< Mezmurlar 53 >
1 Müzik şefi için - Mahalat makamında Davut'un Maskili Akılsız içinden, “Tanrı yok!” der. İnsanlar bozuldu, iğrençlik aldı yürüdü, İyilik eden yok.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Mahalati. Ndakatulo ya Davide. Chitsiru chimati mu mtima mwake, “Kulibe Mulungu.” Iwo ndi oyipa ndipo njira zawo ndi zonyansa; palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino.
2 Tanrı göklerden bakar oldu insanlara, Akıllı, Tanrı'ya yönelen biri var mı diye.
Mulungu kumwamba amayangʼana pansi pano pa ana a anthu kuti aone ngati alipo wina wanzeru, wofunafuna Mulungu.
3 Hepsi saptı, Tümü yozlaştı, İyilik eden yok, Bir kişi bile!
Aliyense wabwerera, iwo onse pamodzi akhala oyipa; palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino, ngakhale mmodzi.
4 Suç işleyenler görmüyor mu? Halkımı ekmek yer gibi yiyor, Tanrı'ya yakarmıyorlar.
Kodi anthu ochita zoyipawa adzaphunziradi; anthu amene amadya anthu anga monga mmene anthu amadyera buledi, ndipo sapemphera kwa Mulungu?
5 Ama korkulmayacak yerde korkacaklar, Çünkü Tanrı seni kuşatanların kemiklerini dağıtacak, Onları reddettiği için hepsini utandıracak.
Iwo anali pamenepo atathedwa nzeru ndi mantha aakulu pamene panalibe kanthu kochititsa mantha. Mulungu anamwazamwaza mafupa a anthu amene anakuthirani nkhondo; inuyo munawachititsa manyazi, pakuti Mulungu anawanyoza.
6 Keşke İsrail'in kurtuluşu Siyon'dan gelse! Tanrı halkını eski gönencine kavuşturunca, Yakup soyu sevinecek, İsrail halkı coşacak.
Ndithu, chipulumutso cha Israeli nʼchochokera ku Ziyoni! Pamene Mulungu adzabwezeretsanso ulemerero wa anthu ake, lolani Yakobo akondwere ndi Israeli asangalale!