< Mezmurlar 49 >
1 Müzik şefi için - Korahoğulları'nın mezmuru Ey bütün halklar, dinleyin! Kulak verin hepiniz, ey dünyada yaşayanlar,
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Imvani izi anthu a mitundu yonse; mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse,
2 Halk çocukları, bey çocukları, Zenginler, yoksullar!
anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika, olemera pamodzinso ndi osauka:
3 Bilgelik dökülecek ağzımdan, Anlayış sağlayacak içimdeki düşünceler,
Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru; mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.
4 Kulak vereceğim özdeyişlere, Lirle yorumlayacağım bilmecemi.
Ndidzatchera khutu langa ku mwambo, ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.
5 Niçin korkayım kötü günlerde Niyeti bozuk düşmanlarım çevremi sarınca?
Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika, pamene achinyengo oyipa andizungulira.
6 Onlar varlıklarına güvenir, Büyük servetleriyle böbürlenirler.
Iwo amene adalira kulemera kwawo ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?
7 Kimse kimsenin hayatının bedelini ödeyemez, Tanrı'ya fidye veremez.
Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu.
8 Çünkü hayatın fidyesi büyüktür, Kimse ödemeye yeltenmemeli.
Dipo la moyo ndi la mtengowapatali, palibe malipiro amene angakwanire,
9 Böyle olmasa, Sonsuza dek yaşar insan, Mezar yüzü görmez.
kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya ndi kusapita ku manda.
10 Kuşkusuz herkes biliyor bilgelerin öldüğünü, Aptallarla budalaların yok olduğunu. Mallarını başkalarına bırakıyorlar.
Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira; opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena.
11 Mezarları, sonsuza dek evleri, Kuşaklar boyu konutları olacak, Topraklarına kendi adlarını verseler bile.
Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya, malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo, ngakhale anatchula malo mayina awo.
12 Bütün gösterişine karşın geçicidir insan, Ölüp giden hayvanlar gibi.
Ngakhale munthu akhale wachuma chotani, adzafa ngati nyama.
13 Budalaların yolu, Onların sözünü onaylayanların sonu budur. (Sela)
Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha, ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula. (Sela)
14 Sürü gibi ölüler diyarına sürülecekler, Ölüm güdecek onları. Tan ağarınca doğrular onlara egemen olacak, Cesetleri çürüyecek, Ölüler diyarı onlara konut olacak. (Sheol )
Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda, ndipo imfa idzawadya. Olungama adzawalamulira mmawa; matupi awo adzavunda mʼmanda, kutali ndi nyumba zawo zaufumu. (Sheol )
15 Ama Tanrı beni Ölüler diyarının pençesinden kurtaracak Ve yanına alacak. (Sela) (Sheol )
Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda; ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini. (Sheol )
16 Korkma biri zenginleşirse, Evinin görkemi artarsa.
Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera, pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira;
17 Çünkü ölünce hiçbir şey götüremez, Görkemi onunla mezara gitmez.
Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira, ulemerero wake sudzapita pamodzi naye.
18 Yaşarken kendini mutlu saysa bile, Başarılı olunca övülse bile.
Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala, ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino,
19 Atalarının kuşağına katılacak, Onlar ki asla ışık yüzü görmeyecekler.
iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake, amene sadzaonanso kuwala.
20 Bütün gösterişine karşın anlayışsızdır insan, Ölüp giden hayvanlar gibi.
Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru adzafa ngati nyama yakuthengo.