< Rut 3 >

1 Kaynanası Naomi bir gün Rut'a, “Kızım, iyiliğin için sana rahat edeceğin bir yer aramam gerekmez mi?” dedi.
Tsiku lina Naomi anafunsa mpongozi wake Rute kuti, “Mwana wanga, kodi si kwabwino kuti ndikupezere kokhala kuti zinthu zizikuyendera bwino?
2 “Hizmetçileriyle birlikte bulunduğun Boaz akrabamız değil mi? Bak şimdi, bu akşam Boaz harman yerinde arpa savuracak.
Bowazi amene adzakazi ake wakhala nawo nthawi yonseyi, si wachibale wathu kodi? Usiku uno akhala akupeta barele ku malo opunthira.
3 Yıkan, kokular sürün, giyinip harman yerine git. Ama adam yemeyi içmeyi bitirene dek orada olduğunu belli etme.
Samba ndi kudzola mafuta onunkhira, ndipo uvale zovala zako zabwino kwambiri. Kenaka upite ku malo opunthirako tirigu ndi barele koma munthuyo asakakuzindikire kufikira atamaliza kudya ndi kumwa.
4 Adam yatıp uyuduğunda, nerede yattığını belle; sonra gidip onun ayaklarının üzerindeki örtüyü kaldır ve oracıkta yat. Ne yapman gerektiğini o sana söyler.”
Akamakagona, iwe ukaonetsetse malo amene wagonawo. Kenaka upite ndi kuvundukula chofunda ku mapazi ake ndi kugona. Iyeyo akakuwuza zoti uchite.”
5 Rut ona, “Söylediğin her şeyi yapacağım” diye karşılık verdi.
Rute anayankha kuti, “Ndichita zonse zimene mwanena.”
6 Harman yerine giderek kaynanasının her dediğini yaptı.
Choncho Rute anapita ku malo opunthirawo ndipo anachita monga momwe apongozi ake anamuwuza.
7 Boaz yiyip içti, keyfi yerine geldi. Sonra harman yığınının dibinde uyumaya gitti. Rut da gizlice yaklaştı, onun ayaklarının üzerindeki örtüyü kaldırıp yattı.
Atamaliza kudya ndi kumwa, Bowazi anakhala wosangalala, ndipo anakagona pa mbali pa mulu wa barele. Tsono Rute anapita mwa kachetechete, navundukula chofunda ku mapazi ake ndi kugona.
8 Gece yarısı adam ürktü; yattığı yerde dönünce ayaklarının dibinde yatan kadını ayrımsadı.
Tsono pakati pa usiku Bowazi anadzidzimuka, natembenuka, ndipo anangoona mkazi akugona ku mapazi ake.
9 Ona, “Kimsin sen?” diye sordu. Kadın, “Ben kölen Rut'um” diye yanıtladı. “Kölenle evlen. Çünkü sen yakın akrabamızsın” dedi.
Iye anafunsa kuti, “Ndiwe yani?” Ndipo anayankha kuti, “Ndine mdzakazi wanu Rute. Popeza ndinu wachibale amene muyenera kundiwombola, ndiye mundilowe chokolo.”
10 Boaz, “RAB seni kutsasın, kızım” dedi. “Bu son iyiliğin, ilkinden de büyük. Çünkü yoksul olsun, zengin olsun, gençlerin peşinden gitmedin.
Ndipo Bowazi anati, “Mwana wanga, Yehova akudalitse popeza kukoma mtima kumene wasonyeza panoku kwaposa koyamba kaja. Iwe sunathamangire anyamata olemera kapena osauka.
11 Ve şimdi, korkma kızım; her istediğini yapacağım. Bütün kent halkı senin erdemli bir kadın olduğunu biliyor.
Ndipo tsopano mwana wanga usaope. Ine ndidzakuchitira chilichonse udzapemphe popeza anzanga onse amʼmudzi muno akudziwa kuti ndiwe mkazi wa khalidwe labwino.
12 Yakın akrabanız olduğum doğrudur. Ama benden daha yakın biri var.
Ngakhale kuti ndinedi wachibale woyenera kukusamala, koma alipo wachibale weniweni kuposa ine.
13 Geceyi burada geçir. Sabah olduğunda eğer adam senin için akrabalık görevini yaparsa ne âlâ, varsın yapsın. Ama o, akrabalık görevini yapmak istemezse, yaşayan RAB'be ant içerim ki, bu görevi ben üstlenirim. Sen sabaha kadar yat.”
Gona konkuno usiku uno mpaka mmawa. Tsono ngati iyeyu adzakulowa chokolo, chabwino alowe. Koma ngati safuna kutero, ine ndikulumbira pamaso pa Yehova Wamoyo kuti ndidzakulowa chokolo. Ugone kuno mpaka mmawa.”
14 Böylece Rut sabaha kadar Boaz'ın ayakları dibinde yattı. Ama ortalık insanların birbirini seçebileceği kadar aydınlanmadan önce kalktı. Çünkü Boaz, ‘Harman yerine kadın geldiği bilinmemeli’ demişti.
Choncho Rute anagona ku mapazi ake mpaka mmawa, koma anadzuka mmamawa kusanayere chifukwa Bowazi anati, “Aliyense asadziwe kuti kopondera barele kunabwera mkazi.”
15 Boaz Rut'a, “Sırtındaki şalı çıkar, aç” dedi. Rut şalı açınca Boaz içine altı ölçek arpa boşaltıp onun sırtına yükledi. Sonra Rut kente döndü.
Bowazi anati kwa Rute, “Bwera nacho kuno chofunda wavalacho ndipo uchiyale pansi.” Ndipo atayala, Bowazi anathira makilogalamu makumi awiri a barele ndi kumusenzetsa Rute. Rute anapita nakalowa mu mzinda.
16 Rut geri dönünce kaynanası, “Nasıl geçti kızım?” diye sordu. Rut, Boaz'ın kendisi için yaptığı her şeyi anlattı.
Rute atafika kwa apongozi ake anamufunsa kuti, “Zinayenda bwanji mwana wanga?” Kenaka iye anafotokoza zonse zimene Bowazi anamuchitira.
17 Sonra ekledi: “‘Kaynanana eli boş dönme’ diyerek bana bu altı ölçek arpayı da verdi.”
Ndipo anati, “Munthuyo anandipatsa makilogalamu makumi awiri awa a barele, nandiwuza kuti usapite kwa apongozi ako wopanda kanthu.”
18 Naomi, “Kızım, bu işin ne olacağını öğreninceye kadar evde kal” dedi. “Çünkü Boaz bugün bu işi bitirmeden rahat edemeyecek.”
Kenaka Naomi anati, “Mwana wanga, dikira mpaka titaona mmene zinthu zikhalire chifukwa munthuyu salekera pomwepo, mpaka zinthuzi zitakonzeka lero.”

< Rut 3 >