< Yesaia 16 >

1 Momfa nguantenmma sɛ sonkahiri nkɔma asase no sodifo, efi Sela fa nweatam no so, kɔka Ɔbabea Sion bepɔw no so.
Anthu a ku Mowabu atumiza mphatso za ana ankhosa onenepa, kuchokera ku Sela kudutsa chipululu mpaka kukafika ku phiri la Ziyoni.
2 Te sɛ nnomaa a wɔaka wɔn afi berebuw mu na wotu nenam wim no saa na Moabfo mmea te wɔ Arnon asutwabea.
Monga momwe mbalame zimawulukira uku ndi uku akazimwaza mʼchisa, momwemonso akazi a ku Mowabu akuyendayenda ku madooko a Arinoni.
3 Moab ka se, “Munsi mo adwene pi, monna mo gyinaesi adi. Monyɛ mo sunsuma sɛ anadwo, awia ketee. Momfa aguanfo no nhintaw munnyi atubrafo no mma.
Amowabu aja anawuza a ku Yuda kuti, “Tiwuzeni chochita, gamulani zoti tichite. Inu mutiteteze kwa adani anthu. Mukhale ngati mthunzi wathu dzuwa lili pa liwombo. Mutibise, musatipereke ife othawa nkhondo kwa adani athu.
4 Momma Moabfo aguanfo no ne mo ntena; monyɛ wɔn bammɔ wɔ ɔsɛefo no ho.” Ɔhyɛsoni no bɛba nʼawie na adesɛe to betwa; opoobɔfo no bɛyera wɔ asase no so.
Lolani kuti anthu othawa nkhondo a ku Mowabu azikhala pakati panu; mukhale populumukira pawo kwa wowonongayo.” Nthawi idzafika ndipo wozunzayo sadzakhalaponso, kuwononga kudzaleka; waukaliyo adzachoka mʼdzikomo.
5 Ɔdɔ mu na Onyankopɔn besi ahengua bi; ɔbarima bi de nokwaredi bɛtena so, obi a ofi Dawid fi, nea atemmu mu no ɔpɛ atɛntrenee na ɔntwentwɛn adetreneeyɛ ho.
Mpando waufumu udzakhazikitsidwa mwachikondi; mmodzi mwa zidzukulu za Davide adzakhalapo mokhulupirika. Iyeyo poweruza adzatsata chilungamo ndipo adzalimbikitsa kuchita zachilungamo.
6 Yɛate Moab ahantan a ɔyɛ, nʼani a atra ne ntɔn mmoroso, nʼahomaso ne nʼasoɔden nanso hwee nni nʼahomaso no mu.
Tinamva kuti Mowabu anadzikuza kwambiri. Kunyada kwawo ndi kunyogodola kwawo ndi kudzitama kwawo, zonse ndi zopanda phindu.
7 Enti Moabfo twa adwo, wɔbɔ mu su ma Moab. Wodi awerɛhow na wɔbɔ abubuw, ma Kir Hereset bobe aba ɔfam.
Nʼchifukwa chake Amowabu akulira kwambiri; iwo akulirira dziko lawo. Akubuma momvetsa chisoni chifukwa cha makeke a mphesa a ku Kiri Hareseti.
8 Hesbon mfuw no hyew, Sibma bobe mfuw nso saa ara. Aman sodifo no atiatia bobe papa no so, nea kan na wɔde kɔ Yaser na ɛtrɛtrɛw kɔ nweatam so no. Wɔn mman trɛtrɛw kɔka mpoano pɛɛ.
Minda ya ku Hesiboni yauma, minda ya mpesa ya ku Sibina yaguga. Atsogoleri a mitundu ina anapondaponda minda ya mpesa wabwino, imene nthambi zake zinakafika ku Yazeri, mpaka kutambalalira ku chipululu. Mizu yake inakafika mpaka ku tsidya la nyanja.
9 Enti misu sɛnea Yaser su, de ma Sibma bobe mfuw. Hesbon ne Eleale, mede misu fɔw mo! Mo aduaba a abere ho ahurusi ne otwabere de no aka.
Kotero Ine ndikulira, monga mmene akulirira anthu a ku Yazeri, chifukwa cha minda ya mpesa ya ku Sibima. Inu anthu a ku Hesiboni, inu anthu a ku Eleali, ndikukunyowetsani ndi misozi! Mwalephera kupeza zokolola, chifukwa cha nkhondo imene inawononga zokolola zonse.
10 Ahosɛpɛw ne anigye nni mfikyifuw no mu; obiara nto dwom, na ɔnteɛteɛ mu wɔ bobeturo mu; obiara nkyi nsa wɔ nsakyiamoa so, efisɛ mede nteɛteɛmu aba nʼawiei.
Chimwemwe ndi chisangalalo zalekeka ku minda yanu ya zipatso; palibe amene akuyimba kapena kufuwula mʼminda ya mpesa; palibe amene akupsinya vinyo ku malo opsinyira mphesa, pakuti ndathetsa kufuwula.
11 Misi apini wɔ me koma mu wɔ Moab ho te sɛ sankuten so kwadwom; na me yam hyehye me ma Kir Hereset.
Chifukwa chake moyo wanga ukulira ngati pangwe kulirira Mowabu, mtima wanga ukubuwula chifukwa cha Kiri Hareseti.
12 Sɛ Moab kɔ ne sorɔnsorɔmmea a ɔhaw ne ho kwa; sɛ ɔkɔ nʼabosonnan mu kɔbɔ mpae a, ɛrenkosi hwee.
Ngakhale anthu a ku Mowabu apite ku malo awo achipembedzo koma amangodzitopetsa ndi kutaya nthawi chabe chifukwa sizidzatheka.
13 Eyi ne asɛm a Awurade aka dedaw afa Moab ho.
Awa ndi mawu amene Yehova wayankhula kale zokhudza Mowabu.
14 Nanso mprempren Awurade ka se, “Mfe abiɛsa mu, sɛnea akoa a nhyehyɛe kyekyere no no bebu nna no, wobebu Moab anuonyam ne ne nkurɔfo dodow no nyinaa animtiaa, na ne nkae no bɛyɛ kakraa bi a wonni ahoɔden.”
Koma tsopano Yehova akuti, “Zisanathe zaka zitatu, potsata mʼmene munthu waganyu amawerengera, ulemerero wa Mowabu udzakhala utatheratu ndipo anthu ake ambiri adzakhala atawonongeka, ndipo opulumuka ake adzakhala ochepa ndi ofowoka.”

< Yesaia 16 >