< Mezmurlar 94 >

1 Ya RAB, öç alıcı Tanrı, Saç ışığını, ey öç alıcı Tanrı!
Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.
2 Kalk, ey yeryüzünün yargıcı, Küstahlara hak ettikleri cezayı ver!
Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera.
3 Kötüler ne zamana dek, ya RAB, Ne zamana dek sevinip coşacak?
Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?
4 Ağızlarından küstahlık dökülüyor, Suç işleyen herkes övünüyor.
Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.
5 Halkını eziyorlar, ya RAB, Kendi halkına eziyet ediyorlar.
Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu.
6 Dulu, garibi boğazlıyor, Öksüzleri öldürüyorlar.
Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye.
7 “RAB görmez” diyorlar, “Yakup'un Tanrısı dikkat etmez.”
Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.”
8 Ey halkın içindeki budalalar, dikkat edin; Ey aptallar, ne zaman akıllanacaksınız?
Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?
9 Kulağı yaratan işitmez mi? Göze biçim veren görmez mi?
Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?
10 Ulusları yola getiren yargılamaz mı? İnsanı eğiten bilmez mi?
Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?
11 RAB insanın düşüncelerinin Boş olduğunu bilir.
Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.
12 Ne mutlu, ya RAB, yola getirdiğin, Yasanı öğrettiğin insana!
Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;
13 Kötüler için çukur kazılıncaya dek, Onu sıkıntılı günlerden kurtarıp rahatlatırsın.
mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.
14 Çünkü RAB halkını reddetmez, Kendi halkını terk etmez.
Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake.
15 Adalet yine doğruluk üzerine kurulacak, Yüreği temiz olan herkes ona uyacak.
Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata.
16 Kötülere karşı beni kim savunacak? Kim benim için suçlulara karşı duracak?
Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?
17 RAB yardımcım olmasaydı, Şimdiye dek sessizlik diyarına göçmüştüm bile.
Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.
18 “Ayağım kayıyor” dediğimde, Sevgin ayakta tutar beni, ya RAB.
Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.
19 Kaygılar içimi sarınca, Senin avutmaların gönlümü sevindirir.
Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.
20 Yasaya dayanarak haksızlık yapan koltuk sahibi Seninle bağdaşır mı?
Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?
21 Onlar doğruya karşı birleşiyor, Suçsuzu ölüme mahkûm ediyorlar.
Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.
22 Ama RAB bana kale oldu, Tanrım sığındığım kaya oldu.
Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.
23 Tanrımız RAB yaptıkları kötülüğü Kendi başlarına getirecek, Kötülükleri yüzünden köklerini kurutacak, Evet, köklerini kurutacak.
Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.

< Mezmurlar 94 >