< Ezgiler Ezgisi 8 >

1 Keşke kardeşim olsaydın, Annemin memelerinden süt emmiş. Dışarıda görünce öperdim seni, Kimse de kınamazdı beni.
Ukanakhala kuti ndiwe mlongo wanga, amene anayamwa mawere a amayi anga! Ndikanakumana nawe pa njira, ndikanakupsompsona, ndipo palibe wina aliyense akanandinyoza.
2 Önüne düşer, Beni eğiten Annemin evine götürürdüm seni; Sana baharatlı şarapla Kendi narlarımın suyundan içirirdim.
Ndikanakutenga ndi kukulowetsa mʼnyumba ya amayi anga, amayi amene anandiphunzitsa, ndikanakupatsa vinyo wotsekemera kuti umwe, zotsekemera za makangadza.
3 Sol eli başımın altında, Sağ eli sarsın beni.
Mutu wanga watsamira dzanja lake lamanzere ndipo dzanja lake lamanja landikumbatira.
4 Ant içiriyorum size, ey Yeruşalim kızları! Aşkımı ayıltmayasınız, uyandırmayasınız diye, Gönlü hoş olana dek.
Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani: musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa mpaka pamene chifunire ichocho.
5 Kim bu, Sevgilisine yaslanarak çölden çıkan? Elma ağacı altında uyandırdım seni, Orada doğum sancıları çekti annen, Orada doğum sancıları çekip doğurdu seni.
Kodi ndani uyo akutuluka ku chipululuyo, atatsamira wokondedwa wakeyo? Mkazi Ndinakudzutsa pa tsinde pa mtengo wa apulosi, pamenepo ndi pamene amayi anachirira, pamenepo ndi pamene wokubereka anamva ululu pokubala iweyo.
6 Beni yüreğinin üzerine bir mühür gibi, Kolunun üzerine bir mühür gibi yerleştir. Çünkü sevgi ölüm kadar güçlü, Tutku ölüler diyarı kadar katıdır. Alev alev yanar, Yakıp bitiren ateş gibi. (Sheol h7585)
Undiyike pamtima pako ngati chidindo, ngati chidindo cha pa dzanja lako; pakuti chikondi nʼchamphamvu ngati imfa, nsanje ndiyaliwuma ngati manda. Chikondi chimachita kuti lawilawi ngati malawi a moto wamphamvu. (Sheol h7585)
7 Sevgiyi engin sular söndüremez, Irmaklar süpürüp götüremez. İnsan varını yoğunu sevgi uğruna verse bile, Yine de hor görülür!
Madzi ochuluka sangachizimitse chikondi, mitsinje singachikokolole chikondicho. Ngati wina apereka chuma chonse cha mʼnyumba mwake chifukwa cha chikondi, adzangonyozeka nazo kotheratu.
8 Küçük bir kızkardeşimiz var, Daha memeleri çıkmadı. Ne yapacağız kızkardeşimiz için, Söz kesileceği gün?
Ife tili naye mlongo wathu wamngʼono, koma alibe mawere, kodi tidzamuchitira chiyani mlongo wathuyu pa tsiku limene adzamufunsire?
9 Eğer o bir sursa, Üzerine gümüş mazgallı siper yaparız; Eğer bir kapıysa, Sedir tahtalarıyla onu kaplarız.
Ngati iye ndi khoma, tidzamumangira nsanja ya siliva. Ngati iye ndi chitseko, tidzamutchinga ndi matabwa a mkungudza.
10 Ben bir surum, memelerim de kuleler gibi, Böylece hoşnut eden biri oldum onun gözünde.
Ine ndili ngati khoma, ndipo mawere anga ndi nsanja zake. Tsono mʼmaso mwa bwenzi langa ndine wobweretsa mtendere.
11 Süleyman'ın bağı vardı Baal-Hamon'da, Kiraya verdi bağını; Her biri bin gümüş öderdi ürünü için.
Solomoni anali ndi munda wampesa ku Baala-Hamoni; iyeyo anabwereketsa munda wamphesawo kwa alimi, aliyense mwa iwo ankayenera kupereka ndalama zasiliva 1,000 mʼmalo mwa zipatso zake.
12 Benim bağım kendi emrimde, Bin gümüş senin olsun, ey Süleyman, İki yüz gümüş de ürününe bakan kiracıların.
Koma munda wanga wampesa ndi wangawanga ndiponso wa ine ndekha. Iwe Solomoni, khala nazo ndalama zasiliva 1,000 ndipo ndalama zasiliva 200 ndi za amene akusamalira mundawo.
13 Ey sen, bahçelerde oturan kadın, Arkadaşlar kulak veriyor sesine, Bana da duyur onu.
Iwe amene umakhala mʼminda uli pamodzi ndi anzako, ndilole kuti ndimve liwu lako!
14 Koş, sevgilim, Mis kokulu dağların üzerinde bir ceylan gibi, Geyik yavrusu gibi ol!
Fulumira wokondedwa wanga, ndipo ukhale ngati gwape kapena mwana wa mbawala wothamanga mʼmapiri mʼmene mumamera mbewu zokometsera chakudya.

< Ezgiler Ezgisi 8 >