< Mezmurlar 58 >

1 Müzik şefi için - “Yok Etme” makamında Davut'un Miktamı Ey yöneticiler, gerçekten adil mi karar verirsiniz? Doğru mu yargılarsınız insanları?
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Kodi inu olamulira mumayankhuladi molungama? Kodi mumaweruza mwachilungamo pakati pa anthu?
2 Hayır! Hep haksızlık tasarlarsınız içinizde, Zorbalık saçar elleriniz yeryüzüne.
Ayi, mʼmitima mwanu mumakonzekera zosalungama, ndipo manja anu amatulutsa zachiwawa pa dziko lapansi.
3 Kötüler daha ana rahmindeyken yoldan çıkar, Doğdu doğalı yalan söyleyerek sapar.
Ngakhale kuchokera tsiku lawo lobadwa oyipa amasochera; kuchokera mʼmimba ya amayi awo, iwo ndi otayika ndipo amayankhula mabodza.
4 Zehirleri yılan zehiri gibidir. Kulakları tıkalı bir kobrayı andırırlar,
Ululu wawo uli ngati ululu wa njoka, ngati uja wa mphiri imene yatseka mʼmakutu mwake.
5 Usta büyücülerin, Afsuncuların sesini duymak istemeyen bir kobrayı.
Imene simva liwu la munthu wamatsenga, ngakhale akhale wa luso lotani munthu wamatsengayo.
6 Ey Tanrı, kır onların ağzında dişlerini, Sök genç aslanların azı dişlerini, ya RAB!
Gululani mano mʼkamwa mwawo, Inu Mulungu, Yehova khadzulani mano a mikango!
7 Akıp giden su gibi yok olsunlar. Yaylarını gerince oklarının ucu kırılsın.
Mulole kuti asowe ngati madzi oyenda pamene iwo akoka uta mulole kuti mivi yawo ikhale yosathwa.
8 Süründükçe eriyen sümüklüböceğe dönsünler. Düşük çocuk gibi güneş yüzü görmesinler.
Akhale ngati nkhono imene imasungunuka pamene ikuyenda; ngati mwana wakufa asanabadwe, iwo asaone dzuwa.
9 Kazanlarınız diken ateşini daha duymadan, Yaşı da kurusu da kasırgayla savrulacak kötülerin.
Miphika yanu isanagwire moto waminga ya mkandankhuku, kaya iyo ndi yobiriwira kapena yowuma, oyipa adzachotsedwa.
10 Doğru adam alınan öcü görünce sevinecek Ve ayaklarını kötünün kanında yıkayacak.
Olungama adzasangalala poona kubwezera chilango, pamene adzasambitsa mapazi awo mʼmagazi a anthu oyipa.
11 O zaman insanlar, “Gerçekten doğrulara ödül var” diyecek, “Gerçekten dünyayı yargılayan bir Tanrı var.”
Ndipo anthu adzanena kuti, “Zoonadi, olungama amalandirabe mphotho; zoonadi kuli Mulungu amene amaweruza dziko lapansi.”

< Mezmurlar 58 >