< Mezmurlar 47 >

1 Müzik şefi için - Korahoğulları'nın mezmuru Ey bütün uluslar, el çırpın! Sevinç çığlıkları atın Tanrı'nın onuruna!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Ombani mʼmanja, inu anthu onse; fuwulani kwa Mulungu ndi mawu achimwemwe.
2 Ne müthiştir yüce RAB, Bütün dünyanın ulu Kralı.
Ndi woopsadi Yehova Wammwambamwamba; Mfumu yayikulu ya dziko lonse lapansi!
3 Halkları altımıza, Ulusları ayaklarımızın dibine serer.
Iye anatigonjetsera mitundu yambirimbiri ya anthu; anayika anthu pansi pa mapazi athu.
4 Sevdiği Yakup'un gururu olan mirasımızı O seçti bizim için. (Sela)
Iye anatisankhira cholowa chathu, chonyaditsa cha Yakobo, amene anamukonda. (Sela)
5 RAB Tanrı sevinç çığlıkları, Boru sesleri arasında yükseldi.
Mulungu wakwera, anthu akumufuwulira mwachimwemwe, Yehova wakwera, akumuyimbira malipenga.
6 Ezgiler sunun Tanrı'ya, ezgiler; Ezgiler sunun Kralımız'a, ezgiler!
Imbani matamando kwa Mulungu, imbani matamando; imbani matamando kwa mfumu yathu, imbani matamando.
7 Çünkü Tanrı bütün dünyanın kralıdır, Maskil sunun!
Pakuti Mulungu ndi mfumu ya dziko lonse lapansi; imbirani Iye salimo la matamando.
8 Tanrı kutsal tahtına oturmuş, Krallık eder uluslara.
Mulungu akulamulira mitundu ya anthu; Mulungu wakhala pa mpando wake waufumu woyera.
9 Ulusların önderleri İbrahim'in Tanrısı'nın halkıyla bir araya gelmiş; Çünkü Tanrı'ya aittir yeryüzü kralları. O çok yücedir.
Anthu otchuka mwa anthu a mitundu ina asonkhana monga anthu a Mulungu wa Abrahamu, pakuti mafumu a dziko lapansi ndi ake a Mulungu; Iye wakwezedwa kwakukulu.

< Mezmurlar 47 >