< Romalilar 2 >

1 Bu nedenle sen, ey başkasını yargılayan insan, kim olursan ol, özrün yoktur. Başkasını yargıladığın konuda kendini mahkûm ediyorsun. Çünkü ey yargılayan sen, aynı şeyleri yapıyorsun.
Choncho, iwe amene umaweruza munthu wina, ulibe pokanira pakuti nthawi iliyonse pamene uweruza wina ukudzitsutsa wekha chifukwa iwe amene umaweruzawe umachitanso zinthu zomwezo.
2 Böyle davrananları Tanrı'nın haklı olarak yargıladığını biliriz.
Tsopano ife tikudziwa kuti chiweruzo cha Mulungu, chotsutsa amene amachita zinthu zotere, nʼchokhazikika pa choonadi.
3 Bu gibi şeyleri yapanları yargılayan, ama aynısını yapan ey insan, Tanrı'nın yargısından kaçabileceğini mi sanıyorsun?
Kodi ukuganiza kuti udzathawa chiweruzo cha Mulungu iwe munthu wamba, pamene uweruza ena, iwe ndi kumachitanso zomwezo?
4 Tanrı'nın sınırsız iyiliğini, hoşgörüsünü, sabrını hor mu görüyorsun? O'nun iyiliğinin seni tövbeye yönelttiğini bilmiyor musun?
Kodi kapena ukupeputsa kukoma mtima kwa Mulungu, kuleza mtima kwake ndi kupirira kwake? Kodi sukuzindikira kuti kukoma mtima kwakeko, nʼkofuna kuti iweyo ulape machimo ako?
5 İnatçılığın ve tövbesiz yüreğin yüzünden Tanrı'nın adil yargısının açıklanacağı gazap günü için kendine karşı gazap biriktiriyorsun.
Koma pakuti ndiwe wosamvera ndi wa mtima wosafuna kulapa, ukudzisungira chilango pa tsiku la mkwiyo wa Mulungu, pamene chiweruzo cholungama cha Mulungu chidzaonetsedwa.
6 Tanrı “herkese, yaptıklarının karşılığını verecektir.”
Mulungu adzabwezera aliyense molingana ndi ntchito zake.
7 Sürekli iyilik ederek yücelik, saygınlık, ölümsüzlük arayanlara sonsuz yaşam verecek. (aiōnios g166)
Iye adzapereka moyo wosatha kwa amene amafunafuna ulemerero, ulemu ndi moyo pochita ntchito zabwino mopirira. (aiōnios g166)
8 Bencillerin, gerçeğe uymayıp haksızlık peşinden gidenlerin üzerineyse gazap ve öfke yağdıracak.
Koma Mulungu adzakhuthulira mkwiyo ndi ukali wake pa amene amachita zofuna zawo ndi kukana choonadi nʼkumatsatira zoyipa.
9 Kötülük eden herkese –önce Yahudi'ye, sonra Yahudi olmayana– sıkıntı ve elem verecek; iyilik eden herkese –yine önce Yahudi'ye, sonra Yahudi olmayana– yücelik, saygınlık, esenlik verecektir.
Masautso ndi zowawa zidzagwera munthu aliyense amene amachita zonyansa, kuyambira Myuda kenaka anthu a mitundu ina.
Koma ulemerero, ulemu ndi mtendere zidzakhala kwa aliyense amene amachita zabwino, kuyambira Myuda kenaka anthu a mitundu ina.
11 Çünkü Tanrı insanlar arasında ayrım yapmaz.
Pajatu Mulungu alibe tsankho.
12 Kutsal Yasa'yı bilmeden günah işleyenler Yasa olmadan da mahvolacaklar. Yasa'yı bildikleri halde günah işleyenlerse Yasa'yla yargılanacaklar.
Onse amene amachimwa osadziwa Malamulo, adzawonongeka ngakhale kuti sadziwa Malamulowo. Ndipo onse amene amachimwa akudziwa Malamulo adzaweruzidwa potsata Malamulowo.
13 Çünkü Tanrı katında aklanacak olanlar Yasa'yı işitenler değil, yerine getirenlerdir.
Pakuti si amene amangomva Malamulo amene amakhala wolungama pamaso pa Mulungu, koma ndi okhawo amene amachita zili mʼMalamulomo amene adzatchedwa olungama.
14 Kutsal Yasa'dan yoksun uluslar Yasa'nın gereklerini kendiliklerinden yaptıkça, Yasa'dan habersiz olsalar bile kendi yasalarını koymuş olurlar.
Ndithu, pamene a mitundu ina, amene alibe Malamulo, koma mwachikhalidwe chawo amachita zimene zili mʼMalamulo, iwowo ndi Malamulo pa iwo okha, ngakhale kuti alibe Malamulowo.
15 Böylelikle Kutsal Yasa'nın gerektirdiklerinin yüreklerinde yazılı olduğunu gösterirler. Vicdanları buna tanıklık eder. Düşünceleriyse onları ya suçlar ya da savunur.
