< Mezmurlar 57 >
1 Müzik şefi için - “Yok Etme” makamında Davut'un Miktamı - Saul'dan kaçıp mağaraya sığındığı zaman Acı bana, ey Tanrı, acı, Çünkü sana sığınıyorum; Felaket geçinceye kadar, Kanatlarının gölgesine sığınacağım.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide, pamene anathawa Sauli kupita ku phanga. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu mundichitire chifundo, pakuti mwa Inu moyo wanga umathawiramo. Ndidzathawira mu mthunzi wa mapiko anu mpaka chiwonongeko chitapita.
2 Yüce Tanrı'ya, Benim için her şeyi yapan Tanrı'ya sesleniyorum.
Ine ndikufuwulira kwa Mulungu Wammwambamwamba, kwa Mulungu amene amakwaniritsa cholinga chake pa ine.
3 Gökten gönderip beni kurtaracak, Beni ezmek isteyenleri azarlayacak, (Sela) Sevgisini, sadakatini gösterecektir.
Mulungu amanditumizira kuchokera kumwamba ndi kundipulumutsa, kudzudzula iwo amene akundithamangitsa kwambiri. Mulungu amatumiza chikondi chake ndi kukhulupirika kwake.
4 Aslanların arasındayım, Alev kusan insanlar arasında yatarım, Mızrak gibi, ok gibi dişleri, Keskin kılıç gibi dilleri.
Ine ndili pakati pa mikango, ndagona pakati pa zirombo zolusa; anthu amene mano awo ndi milomo yawo ndi mivi, malilime awo ndi malupanga akuthwa.
5 Yüceliğini göster göklerin üstünde, ey Tanrı, Görkemin bütün yeryüzünü kaplasın!
Mukwezekedwe Inu Mulungu, kuposa mayiko onse akumwamba; mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
6 Ayaklarım için ağ serdiler, Çöktüm; Yoluma çukur kazdılar, İçine kendileri düştüler. (Sela)
Iwo anatchera mapazi anga ukonde ndipo ndinawerama pansi mosautsidwa. Anakumba dzenje mʼnjira yanga koma agweramo okha mʼmenemo.
7 Kararlıyım, ey Tanrı, kararlıyım, Ezgiler, ilahiler söyleyeceğim.
Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu mtima wanga ndi wokhazikika. Ndidzayimba nyimbo, nyimbo yake yamatamando.
8 Uyan, ey canım, Uyan, ey lir, ey çenk, Seheri ben uyandırayım!
Dzuka moyo wanga! Dzukani zeze ndi pangwe! Ndidzadzuka mʼbandakucha.
9 Halkların arasında sana şükürler sunayım, ya Rab, Ulusların arasında seni ilahilerle öveyim.
Ndidzakutamandani Ambuye, pakati pa mitundu ya anthu, ndidzayimba za Inu pakati pa mayiko.
10 Çünkü sevgin göklere erişir, Sadakatin gökyüzüne ulaşır.
Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kufikira ku mayiko akumwamba; kukhulupirika kwanu kwafika ku mitambo.
11 Yüceliğini göster göklerin üstünde, ey Tanrı, Görkemin bütün yeryüzünü kaplasın!
Mukwezekedwe Inu Mulungu kuposa mayiko akumwamba, mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.