< Yesaia 49 >

1 Muntie me, mo mpoano aman; monyɛ aso mo akyirikyiri aman ansa na wɔrebɛwo me no, Awurade frɛɛ me ɔbɔɔ me din ansa na wɔrewo me.
Mverani Ine, inu anthu a pa zilumba tcherani khutu, inu anthu a mayiko akutali: Yehova anandiyitana ine ndisanabadwe, ananditchula dzina ndili mʼmimba ya amayi anga.
2 Ɔyɛɛ mʼano sɛ afoa nnamnam, Ɔde me hintaw ne nsa ase nwini mu; ɔde me yɛɛ agyan a ano yɛ nnam na ɔde me hyɛɛ ne boha mu.
Iye anasandutsa pakamwa panga kukhala ngati lupanga lakuthwa, anandibisa mu mthunzi wa dzanja lake; Iye anandisandutsa ngati muvi wakuthwa ndipo anandibisa mʼchimake.
3 Ɔka kyerɛɛ me se, “Woyɛ me somfo, Israel, wo mu na mɛda mʼanuonyam adi.”
Iye anati kwa ine, “Ndiwe mtumiki wanga, Israeli. Anthu adzanditamanda chifukwa cha iwe.”
4 Nanso mekae se, “Mabrɛ agu masɛe mʼahoɔden kwa, mannya mu hwee nanso nea ɛwɔ me wɔ Awurade nsam na mʼakatua wɔ me Nyankopɔn nkyɛn.”
Koma Ine ndinati, “Ine ndinkaganiza kuti ndinagwira ntchito ndi kuwononga mphamvu zanga pachabe, koma ayi, zondiyenera zili mʼmanja a Yehova, ndipo mphotho yanga ili mʼmanja mwa Mulungu wanga.”
5 Na afei, Awurade kasa se, nea ɔnwen me wɔ awotwaa mu sɛ memmɛyɛ ne somfo sɛ memfa Yakob nsan mmra ne nkyɛn na me mmoaboa Israel ano mma no no, wahyɛ me anuonyam wɔ Awurade ani so na me Nyankopɔn ayɛ mʼahoɔden.
Yehova anandiwumba ine mʼmimba mwa amayi anga kuti ndikhale mtumiki wake kuti ndibweze fuko la Yakobo kwa Iye ndi kusonkhanitsa Israeli kwa Iye, choncho ndimalemekezeka mʼmaso mwa Yehova, ndipo ndimapeza mphamvu mwa Mulungu wanga.
6 Ɔka se, “Ɛyɛ ade ketewa bi ma wo sɛ wobɛyɛ me somfo sɛ wode Yakob mmusuakuw bɛsan aba na wode Israelfo a mede wɔn asie bɛsan aba. Mɛma moayɛ amanamanmufo nyinaa kanea, ɛnam mo so na wobegye wiasefo nyinaa nkwa.”
Yehovayo tsono akuti, “Nʼchinthu chochepa kwambiri kwa iwe kuti ukhale mtumiki wanga, kuti udzutse mafuko a Yakobo ndi kuwabweretsa kwawo Aisraeli amene anapulumuka. Choncho iwe udzakhala ngati chowunikira, udzafikitsa uthenga wa chipulumutso changa ku mathero a dziko lapansi.”
7 Sɛɛ na Awurade se, Ogyefo ne Israel ɔkronkronni no de kɔma nea aman buu no animtiaa na wokyii no, ahemfo somfo no; “Ahene behu wo na wɔasɔre ahenemma behu wo na wɔakotow wo esiane Awurade a ɔyɛ ɔnokwafo, Israel ɔkronkronni a wayi wo no nti.”
Yehova Mpulumutsi ndi Woyerayo wa Israeli akuyankhula, Woyerayo wa Israeli akunena, amene mitundu ya anthu inamuda, amenenso anali kapolo wa mafumu ankhanza uja kuti, “Mafumu adzaona ntchito ya chipulumutso changa ndipo adzayimirira. Akalonga nawonso adzagwada pansi. Zimenezi zidzachitika chifukwa cha Yehova amene ndi wokhulupirika ndi Woyerayo wa Israeli amene wakusankha iwe.”
