< Hiob 39 >
1 “So wunim bere a bepɔw so mmirekyi wowo? Woahwɛ, ahu bere a ɔforote nyinsɛn ne ba?
“Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera? Kodi umaonerera pamene nswala ikubala?
2 So woakan asram dodow a wɔde nyinsɛn? Wunim bere a wɔwo ana?
Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere? Kodi nthawi imene zimaswana iwe umayidziwa?
3 Wɔkotow wowo wɔn mma; wɔn awoko yaw to twa.
Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo; pamenepo ululu wobereka nʼkutha.
4 Wɔn mma nyin ahoɔden so wɔ wuram; na wogyaw wɔn awofo hɔ a wɔnnsan nkɔ wɔn nkyɛn bio.
Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo; kenaka amachoka ndipo sabwereranso.
5 “Hena na ɔma wuram afurum fa ne ho di? Hena na ɔsan ne hama?
“Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera? Ndani amamasula zingwe zake?
6 Mede asase kesee maa no sɛ ne fi, ne nkyene asase tamaa sɛ nʼatenae.
Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake, nthaka ya mchere kuti ikhale malo ake okhalamo
7 Ɔserew kurom gyegyeegyeyɛ; na ɔnte ɔkafo nteɛteɛmu.
Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda; ndipo samva kufuwula kwa oyendetsa nyama zakatundu.
8 Okyinkyin mmepɔw no so sɛ ne didibea ɛhɔ na okyin hwehwɛ wura amono biara.
Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu ndipo amafunafuna msipu uliwonse wobiriwira.
9 “Ɛko bɛpene sɛ ɔbɛsom wo ana? Ɔbɛtena wo mmoa adididaka nkyɛn anadwo ana?
“Kodi njati ingavomere kukutumikira? Kodi ingagone mu gome lako usiku?
10 Wubetumi asa no wɔ funtumfiri so ana? Ɔbɛfɛntɛm aku a ɛda wʼakyi no ana?
Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima? Kodi ingasalaze nthumbira mʼmunda mwako?
11 Wubetumi de wo ho ato no so esiane nʼahoɔden dodo nti? Wubegyaw wʼadwuma a ɛyɛ den no ama no ana?
Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake? Kodi ungayilekere kuti igwire ntchito zako zolemetsa?
12 Wugye di sɛ ɔde wʼaburow bɛba na waboa ano de akɔ awiporowbea ana?
Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako ndi kumuyika ku malo opunthira?
13 “Sohori bɔ ne ntaban mu anigye so, nanso wontumi mfa ntoto asukɔnkɔn de ho.
“Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira, koma mapikowo sangafanane ndi mapiko ndi nthenga za kakowa.
14 Ɔtow ne nkesua gu asase so ma mfutuma ka no hyew,
Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi ndipo amafundidwa ndi nthaka,
15 ɛmfa ne ho sɛ ɛnan bi bɛpɛtɛw no, sɛ wuram aboa bi betiatia so.
nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa, ndi kuti nyama zakuthengo zitha kuwaponda.
16 Ɔbɔ ne mma atirimɔden sɛnea wɔnyɛ ne dea; ɛmfa ne ho sɛ nʼadwuma bɛyɛ ɔkwa,
Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake; Imayiwala zoti inavutika powabala.
17 efisɛ Onyankopɔn amma no nyansa wamma no nhumu biara.
Chifukwa Mulungu anayimana nzeru, simvetsa kanthu kalikonse.
18 Nanso sɛ ɔtrɛw ne ntaban mu tu mmirika a, ɔserew ɔpɔnkɔ ne ne sotefo.
Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga, imamusiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.
19 “Wo na woma ɔpɔnkɔ no nʼahoɔden anaa woma ne kɔn mu nwi kuhaa no?
“Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo kapena kumuveka chenjerere mʼkhosi mwake?
20 Wo na woma no huruw te sɛ mmoadabi, na ɔde ne nkotɔ hunahuna ana?
Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira, ukali wake nʼkumachititsa mantha?
21 Ɔde ne nan tintim fam dennen, na nʼani gye nʼahoɔden mu, na afei ɔbɔ wura ɔko mu.
Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake, ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse.
22 Ɔmmɔ hu, na onsuro biribiara; ohu afoa a onguan.
Iye sachita mantha, saopa chilichonse; sabwerera mʼmbuyo akaona lupanga.
23 Bɛmma wosow wɔ ne nkyɛn mu boha mu, na peaw ne pɛmɛ nso di ahim wɔ ne ho.
Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake pamodzi ndi mkondo wonyezimira ndi nthungo.
24 Ofi ahopere mu de nʼano sisi fam; na sɛ wɔhyɛn torobɛnto a ontumi nnyina faako.
Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha; satha kungoyima pamene wamva kulira kwa lipenga.
25 Sɛ torobɛnto hyɛn a ɔka se, ‘Wiɛ!’ ɔte ɔko ho hua fi akyirikyiri, ɔsahene no nteɛmu ne ɔko mu osebɔ.
Lipenga likalira amati, ‘Twee!’ Amamva fungo la nkhondo ali patali, kufuwula kwa anthu olamulira nkhondo ndi mfuwu wankhondo.
26 “Wo nyansa na ɛma akoroma tu na ɔtrɛw ne ntaban mu fa anafo?
“Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako, ndi kutambasula mapiko ake kupita kummwera?
27 Wo na wohyɛ ɔkɔre ma no tu kɔ sorosoro kɔyɛ ne berebuw wɔ hɔ?
Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka ndi kumanga chisa chake pamwamba penipeni?
28 Ɔbotan mu na ɔte na ɛhɔ na ɔda; ɔbotan sorɔnsorɔn yɛ nʼabandennen.
Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku; chimakhala pa msonga penipeni pa mwala.
29 Ɛhɔ na ofi kɔhwehwɛ nʼaduan; nʼani hu ade a ɛwɔ akyirikyiri.
Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye; maso ake amachionera patali chinthucho.
30 Mogya yɛ ne mma aduan, na faako a atɔfo wɔ no, ɛhɔ na ɔwɔ.”
Ana ake amayamwa magazi, ndipo kumene kuli mitembo ndiko chimapezeka.”