< Zekeriya 7 >

1 Kral Darius'un krallığının dördüncü yılının dokuzuncu ayı olan Kislev ayının dördüncü günü RAB Zekeriya'ya seslendi.
Pa chaka chachinayi cha Mfumu Dariyo, pa tsiku lachinayi la Kisilevi, mwezi wachisanu ndi chinayi, Yehova anayankhula ndi Zekariya.
2 Beytel halkı, Her Şeye Egemen RAB'bin Tapınağı'ndaki kâhinlerle peygamberlere, “Yıllardır yaptığımız gibi beşinci ay oruç tutup ağlayalım mı?” diye sormuş ve RAB'be yalvarmaları için Sareser'i, Regem-Melek'i ve adamlarını göndermişti.
Anthu a ku Beteli anali atatuma Sarezeri ndi Regemu-Meleki pamodzi ndi anthu awo, kuti akapemphe chifundo kwa Yehova
3
pokafunsa kwa ansembe a ku Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse ndi aneneri kuti, “Kodi ine ndizilira ndi kusala zakudya pa mwezi wachisanu, monga mmene ndakhala ndikuchitira pa zaka zambiri?”
4 Her Şeye Egemen RAB bana dedi ki,
Pamenepo Yehova Wamphamvuzonse anayankhula nane kuti,
5 “Bütün ülke halkına ve kâhinlere sor: ‘Yetmiş yıldır beşinci ve yedinci aylarda oruç tutup dövündüğünüzde gerçekten benim için mi oruç tuttunuz?
“Funsa anthu onse a mʼdziko ndi ansembe kuti, ‘Pamene munkasala zakudya pa mwezi wachisanu ndi wachisanu ndi chiwiri pa zaka 70 zapitazi, kodi munkasala chifukwa cha Ine?
6 Yiyip içerken kendiniz için yiyip içmiyor muydunuz?
Ndipo pamene munkadya ndi kumwa, kodi simunkachita zimenezi podzisangalatsa nokha?
7 Yeruşalim'le çevresindeki kentler gönenç içinde yaşarken, Negev ve Şefela insanlarla doluyken, RAB'bin önceki peygamberler aracılığıyla açıkladığı sözler bunlar değil mi?’”
Kodi awa si mawu amene Yehova ankanena kudzera mwa aneneri oyamba aja pamene Yerusalemu ndi mizinda yake yozungulira anali pa mtendere ndi pa ulemerero, ndi pamene Negevi ndi ku madera akumadzulo a mʼmbali mwa phiri munali anthu?’”
8 RAB Zekeriya'ya yine seslendi:
Ndipo Yehova anayankhulanso ndi Zekariya kuti,
9 “Her Şeye Egemen RAB diyor ki, ‘Gerçek adaletle yargılayın; birbirinize sevgi ve sevecenlik gösterin.
“Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Muziweruza molungama; muzichitirana chifundo ndi kumverana chisoni.
10 Dul kadına, öksüze, yabancıya, yoksula baskı yapmayın. Yüreğinizde birbirinize karşı kötülük tasarlamayın.’
Musamazunze akazi amasiye kapena ana amasiye, alendo kapena osauka. Musamaganizirane zoyipa mʼmitima mwanu.’
11 “Ama atalarımız dinlemek istemediler; inatla sırtlarını çevirdiler, duymamak için kulaklarını tıkadılar.
“Koma makolo anu anakana kumvera uthenga umenewu; anawumitsa mtima nandifulatira, natseka makutu awo kuti asamve.
12 Kutsal Yasa'yı ve Her Şeye Egemen RAB'bin kendi Ruhu'yla gönderdiği, önceki peygamberler aracılığıyla ilettiği sözleri dinlememek için yüreklerini taş gibi sertleştirdiler. Bu yüzden Her Şeye Egemen RAB onlara çok öfkelendi.
Anawumitsa mitima yawo ngati mwala wa sangalabwi ndipo sanamvere lamulo kapena mawu amene Yehova Wamphamvuzonse anawatumiza mwa Mzimu wake kudzera mwa aneneri oyamba aja. Kotero Yehova Wamphamvuzonse anakwiya kwambiri.
13 “‘Madem ben çağırınca dinlemediler’ diyor Her Şeye Egemen RAB, ‘Onlar çağırınca, ben de onları dinlemeyeceğim.
“‘Pamene ndinawayitana, iwo sanamvere; choncho pamene iwo anandiyitana, Ine sindinamverenso,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
14 Onları tanımadıkları ulusların arasına fırtına gibi dağıttım. Geride bıraktıkları ülke öyle ıssız kaldı ki, oraya kimse gidip gelemez oldu. Güzelim ülkeyi viraneye çevirdiler.’”
‘Ndinawamwaza ndi kamvuluvulu pakati pa mitundu yonse ya anthu, kumene anali alendo. Dziko lawo linatsala litasakazidwa kwambiri kotero kuti palibe amene amabwera kapena kupitamo. Umu ndi mmene anasandutsira dziko labwino kukhala chipululu.’”

< Zekeriya 7 >