< Hiob 12 >

1 Na Hiob buae se,
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 “Akyinnye nni ho, mo ne nnipa no na muwu a na nyansa asa!
“Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
3 Nanso mewɔ adwene sɛ mo ara monnsen me. Hena na onnim saa nneɛma yi nyinaa?
Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
4 “Mayɛ aserewde ama me nnamfonom, mefrɛɛ Onyankopɔn na obuae, aserewde teta bi, nanso meteɛ na me ho nni asɛm.
“Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
5 Nnipa a wɔn ho tɔ wɔn no bu amanehunu animtiaa sɛnea wobu wɔn a wɔn nan rewatiri no awiei animtiaa no.
Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
6 Wɔmmfa wɔn nsa nka akorɔmfo ntamadan, na wɔn a woyi Onyankopɔn abufuw wɔ bammɔ na Onyankopɔn bɔ nea ɔde ma wɔn ho ban.
Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
7 “Bisa mmoa no, na wɔbɛkyerɛ wo anaasɛ wim nnomaa no, na wɔbɛka akyerɛ wo
“Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
8 anaasɛ kasa kyerɛ asase, na ɛbɛkyerɛ wo, anaasɛ ma po mu mpataa nka nkyerɛ wo.
kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
9 Wɔn nyinaa mu hena na onnim sɛ Awurade nsa na ayɛ eyi.
Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
10 Ne nsam na abɔde nyinaa home wɔ ne adesamma nyinaa home.
Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
11 So aso nsɔ nsɛm nhwɛ sɛnea tɛkrɛma ka aduan hwɛ no ana?
Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
12 Wonnya nyansa mfi mpanyin nkyɛn, na ɛnyɛ onyinkyɛ na ɛde ntease ba ana?
Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
13 “Nyansa ne tumi yɛ Onyankopɔn de; afotu ne ntease yɛ ne dea.
“Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
14 Nea obubu gu no, obiara rentumi nsi; nea ɔde no to afiase no, obiara rentumi nyi no.
Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
15 Sɛ ɔma osu gyae tɔ a, asase no so yɛ wosee; sɛ ogyaa osutɔ mu a, ɛsɛe asase no.
Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
16 Ahoɔden ne nkonimdi yɛ ne de osisifo ne nea wosisi no no nso yɛ ne de.
Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
17 Ɔpa afotufo ho ntama ma wɔkɔ na ɔma atemmufo yɛ nkwasea.
Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
18 Ɔworɔw ahemfo nkyehama na ɔde abɔso bɔ wɔn asen.
Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
19 Ɔpa asɔfo ho ntama, na otu nnipa a wɔn ase atim akyɛ gu.
Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
20 Ɔka afotufo a wogye wɔn di no kasaboa hyɛ, na ogye mpanyimfo nhumu.
Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
21 Ɔde animguase gu atitiriw so na otintim gye ahoɔdenfo nsam akode.
Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
22 Ɔda sum mu nneɛma a ahintaw adi na ɔde sum kabii ba hann mu.
Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
23 Ɔyɛ aman akɛse, na ɔsɛe wɔn; ɔtrɛw aman mu, na ɔhwete wɔn mu.
Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
24 Ogye wiase akannifo adwene fi wɔn nsam; na ɔma wokyinkyin asase wosee a ɔkwan nna so so.
Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
25 Wɔkeka wɔ sum mu a wonni kanea; na ɔma wɔtɔ ntintan sɛ asabowfo.”
Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.

< Hiob 12 >