8 Sɛɛ na Awurade se: “Bere a ɛsɛ mu no, mebua wo, na nkwagyeda no, mɛboa wo; mɛkora wo na mede wo ayɛ apam ama nkurɔfo no, de agye asase no asi hɔ akyekyɛ agyapade ahorow a asɛe no bio,
Yehova akuti, “Pa nthawi imene ndinakukomera mtima ndinakuyankha, ndipo pa tsiku lachipulumutso ndinakuthandiza; ndinakusunga ndi kukusandutsa kuti ukhale pangano kwa anthu, kuti dziko libwerere mwakale ndi kuti cholowa changa chowonongeka chija ndichigawegawenso.
9 wobɛka akyerɛ nneduafo se, ‘Mumfi mmra!’ ne wɔn a wɔwɔ sum mu se, ‘Momfa mo ho nni!’ “Wobedidi wɔ akwan ho wobenya adidibea wɔ koko kesee biara so.
Ndidzawuza a mʼndende kuti atuluke ndi a mu mdima kuti aonekere poyera. “Adzapeza chakudya mʼmphepete mwa njira ndi msipu pa mʼmalo owuma.
10 Ɔkɔm renne wɔn na osukɔm nso renne wɔn; nweatam so hyew ne owia ano hyew renka wɔn, nea ɔwɔ ayamhyehye ma wɔn no bɛkyerɛ wɔn kwan na ɔde wɔn akɔ nsuaniwa ho.
Iwo sadzamva njala kapena ludzu, kutentha kwa mʼchipululu kapena dzuwa silidzawapsereza; chifukwa Iye amene amawachitira chifundo adzawatsogolera ndi kuwaperekeza ku akasupe a madzi.
11 Mɛyɛ me mmepɔw nyinaa akwan, na mʼatempɔn nso mɛma akrɔn.
Mapiri anga onse ndidzawasandutsa njira yoyendamo, ndipo misewu yanga yayikulu ndidzayikweza.
12 Hwɛ, wufi akyirikyiri bɛba ebinom befi atifi fam, ebinom befi atɔe fam ebinom nso befi Sinin mantam mu.”
Taonani, anthu anga adzachokera kutali, ena kumpoto, ena kumadzulo, enanso adzachokera ku chigawo cha Asuwani.”
13 Momfa anigye nteɛ mu, ɔsoro; di ahurusi, asase; mompae mu nnwonto mu, mmepɔw! Na Awurade kyekye ne nkurɔfo werɛ, na obehu nʼamanehunufo mmɔbɔ.
Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga; kondwera, iwe dziko lapansi; imbani nyimbo inu mapiri! Pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake, ndipo wachitira chifundo anthu ake ovutika.
14 Nanso Sion kae se, “Awurade agyaw me hɔ, Awurade werɛ afi me.”
Koma Ziyoni anati, “Yehova wandisiya, Ambuye wandiyiwala.”
15 “Ɛna werɛ betumi afi ne ba a otua nufu ano a ɔrennya ayamhyehye mma ɔba a waturu no no ana? Ebia ne werɛ befi, na me werɛ remfi wo!
“Kodi amayi angathe kuyiwala mwana wawo wakubere ndi kusachitira chifundo mwana amene anabereka iwo eni? Ngakhale iye angathe kuyiwala, Ine sindidzakuyiwala iwe!
16 Hwɛ, makurukyerɛw wo din agu me nsa yam wʼafasu wɔ mʼani so daa.
Taona, ndakulemba iwe mʼzikhantho zanga; makoma ako ndimawaona nthawi zonse.
17 Mo mmabarima resan aba ntɛm so; na wɔn a wɔsɛe mo no refi mo nkyɛn akɔ.
Amisiri odzakumanganso akubwerera mofulumira, ndipo amene anakupasula akuchokapo.
18 Momma mo ani so nhwɛ mo ho nhyia; mo mmabarima nyinaa reboa wɔn ho ano aba mo nkyɛn. Sɛ mete ase yi” sɛnea Awurade se, “mode wɔn bɛyɛ ahyehyɛde ama mo ho mubefura wɔn sɛ ayeforokunu.
Kweza maso ako ndipo uyangʼaneyangʼane ana ako onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe. Yehova akuti, ‘Ine Yehova wamoyo, anthu ako adzakhala ngati chinthu chodzikongoletsa chimene mkwatibwi wavala pa mkono pake.’
