< Yeremia 30 >

1 Asɛm a efi Awurade nkyɛn baa Yeremia hɔ ni:
Yehova anawuza Yeremiya kuti,
2 “Sɛɛ na Awurade, Israel Nyankopɔn, se: ‘Kyerɛw nsɛm a maka akyerɛ wo nyinaa gu nhoma mu.
“Ine Yehova, Mulungu wa Israeli ndikuti, ‘Lemba mʼbuku mawu onse amene ndakuwuza.
3 Nna bi reba,’ sɛnea Awurade se, ‘a mede me nkurɔfo Israelfo ne Yudafo befi nnommum mu asan aba na mede wɔn aba asase a mede maa wɔn agyanom sɛ wɔmfa ntena so no so,’ Awurade na ose.”
Nthawi ikubwera pamene ndidzachotse anthu anga, Israeli ndi Yuda kuchokera ku ukapolo ndi kuwabwezera dziko limene ndinapatsa makolo awo,’ akutero Yehova.”
4 Eyi ne nsɛm a Awurade ka faa Israel ne Yuda ho:
Nawa mawu amene Yehova anayankhula ndi anthu a ku Israeli ndi Yuda:
5 “Nea Awurade se ni: “‘Akomatu nteɛteɛmu na mete, mete basabasayɛ, na ɛnyɛ asomdwoe.
“Yehova akuti: “Ndamva kulira chifukwa cha nkhawa, ndamva kulira kwa mantha popeza palibe mtendere.
6 Mummisa na munhu: Ɔbarima betumi awo mma ana? Afei, adɛn nti na mihu ɔbarima hoɔdenfo biara sɛ ne nsa gu ne yafunu so te sɛ ɔbea a ɔwɔ awoko mu, na anim biara ayɛ bosaa saa?
Tsono khalani pansi ndi kudzifunsa kuti: Kodi munthu wamwamuna angathe kubereka mwana? Nanga nʼchifukwa chiyani ndikuona munthu aliyense wamwamuna atagwira manja ake pa mimba pake ngati mayi pa nthawi yake yochira? Chifukwa chiyani nkhope iliyonse ili yakugwa?
7 Sɛnea da no bɛyɛ hu afa! Da biara renyɛ sɛ ɛno. Ɛbɛyɛ amanehunu bere ama Yakob, nanso wobeyi no afi mu.
Mayo ine! Tsiku limeneli ndi lalikulu kwambiri! Sipadzakhala lina lofanana nalo. Idzakhala nthawi ya masautso kwa Yakobo, koma adzapulumuka ku masautsowo.”
8 “‘Saa da no,’ Asafo Awurade na ose, ‘Mebubu konnua no afi wɔn kɔn mu, na matetew wɔn nkyehama no mu; ananafo remfa wɔn nyɛ nkoa bio.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Pa tsiku limenelo, ndidzathyola goli la ukapolo mʼkhosi mwawo ndipo ndidzadula zingwe zowamanga; Aisraeli sadzakhalanso akapolo a alendo.
9 Na mmom wɔbɛsom Awurade, wɔn Nyankopɔn ne Dawid, wɔn hene, a mɛpagyaw no ama wɔn.
Mʼmalo mwake, adzatumikira Yehova Mulungu wawo ndiponso Davide mfumu yawo, amene ndidzawasankhira.
10 “‘Enti nsuro, Yakob, me somfo; mma wʼaba mu mmu, Israel,’ nea Awurade se ni. ‘Nokware, megye wo afi akyirikyiri, ne wʼasefo afi wɔn nnommum asase so. Yakob bɛsan anya asomdwoe ne bammɔ na obiara renhunahuna no bio.
“‘Tsono usachite mantha, iwe mtumiki wanga Yakobo; usade nkhawa, iwe Israeli,’ akutero Yehova. ‘Ndithu ndidzakupulumutsa kuchokera ku dziko lakutali, zidzukulu zako kuchokera ku dziko la ukapolo wawo. Yakobo adzabwerera ndipo adzakhala modekha pa mtendere, ndipo palibe amene adzamuchititsa mantha.
11 Me ne wo wɔ hɔ na megye wo nkwa,’ Awurade na ose. ‘Ɛwɔ mu, mesɛe amanaman no nyinaa pasaa, emu na mebɔ mo ahwete kɔ, nanso merensɛe mo korakora. Mɛteɛteɛ mo, nanso mɛyɛ no wɔ trenee kwan so; meremma mo mfa mo ho nni koraa a merentwe mo aso.’
Ine ndili nanu ndipo ndidzakupulumutsani,’ akutero Yehova. ‘Ngakhale ndidzawononga kotheratu mitundu yonse ya anthu kumene ndinakubalalitsirani, koma inu sindidzakuwonongani kotheratu. Sindidzakulekani kuti mukhale osalangidwa. Koma ndidzakulangani mwachilungamo.’”
12 “Sɛɛ na Awurade se: “‘Wʼapirakuru ayɛ akisikuru, na wontumi nsa.
Yehova akuti, “Chilonda chanu nʼchosachizika, bala lanu ndi lonyeka.
13 Obiara nni hɔ a ɔbɛka bi ama wo, wo kuru no rennya aduru, na worennya ayaresa.
Palibe amene angathe kukutetezani pa mlandu wanu, palibe chiyembekezo choti inu nʼkuchira, palibe mankhwala ochiritsa inu.