Ntchito zawo zimaonetsa kuti Malamulowo alembedwa mʼmitima mwawo. Chikumbumtima chawonso chimawachitira umboni pakuti maganizo awo amawatsutsa kapena kuwavomereza.
16 Yaydığım Müjde'ye göre Tanrı'nın, insanları gizlice yaptıkları şeylerden ötürü İsa Mesih aracılığıyla yargılayacağı gün böyle olacaktır.
Izi zidzachitika pa tsiku limene Mulungu adzaweruza zinsinsi za anthu kudzera mwa Yesu Khristu, monga momwe Uthenga wanga Wabwino unenera.
17 Ya sen? Kendine Yahudi diyor, Kutsal Yasa'ya dayanıp Tanrı'yla övünüyorsun.
Koma iweyo, amene umadzitcha kuti ndiwe Myuda, umadalira Malamulo, ndipo umanyadira ubale wako ndi Mulungu,
18 Tanrı'nın isteğini biliyorsun. En üstün değerleri ayırt etmeyi Yasa'dan öğrenmişsin.
ngati umadziwa chifuniro chake, ndi kudziwa zoyenera kuchita chifukwa unaphunzitsidwa ndi Malamulo;
19 Kutsal Yasa'da bilginin ve gerçeğin özüne kavuşmuş olarak körlerin kılavuzu, karanlıkta kalanların ışığı, akılsızların eğiticisi, çocukların öğretmeni olduğuna inanmışsın.
ngati umadziwadi kuti ndiwe mtsogoleri wa osaona, nyale yowunikira amene ali mu mdima,
mlangizi wa anthu opusa, mphunzitsi wa makanda, chifukwa umadziwa kuti mʼMalamulo uli nayo nzeru yonse ndi choonadi,
21 Öyleyse başkasına öğretirken, kendine de öğretmez misin? Çalmamayı öğütlerken, çalar mısın?
tsono, iwe amene umaphunzitsa ena, sudziphunzitsa wekha kodi? Kodi iwe amene umalalikira kuti anthu asabe, umabanso?
22 “Zina etmeyin” derken, zina eder misin? Putlardan tiksinirken, tapınakları yağmalar mısın?
Kodi iwe amene umanena kuti anthu asachite chigololo, umachitanso chigololo? Kodi iwe amene umanyasidwa ndi mafano, umalandanso za mʼnyumba zopembedzera mafanowo?
23 Kutsal Yasa'yla övünürken, Yasa'ya karşı gelerek Tanrı'yı aşağılar mısın?
Kodi iwe amene umadzitama ndi Malamulo, umamuchititsa manyazi Mulungu posamvera Malamulowo?
24 Nitekim şöyle yazılmıştır: “Sizin yüzünüzden uluslar arasında Tanrı'nın adına küfrediliyor.”
Monga kwalembedwa, “Dzina la Mulungu likuchitidwa chipongwe pakati pa a mitundu ina chifukwa cha inu.”
25 Kutsal Yasa'yı yerine getirirsen, sünnetin elbet yararı vardır. Ama Yasa'ya karşı gelirsen, sünnetli olmanın hiçbir anlamı kalmaz.
Mdulidwe umakhala ndi phindu ngati usunga Malamulo, koma ngati sumvera Malamulo, iweyo umakhala ngati kuti sunachite mdulidwe.
26 Bu nedenle, sünnetsizler Yasa'nın buyruklarına uyarsa, sünnetli sayılmayacak mı?
Ngati amene sanachite mdulidwe achita zomwe zili mʼMalamulo, kodi sadzatengedwa ngati ochita mdulidwe?
27 Sen Kutsal Yazılar'a ve sünnete sahip olduğun halde Yasa'yı çiğnersen, bedence sünnetli olmayan ama Yasa'ya uyan kişi seni yargılamayacak mı?
Munthu amene sanachite mdulidwe mʼthupi koma amamvera Malamulo adzakutsutsa iwe wosamvera Malamulowe, ngakhale kuti uli nawo Malamulo olembedwawo.
28 Çünkü ne dıştan Yahudi olan gerçek Yahudi'dir, ne de görünüşte, bedensel olan sünnet gerçek sünnettir.
Myuda weniweni si amene angooneka ngati Myuda pamaso pa anthu, ndipo mdulidwe weniweni si umene umangochitika mʼthupi pamaso pa anthu.
29 Ancak içten Yahudi olan Yahudi'dir. Sünnet de yürekle ilgilidir; yazılı yasanın değil, Ruh'un işidir. İçten Yahudi olan kişi, insanların değil, Tanrı'nın övgüsünü kazanır.
Ayi, Myuda weniweni ndi amene ali Myuda mu mtima mwake, ndipo mdulidwe weniweni ndi wa mtima, wochitika ndi Mzimu, osati ndi malamulo olembedwa. Woyamikira munthu wotere ndi Mulungu, osati anthu ayi.

< Romalilar 2 >