19 “Ɛwɔ mu sɛ wɔsɛee mo yɛɛ mo pasaa maa mo asase daa mpan, afei nnipa bɛhyɛ wo so ma, ama aboro wo so, na wɔn a wɔsɛee wo no bɛkɔ akyirikyiri.
“Ngakhale unasanduka bwinja ndi kuwonongedwa ndipo dziko lako ndi kusakazidwa, chifukwa cha kuchuluka kwa anthu malo okhalamo adzakhala operewera ndipo amene anakuwononga iwe aja adzakhala kutali.
20 Mmofra a wɔwoo wɔn wɔ mo nna bɔne mu no bɛka ama moate sɛ, ‘Ɛha sua ma yɛn dodo; momma yɛn asase no bi nka ho na yɛntena so.’
Ana obadwa nthawi yako yachisoni adzanena kuti, ‘Malo ano atichepera, tipatse malo ena woti tikhalemo.’
21 Na wobɛka wɔ wo koma mu se, ‘Hena na ɔwoo eyinom maa me? Na meyɛ ɔwerɛhowni ne obonin; wotuu me kɔɔ asase foforo so na wɔpoo me. Hena na ɔtetew eyinom? Wogyaw me nko ara na eyinom, he na wofi bae?’”
Tsono iwe udzadzifunsa kuti, ‘Kodi ndani anandiberekera ana amenewa? Ana anga onse anamwalira ndipo sindinathenso kukhala ndi ana ena; ndinapita ku ukapolo ndipo ndinachotsedwa. Ndani anawalera ana amenewa? Ndinatsala ndekha, nanga awa, achokera kuti?’”
22 Sɛɛ na Asafo Awurade se: “Hwɛ, menyama amanamanmufo, mɛma me frankaa no so akyerɛ nkurɔfo no wobeturu wo mmabarima wɔ wɔn nsa so aba na wɔbɛsoa wo mmabea wɔ wɔn mmati so.
Zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi, “Taonani, Ine ndidzakodola Anthu a mitundu ina kuti abwere. Ndidzawakwezera anthu a mitundu ina mbendera yanga kuti abwere. Tsono adzabwera ndi ana ako aamuna atawanyamula mʼmanja mwawo ndipo adzanyamula ana ako aakazi pa mapewa awo.
23 Ahemfo bɛyɛ mo agyanom nsiananmu, na wɔn ahemmea ayɛ ɛnanom a wɔbɛhwɛ mo. Wɔbɛkotow mo a wɔn anim butubutuw fam; wɔbɛtaforo mo nan ase mfutuma. Afei mubehu sɛ mene Awurade. Wɔn a wɔn ani da me so no, merenni wɔn huammɔ.”
Mafumu adzakhala abambo wongokulera ndipo akazi a mafumu adzakhala amayi wongokulera. Iwo adzagwetsa nkhope zawo pansi. Ndiye inu mudzazindikira kuti Ine ndine Yehova; iwo amene amadalira Ine sadzakhumudwa.”
24 Wobetumi agye asade afi akofo nsam; anaa wobetumi agye nnommumfo afi otirimɔdenfo nsam?
Kodi mungathe kulanda anthu ankhondo zofunkha zawo, kapena kupulumutsa anthu ogwidwa mʼdzanja la munthu wankhanza?
25 Nanso, sɛɛ na Awurade se: “Yiw, wobegye nnommumfo afi akofo nsam na wɔagye asade afi otirimɔdenfo nsam; me ne wɔn a wɔne wo nya no benya na megye wo mma nkwa.
Koma zimene Yehova akunena ndi izi, “Ankhondo adzawalanda amʼndende awo, ndipo munthu woopsa adzamulanda zofunkha zawo; ndidzalimbana ndi amene amalimbana nanu, ndipo ndidzapulumutsa ana anu.
26 Mema wɔn a wɔhyɛ wo so no awe wɔn ankasa honam; wɔn mogya bɛbow wɔn sɛnea wɔanom nsa. Afei adesamma nyinaa behu sɛ me, Awurade, me ne wʼAgyenkwa no, wo Gyefo, Yakob Tumfo No.”
Anthu amene anakuponderezani adzadya mnofu wawo omwe; adzamwa magazi awo omwe ngati aledzera ndi vinyo. Zikadzatero anthu onse adzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wanu, Momboli wanu, Wamphamvu wa Yakobo.”

< Yesaia 49 >