< Mezmurlar 74 >

1 Asaf'ın Maskili Ey Tanrı, neden bizi sonsuza dek reddettin? Niçin otlağının koyunlarına karşı öfken tütmekte?
Ndakatulo ya Asafu. Nʼchifukwa chiyani mwatitaya ife kwamuyaya, Inu Mulungu? Chifukwa chiyani mkwiyo wanu ukutukutira pa nkhosa za busa lanu?
2 Anımsa geçmişte sahiplendiğin topluluğu, Kendi halkın olsun diye kurtardığın oymağı Ve üzerine konut kurduğun Siyon Dağı'nı.
Kumbukirani anthu amene munawagula kalekale, fuko la cholowa chanu, limene Inu munaliwombola, phiri la Ziyoni, kumene inuyo mumakhala.
3 Yönelt adımlarını şu onarılmaz yıkıntılara doğru, Düşman kutsal yerdeki her şeyi yıktı.
Tembenuzani mapazi kuloza ku mabwinja awa amuyaya chiwonongeko ichi chonse mdani wabweretsa pa malo opatulika.
4 Düşmanların bizimle buluştuğun yerde kükredi, Zafer simgesi olarak kendi bayraklarını dikti.
Adani anu anabangula pa malo pamene Inu munkakumana nafe; anayimika mbendera zawo monga zizindikiro zachigonjetso.
5 Gür bir ormana Baltayla dalar gibiydiler.
Iwo anachita ngati anthu oti anyamula mbendera zawo kuti adule mitengo mʼnkhalango.
6 Baltayla, balyozla kırdılar, Bütün oymaları.
Kenaka anaphwanya ndi nkhwangwa ndi akasemasema awo zonse zimene tinapachika.
7 Ateşe verdiler tapınağını, Yerle bir edip kutsallığını bozdular Adının yaşadığı konutun.
Iwo anatentha malo anu opatulika mpaka kuwagwetsa pansi; anadetsa malo okhalamo dzina lanu.
8 İçlerinden, “Hepsini ezelim!” dediler. Ülkede Tanrı'yla buluşma yerlerinin tümünü yaktılar.
Ndipo anati mʼmitima yawo, “Tawatha kwathunthu.” Anatentha malo aliwonse amene Mulungu amapembedzedwerako mʼdzikomo.
9 Artık kutsal simgelerimizi görmüyoruz, Peygamberler de yok oldu, İçimizden kimse bilmiyor ne zamana dek...
Ife sitinapatsidwe chizindikiro chodabwitsa; palibe aneneri amene atsala ndipo palibe aliyense wa ife akudziwa kuti izi zidzatenga nthawi yayitali bwanji.
10 Ey Tanrı, ne zamana dek düşman sana sövecek, Hasmın senin adını hor görecek?
Kodi mpaka liti, mdani adzanyoze Inu Mulungu? Kodi amaliwongowa adzapeputsa dzina lanu kwamuyaya?
11 Niçin geri çekiyorsun elini? Çıkar sağ elini bağrından, yok et onları!
Chifukwa chiyani mukubweza dzanja lanu lamanja? Litulutseni kuchoka pachifuwa chanu ndipo muwawononge!
12 Ama geçmişten bu yana kralım sensin, ey Tanrı, Yeryüzünde kurtuluş sağladın.
Koma Inu Mulungu, ndinu Mfumu yanga kuyambira kalekale; Mumabweretsa chipulumutso pa dziko lapansi.
13 Gücünle denizi yardın, Canavarların kafasını sularda parçaladın.
Ndinu amene munagawa nyanja ndi mphamvu yanu; munathyola mitu ya zirombo za mʼmadzi.
14 Livyatan'ın başlarını ezdin, Çölde yaşayanlara onu yem ettin.
Ndinu amene munaphwanya mitu ya Leviyatani ndi kuyipereka ngati chakudya cha zirombo za mʼchipululu.
15 Kaynaklar, dereler fışkırttın, Sürekli akan ırmakları kuruttun.
Ndinu amene munatsekula akasupe ndi mitsinje, munawumitsa mitsinje imene siphwa nthawi zonse.
16 Gün senindir, gece de senin, Ay ve güneşi sen yerleştirdin,
Masana ndi anu ndipo usiku ndi wanunso; Inuyo munakhazikitsa dzuwa ndi mwezi.
17 Yeryüzünün bütün sınırlarını sen saptadın, Yazı da kışı da yaratan sensin.
Ndinu amene munakhazikitsa malire onse a dziko lapansi; munakhazikitsa chilimwe ndi dzinja.
18 Anımsa, ya RAB, düşmanın sana nasıl sövdüğünü, Akılsız bir halkın, adını nasıl hor gördüğünü.
Kumbukirani momwe mdani wakunyozerani Inu Yehova, momwe anthu opusa apeputsira dzina lanu.
19 Canavara teslim etme kumrunun canını, Asla unutma düşkün kullarının yaşamını.
Musapereke moyo wa nkhunda yanu ku zirombo zakuthengo; nthawi zonse musayiwale miyoyo ya anthu anu osautsidwa.
20 Yaptığın antlaşmayı gözönüne al, Çünkü ülkenin her karanlık köşesi Zorbaların inleriyle dolmuş.
Mukumbukire pangano lanu, pakuti malo obisika a mʼdziko asanduka mochitira zachiwawa zochuluka.
21 Düşkünler boynu bükük geri çevrilmesin, Mazlumlar, yoksullar adına övgüler dizsin.
Musalole kuti osautsidwa abwerere mwamanyazi; osauka ndi osowa atamande dzina lanu.
22 Kalk, ey Tanrı, davanı savun! Anımsa akılsızların gün boyu sana nasıl sövdüğünü!
Dzukani Inu Mulungu ndipo dzitetezeni pa mlandu; kumbukirani momwe opusa akukunyozerani tsiku lonse.
23 Unutma hasımlarının yaygarasını, Sana başkaldıranların durmadan yükselen patırtısını!
Musalekerere phokoso la otsutsana nanu, chiwawa cha adani anu, chimene chikumveka kosalekeza.

< Mezmurlar 74 >