< Yesaia 61 >

1 Otumfo Awurade Honhom wɔ me so, efisɛ, wɔafrɛ me sɛ memmɛka asɛmpa nkyerɛ ahiafo. Wasoma me se, menkɔkyekye wɔn a wɔn koma abubu werɛ, se mempae mu nka ahofadi nkyerɛ nnommum na wonyi nneduafo mfi sum mu,
Mzimu wa Ambuye Yehova uli pa ine, chifukwa Yehova wandidzoza kuti ndilalikire uthenga wabwino kwa anthu osauka. Wandituma kuti ndikatonthoze anthu osweka mtima, ndikalengeze kwa akapolo kuti alandire ufulu ndiponso kuti ndikamasule a mʼndende.
2 se mempae mu nka Awurade adom no ho asɛm, ne yɛn Nyankopɔn aweretɔ da. Wasoma me se, menkyekye wɔn a wodi awerɛhow nyinaa werɛ,
Wandituma kuti ndikalengeze nthawi imene Yehova adzapulumutsa anthu ake; za tsiku limene Yehova adzalanga adani a anthu ake. Wandituma kuti ndikatonthoze olira.
3 na memma wɔn a wodi awerɛhow wɔ Sion no nea wohia, na menhyɛ wɔn ahenkyɛw fɛfɛ nsi nsõ anan mu, anigye ngo nsi awerɛhowdi anan mu, ayeyi atade nsi abasamtu honhom anan mu. Wɔbɛfrɛ wɔn trenee adum nea Awurade adua de ada nʼanuonyam adi.
Wandituma kuti ndiwakonzere olira a ku Ziyoni, nkhata ya maluwa yokongola mʼmalo mwa phulusa, ndiwapatse mafuta achikondwerero mʼmalo mwa kulira. Ndiwapatse chovala cha matamando mʼmalo mwa mtima wopsinjika. Ndipo iwo adzatchedwa mitengo ya thundu yamphamvu yachilungamo, yoyidzala Yehova kuti Iye mwini apezemo ulemerero wake.
4 Wobesi tete mmubui no bio, na wɔasiesie mmeaemmeae a asɛe dedaada no; wɔbɛyɛ nkuropɔn a asɛe no foforo nea asɛe awo ntoatoaso bebree no.
Adzamanganso mabwinja akale a mzinda ndipo malo amene anawonongeka kalekale aja adzakonzanso. Adzakonzanso mizinda imene inapasuka, imene yakhala yowonongeka kwa nthawi yayitali kwambiri.
5 Ananafo bɛhwɛ mo nguankuw; ahɔho bɛyɛ adwuma wɔ mo mfuw ne bobeturo mu.
Anthu achilendo adzakutumikirani; adzazidyetsa ziweto zanu; iwo adzagwira ntchito mʼminda yanu ya mpesa.
6 Na wɔbɛfrɛ mo Awurade asɔfo, wɔbɛto mo din sɛ yɛn Nyankopɔn asomfo. Amanaman no ahonya no na mubedi na wɔn ahode na mode bɛhoahoa mo ho.
Ndipo inu mudzatchedwa ansembe a Yehova, adzakutchulani kuti ndinu atumiki a Mulungu wathu. Mudzadyerera chuma cha mitundu ya anthu, ndipo mudzanyadira ulemu umene mwalandira.
7 Wɔn animguase anan mu me nkurɔfo benya anuonyam mmɔho, na ahohora anan mu wɔbɛsɛpɛw wɔn ho wɔ wɔn adedi mu; ne saa nti wɔn asase no so kyɛfa bɛyɛ mmɔho, na anigye a enni awiei bɛyɛ wɔn dea.
Chifukwa manyazi awo anali owirikiza; ndi kuti munalandira chitonzo ndi kutukwana, adzakondwera ndi cholowa chawo, tsono adzalandira cholowa chawo cha chigawo cha dziko mowirikiza, ndipo chimwemwe chamuyaya chidzakhala chawo.
8 “Na me Awurade, mepɛ atɛntrenee. Mikyi korɔn ne nnebɔne. Me nokware mu, mɛbɔ wɔn aba so na me ne wɔn ayɛ apam a ɛbɛtena hɔ daa.
“Pakuti Ine Yehova, ndimakonda chilungamo; ndimadana ndi zakuba ndi zoyipa. Anthu anga ndidzawapatsa mphotho mokhulupirika ndikupangana nawo pangano losatha.
9 Wɔn asefo begye din wɔ amanaman no mu ne wɔn mma wɔ nkurɔfo no mu. Wɔn a wohu wɔn nyinaa begye ato mu sɛ wɔyɛ nnipa a Awurade ahyira wɔn.”
Ana awo adzakhala odziwika pakati pa mitundu ya anthu ndipo adzukulu awo adzakhala otchuka pakati pa anthu a mitundu ina. Aliyense wowaona adzazindikira kuti ndi anthu amene Yehova wawadalitsa.”
10 Awurade mu na me ho sɛpɛw me mmoroso, me Nyankopɔn mu na me kra di ahurusi. Efisɛ, ɔde nkwagye ntama afura me na ɔde trenee atade yuu awura me, sɛnea ayeforokunu siesie me ti so sɛ ɔsɔfo, ne sɛnea ayeforo de nnwinne hyehyɛ ne ho no.
Ine ndikusangalala kwambiri chifukwa cha Yehova; moyo wanga ukukondwera chifukwa cha Mulungu wanga. Pakuti Iye wandiveka zovala zachipulumutso, ndipo wandiveka mkanjo wachilungamo. Zili ngati mkwati wovala nkhata ya maluwa mʼkhosi mwake, ndiponso ngati mkwatibwi wovala mikanda yamtengowapatali.
11 Na sɛnea asase ma afifide pue na turo nso ma aba nyin no, saa ara na Otumfo Awurade bɛma trenee ne ayeyi apue wɔ amanaman anim.
Monga momwe nthaka imameretsa mbewu ndiponso monga munda umakulitsa mbewu zimene anadzala, momwemonso Ambuye Yehova adzaonetsa chilungamo ndi matamando pamaso pa mitundu yonse ya anthu.

< Yesaia 61 >