< Mezmurlar 95 >

1 Gelin, RAB'be sevinçle haykıralım, Bizi kurtaran kayaya sevinç çığlıkları atalım,
Bwerani, tiyeni timuyimbire Yehova mwachimwemwe, tiyeni tifuwule kwa Thanthwe la chipulumutso chathu
2 Şükranla huzuruna çıkalım, O'na sevinç ilahileri yükseltelim!
Tiyeni tibwere pamaso pake ndi chiyamiko ndipo mupembedzeni Iyeyo ndi zida zoyimbira ndi nyimbo.
3 Çünkü RAB ulu Tanrı'dır, Bütün ilahların üstünde ulu kraldır.
Pakuti Yehova ndi Mulungu wamkulu, mfumu yayikulu pamwamba pa milungu yonse.
4 Yerin derinlikleri O'nun elindedir, Dağların dorukları da O'nun.
Mʼmanja mwake muli maziko ozama a dziko lapansi, ndipo msonga za mapiri ndi zake.
5 Deniz O'nundur, çünkü O yarattı, Karaya da O'nun elleri biçim verdi.
Nyanja ndi yake, pakuti anayilenga ndi Iye, ndipo manja ake anawumba mtunda wowuma.
6 Gelin, tapınalım, eğilelim, Bizi yaratan RAB'bin önünde diz çökelim.
Bwerani, tiyeni tiwerame pomulambira, tiyeni tigwade pamaso pa Yehova Mlengi wathu;
7 Çünkü O Tanrımız'dır, Bizse O'nun otlağının halkı, Elinin altındaki koyunlarız. Bugün sesini duyarsanız,
pakuti Iye ndiye Mulungu wathu ndipo ife ndife anthu a pabusa pake, ndi nkhosa za mʼdzanja lake. Lero ngati inu mumva mawu ake,
8 Meriva'da, o gün çölde, Massa'da olduğu gibi, Yüreklerinizi nasırlaştırmayın.
musawumitse mitima yanu monga momwe munachitira pa Meriba, monga munachitira tsiku lija pa Masa mʼchipululu.
9 Yaptıklarımı görmelerine karşın, Atalarınız orada beni sınayıp denediler.
Kumene makolo anu anandiyesa ndi kundiputa, ngakhale anaona zimene Ine ndinazichita.
10 Kırk yıl o kuşaktan hep iğrendim, “Yüreği kötü yola sapan bir halktır” dedim, “Yollarımı bilmiyorlar.”
Kwa zaka makumi anayi ndinali wokwiya ndi mʼbado umenewo; ndipo ndinati, “Iwo ndi anthu amene mitima yawo imasochera ndipo sanadziwe njira zanga.”
11 Bu yüzden öfkeyle ant içtim: “Huzur diyarıma asla girmeyecekler!”
Choncho ndili chikwiyire, ndinalumbira kuti, “Iwowa sadzalowa ku malo anga a mpumulo.”

< Mezmurlar 95 >