< Hiob 32 >

1 Enti saa mmarima baasa yi ammua Hiob bio, efisɛ na ɔteɛ wɔ ɔno ara ani so.
Tsono anthu atatuwa analeka kumuyankha Yobu, chifukwa chakuti iyeyo ankadziona kuti ndi wolungama.
2 Na Busini Barakel babarima Elihu a ofi Ram abusua mu no bo fuw Hiob yiye sɛ obu ne ho bem na ommu Onyankopɔn mmom bem.
Koma Elihu, mwana wa Barakeli, wa fuko la Buzi, wa banja la Ramu, anapsera mtima kwambiri Yobu chifukwa choti Yobuyo anakana kuvomera kuti anachimwa ndi kuti Mulungu anakhoza pomulanga.
3 Ne bo fuw nnamfonom baasa no sɛ wɔantumi anya nnyinaso bi ammɔ Hiob nsɛm no angu, nanso wobuu no fɔ.
Anapseranso mtima abwenzi ake atatu aja chifukwa sanapeze njira yomutsutsira Yobu, ngakhale iwo anamupeza kuti anali wolakwa.
4 Elihu twɛn sɛ afoforo no bɛkasa akyerɛ Hiob, efisɛ na wɔanyinyin sen no.
Tsono Elihu anadikira kuti ayankhule ndi Yobu chifukwa choti abwenziwo anali akuluakulu kupambana iyeyo.
5 Na ohuu sɛ nnipa baasa no nni asɛm biara ka bio no, nʼabufuw no sɔree.
Koma Elihu ataona kuti anthu atatuwo analibe mawu oti ayankhulenso, iye anapsa mtima.
6 Enti Busini Barakel babarima Elihu kae se, “Meyɛ abofra, na moyɛ mpanyimfo; ɛno nti na misuroo sɛ mɛka nea minim akyerɛ mo.
Choncho Elihu mwana wa Barakeli wa fuko la Buzi anati: “Ine ndine wamngʼono, inuyo ndinu akuluakulu, nʼchifukwa chake ndimaopa, ndimachita mantha kuti ndikuwuzeni zimene ndimadziwa.
7 Medwenee sɛ, ‘Ɛsɛ sɛ mpanyimfo kasa; ɛsɛ sɛ wɔn a wɔn ani afi kyerɛ nyansa.’
Ndimaganiza kuti, ‘Ayambe ndi akuluakulu kuyankhula; anthu amvulazakale ndiwo amaphunzitsa nzeru.’
8 Nanso honhom a ɛte onipa mu, Otumfo no home no na ɛma ntease.
Koma mzimu wa Mulungu mwa munthu, mpweya wa Wamphamvuzonse, ndi umene umapereka nzeru zomvetsa zinthu.
9 Ɛnyɛ mpanyimfo nko na wɔyɛ anyansafo, ɛnyɛ wɔn a wɔn ani afi nko na wɔte nea eye ase.
Si okalamba amene ali ndi nzeru, si amvulazakale okha amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu zimene zili zoyenera.
10 “Enti mise: Muntie me; me nso mɛka mʼadwene.
“Nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Mvereni; inenso ndikukuwuzani zimene ndikuzidziwa.’
11 Metwɛn wɔ bere a na morekasa, mitiee mo adwenkyerɛ; bere a na munhu nea monka no,
Ndadikira nthawi yonseyi, ndimamvetsera mwachidwi zimene mumayankhula, pamene mumafunafuna mawu oti muyankhule,
12 meyɛɛ aso maa mo pa ara, nanso mo mu biara antumi ankyerɛ sɛ Hiob ayɛ mfomso; mo mu biara anyi ne nsɛm no ano.
ineyo ndinakumvetseranidi. Koma palibe ndi mmodzi yemwe wa inu amene anatsutsa Yobu; palibe aliyense wa inu amene anamuyankha mawu ake.
13 Monnka se, ‘Yɛahu nyansa; momma Onyankopɔn mmɔ nʼasɛm no ngu, na ɛnyɛ onipa.’
Musanene kuti, ‘Ife tapeza nzeru; Mulungu ndiye amutsutse, osati munthu.’
14 Nanso Hiob nkasa ntia me, na merennyina mo adwenkyerɛ so mmua no.
Koma Yobu sanayankhule motsutsana ndi ine, ndipo ine sindimuyankha monga mmene inu mwamuyankhira.
15 “Wɔn ho adwiriw wɔn, wonni hwee ka bio; wɔn nsɛm asa.
“Iwo asokonezeka ndipo alibe choti ayankhulenso; mawu awathera.
16 So ɛsɛ sɛ metwɛn wɔ bere a wɔayɛ komm yi, saa bere yi a wogyinagyina ha yi a wonni mmuae biara no?
Kodi ine ndidikire chifukwa iwo sakuyankhula tsopano, pakuti angoyima phee wopanda yankho?
17 Me nso mɛka bi me nso mɛka mʼadwene.
Inenso ndiyankhulapo tsopano; nanenso ndinena zimene ndikudziwa.
18 Efisɛ nsɛm ahyɛ mʼanom ma, na honhom a ɛte me mu no hyɛ me sɛ menka;
Pakuti ndili nawo mawu ambiri, ndipo mtima wanga ukundikakamiza;
19 Me mu no, mete sɛ nsa a ɛhyɛ toa mu te sɛ nsa kotoku foforo a ɛrebɛpae.
mʼkati mwanga ndili ngati botolo lodzaza ndi vinyo, ngati matumba a vinyo watsopano amene ali pafupi kuphulika.
20 Ɛsɛ sɛ mekasa na me ho tɔ me; ɛsɛ sɛ mibue mʼano na mema mmuae.
Ndiyenera kuyankhula kuti mtima utsike; ndiyenera kutsekula pakamwa panga ndi kuyankha.
21 Merenyɛ nhwɛanim na merennɛfɛdɛfɛ obiara;
Sindidzakondera munthu wina aliyense, kapena kuyankhula zoshashalika,
22 na sɛ makwadaw adɛfɛdɛfɛ mu a, anka me Yɛfo beyi me afi hɔ ntɛm so.
pakuti ndikanakhala wa luso loyankhula moshashalika, Mlengi wanga akanandilanga msanga.”

< Hiob 32 >