< Mezmurlar 45 >

1 Müzik şefi için - “Zambaklar” makamında Korahoğulları'nın Maskili - Aşk ilahisi Yüreğimden güzel sözler taşıyor, Kral için söylüyorum şiirlerimi, Dilim usta bir yazarın kalemi gibi olsun.
Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a “Maluwa a Kakombo.” Salimo la ana a Kora. Nyimbo ya pa ukwati. Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma pamene ndikulakatula mawu anga kwa mfumu; lilime langa ndi cholembera cha wolemba waluso.
2 Sen insanların en güzelisin, Lütuf saçılmış dudaklarına. Çünkü Tanrı seni sonsuza dek kutsamış.
Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse ndipo milomo yanu inadzozedwa ndi chikondi cha Mulungu chosasinthika, popeza Mulungu wakudalitsani kwamuyaya.
3 Ey yiğit savaşçı, kuşan kılıcını beline, Görkemine, yüceliğine bürün.
Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu; mudziveke nokha ndi ulemerero ndi ukulu wanu.
4 At sırtında görkeminle, zaferle ilerle, Gerçek ve adalet uğruna Sağ elin korkunç işler göstersin.
Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso mʼmalo mwa choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo; dzanja lanu lamanja lionetsere ntchito zanu zoopsa.
5 Okların sivridir, Kral düşmanlarının yüreğine saplanır, Halklar ayaklarının altına serilir.
Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu, mitundu ya anthu igwe pansi pa mapazi anu.
6 Ey Tanrı, tahtın sonsuzluklar boyunca kalıcıdır, Krallığının asası adalet asasıdır.
Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi; ndodo yaufumu yachilungamo idzakhala ndodo yaufumu ya ufumu wanu.
7 Doğruluğu sever, kötülükten nefret edersin. Bunun için Tanrı, senin Tanrın, Seni sevinç yağıyla Arkadaşlarından daha çok meshetti.
Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa; choncho Mulungu, Mulungu wanu, wakukhazikani pamwamba pa anzanu pokudzozani ndi mafuta a chimwemwe.
8 Giysilerinin tümü mür, öd, tarçın kokuyor; Fildişi saraylardan gelen çalgı sesleri seni eğlendiriyor!
Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya; kuchokera ku nyumba zaufumu zokongoletsedwa ndi mnyanga wanjovu nyimbo za zoyimbira zazingwe zimakusangalatsani.
9 Kral kızları senin saygın kadınların arasında, Kraliçe, Ofir altınları içinde senin sağında duruyor.
Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka; ku dzanja lanu lamanja kuli mkwatibwi waufumu ali mu golide wa ku Ofiri.
10 Dinle, ey kral kızı, bak, kulak ver, Halkını, baba evini unut.
Tamvera, iwe mwana wa mkazi ganizira ndipo tchera khutu; iwala anthu ako ndi nyumba ya abambo ako.
11 Kral senin güzelliğine vuruldu, Efendin olduğu için önünde eğil.
Mfumu yathedwa nzeru chifukwa cha kukongola kwako; mulemekeze pakuti iyeyo ndiye mbuye wako.
12 Sur halkı armağan getirecek, Halkın zenginleri lütfunu kazanmak isteyecek.
Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso, amuna a chuma adzafunafuna kukoma mtima kwako.
13 Kral kızı odasında ışıl ışıl parıldıyor, Giysisi altınla dokunmuş.
Wokongola kwambiri ndi mwana wa mfumu ali mʼchipinda mwake, chovala chake ndi cholukidwa ndi thonje ndi golide.
14 İşlemeli giysiler içinde kralın önüne çıkarılacak, Arkadaşları, ona eşlik eden kızlar sana getirilecek.
Atavala zovala zamaluwamaluwa akupita naye kwa mfumu; anamwali okhala naye akumutsatira ndipo abweretsedwa kwa inu.
15 Sevinç ve coşkuyla götürülecek, Kralın sarayına girecekler.
Iwo akuwaperekeza ndi chimwemwe ndi chisangalalo; akulowa mʼnyumba yaufumu.
16 Atalarının yerini oğulların alacak, Onları önder yapacaksın bütün ülkeye.
Ana ako aamuna adzatenga malo a makolo ako; udzachititsa kuti akhale ana a mfumu mʼdziko lonse.
17 Adını kuşaklar boyunca yaşatacağım, Böylece halklar sonsuza dek övecek seni.
Ndidzabukitsa mbiri yako mʼmibado yonse; choncho mitundu yonse idzakutamanda ku nthawi za nthawi.

< Mezmurlar 45 >