼombe zazimuna zinachita phokoso lalikulu, akavalo ali pa liwiro, akuthamanga kwambiri.
23 ‘Nnome nka Merosfo,’ Awurade bɔfo na ose. Ma nnome a ano yɛ den nka wɔn efisɛ wɔammɛboa Awurade, wɔammɛboa Awurade anko antia akofo ahoɔdenfo no.
Mngelo wa Yehova anati ‘Tembererani Merozi.’ ‘Tembererani nzika zake mwaukali, chifukwa sanabwere kudzathandiza Yehova, kulimbana ndi adani ake amphamvu.’
24 “Nhyira nka Yael, Heber a ofi Keni yere. Ne nhyira nsen mmea a wɔtete ntamadan mu nyinaa.
“Akhale wodala kupambana akazi onse, Yaeli mkazi wa Heberi Mkeni; inde mwa akazi onse okhala mʼdziko, akhale wodala iyeyu.
25 Sisera srɛɛ nsu, na Yael maa no nufusu. Kuruwa a ɛfata ahemfo no mu na ɔde nufusu ani srade brɛɛ no.
Munthu uja anapempha madzi akumwa, koma iye anamupatsa mkaka; anamupatsa chambiko mʼchikho cha wolemekezeka.
26 Afei, ɔde ne nsa benkum yii ntamadan pɛe, na ɔde ne nsa nifa faa odwumfo asae. Ɔde bɔɔ Sisera, pɛtɛw ne ti. Ɔde pɛe no wɔɔ ne moma so, bɔɔ so kɔɔ ne tirim.
Anatenga chikhomo cha tenti mʼdzanja lake, anatenganso nyundo ndi dzanja lake lamanja. Ndipo anakhoma nacho Sisera, anamuphwanya mutu wake, ndi kumubowola mu litsipa mwake.
27 Ɔmemee, ɔhwee ase; owui wɔ ne nan ase.
Anathifukira ku mapazi a mkaziyo nagwa, anagwa; iye anagona pamenepo. Anagwera pa mapazi a mkaziyo, iye anagwa; pamene anagwera, pamenepo anaferapo.
28 “Sisera nena hwɛɛ mfɛnsere mu; ɔtɛw mfɛnsere mu hwɛɛ no kwan, ɔkae se, ‘Adɛn nti na ne teaseɛnam akyɛ ba yi? Adɛn nti na yɛnte teaseɛnam nhankare nnyigyei yi?’
“Amayi ake a Sisera anasuzumira pa zenera; nafuwula mokweza kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani galeta lake lachedwa kufika? Nʼchifukwa chiyani phokoso la magaleta ake silikumveka?’
29 Ne mmea anyansafo no rema mmuae no, otii mu kaa saa nsɛm yi kyerɛɛ ne ho se:
Amayi ake anzeru kwambiri anamuyankha, ndithudi, mwiniwake anadziyankha yekha kuti,
30 ‘Wɔrekyɛ asade a wonyae no, ɔbarima biara rennya ɔbea baako anaa baanu. Sisera rennya ntade a ɛyɛ fɛ na me nso merennya ntade a ekura ahosu ahorow na wɔanwen mu fɛfɛ?’
‘Kodi iwo sakufunafuna zofunkha kuti agawane; akugawana wankhondo aliyense mtsikana mmodzi kapena awiri. Sisera akumupatsa zofunkha: zovala zonyikidwa mu utoto, zoti ndizivala mʼkhosi zovala zopeta zonyika mu utoto, ndi zopeta zomavala mʼkhosi?’
31 “Awurade, ma wʼatamfo nyinaa nwu sɛ Sisera! Nanso ma wɔn a wɔdɔ wo no nkɔso sɛ owigyinae.” Afei, asomdwoe baa asase no so mfirihyia aduanan.
“Choncho Yehova! adani anu onse awonongeke, koma iwo amene amakukondani inu akhale ngati dzuwa pamene lituluka ndi mphamvu zake.” Ndipo dziko linakhala pa mtendere zaka makumi anayi.