14 Wʼapamfo nyinaa werɛ afi wo; wo ho biribiara mfa wɔn ho. Mabɔ wo sɛnea wo tamfo bɛyɛ na matwe wʼaso sɛnea otirimɔdenfo bɛtwe, efisɛ wʼafɔdi so dodo na wʼamumɔyɛ nso dɔɔso.
Abwenzi anu onse akuyiwalani; sasamalanso za inu. Ndakukanthani ngati mmene mdani akanachitira. Ndipo ndakulangani mwa nkhanza, chifukwa machimo anu ndi ambiri, ndipo kulakwa kwanu ndi kwakukulu.
15 Adɛn nti na wusu dennen wɔ wʼapirakuru, wo yawdi a ano nni aduru no ho? Wʼafɔdi kɛse ne wʼamumɔyɛ bebrebe nti na mede saa nneɛma yi ayɛ wo.
Chifukwa chiyani mukulira nacho chilonda chanu? Bala lanu silingapole ayi. Ine ndakuchitani zimenezi chifukwa machimo anu ndi ambiri ndipo kulakwa kwanu nʼkwakukulu.
16 “‘Nanso wɔbɛsɛe wɔn a wɔsɛe mo; mo atamfo nyinaa bɛkɔ nnommum mu. Wɔn a wɔfow mo no wɔbɛfow wɔn wɔn a wɔtow hyɛɛ mo so no, mɛtow ahyɛ wɔn so.
“Tsono onse amene anakuwonongani, nawonso adzawonongedwa; adani anu onse adzapita ku ukapolo. Iwo amene anafunkha zinthu zanu, zinthu zawo zidzafunkhidwanso; onse amene anakusakazani nawonso adzasakazidwa.
17 Nanso mɛma wo ahoɔden bio na masa wʼapirakuru,’ Awurade na ose, ‘efisɛ wɔfrɛ wo nea wɔapam no, Sion a wo ho nhia obiara.’”
Ndidzachiza matenda anu ndi kupoletsa zilonda zanu, akutero Yehova, ‘chifukwa mukutchedwa anthu otayika. Amati, ndi anthu a ku Ziyoni awa amene alibe wowasamala.’”
18 Sɛɛ na Awurade se: “‘Mɛsan de Yakob ntamadan mu ahonyade aba na manya ayamhyehye ama nʼatenae ahorow no; wɔbɛkyekye kuropɔn no bio wɔ ne mmubui so, na ahemfi no besi nea ɛsɛ sɛ esi.
Yehova akuti, “Ndidzabwera nalo banja la Yakobo ku dziko lawo ndipo ndidzachitira chifundo malo ake okhalamo; mzinda wa Yerusalemu udzamangidwanso pa bwinja pake, nyumba yaufumu idzamangidwanso pa malo pake penipeni.
19 Wɔn mu na aseda nnwom befi aba ne ahosɛpɛw nnyigyei. Mɛma wɔadɔɔso, na wɔn dodow no so rentew; mɛhyɛ wɔn anuonyam, na wɔremmu wɔn abomfiaa.
Anthuwo adzayimba nyimbo zoyamika Yehova ndipo kudzamveka phokoso lachisangalalo. Ndidzawachulukitsa, ndipo chiwerengero chawo sichidzatsika; ndidzawapatsa ulemerero, ndipo sadzanyozedwanso.
20 Wɔn mma bedi yiye sɛ kan no, mɛma wɔn asafo atim wɔ mʼanim; wɔn a wɔhyɛ wɔn so nyinaa mɛtwe wɔn aso.
Ana awo adzakhalanso monga mmene analili kale, ndipo gulu lawo ndidzalikhazikitsa pamaso panga; ndidzalanga onse owazunza.
21 Wɔn kannifo bɛyɛ wɔn ankasa nipa; na wɔn sodifo befi wɔn mu. Mɛka no abata me ho na wabɛn me, na hena na ɔde ne ho bɛma sɛ ɔbɛbɛn me?’” Awurade na ose.
Mtsogoleri wawo adzakhala mmodzi mwa iwo. Wodzawalamulira adzachokera pakati pawo. Choncho ndidzawakokera kufupi ndi Ine ndipo iye adzandiyandikira. Ndani angalimbe mtima payekha kuyandikana nane popanda kuyitanidwa?” akutero Yehova.
22 “‘Enti mobɛyɛ me nkurɔfo, na mayɛ mo Nyankopɔn.’”
“Choncho inu mudzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wanu.”
23 Hwɛ, Awurade ahum betu abufuwhyew mu, mfɛtɛ bedi kyinhyia wɔ amumɔyɛfo mpampam.
Taonani ukali wa Yehova wowomba ngati mphepo ya mkuntho. Mphepo ya namondwe ikuwomba pa mitu ya anthu oyipa.
24 Awurade abufuw rennwo kosi sɛ obewie ne koma mu nhyehyɛe nyinaa. Nna a ɛreba no mu no mobɛte eyi ase.
Mkwiyo woopsa wa Yehova sudzachoka mpaka atakwaniritsa zolinga za mu mtima mwake. Mudzamvetsa zimenezi masiku akubwerawo.

< Yeremia 30 >