< Mezmurlar 37 >

1 Davut'un mezmuru Kötülük edenlere kızıp üzülme, Suç işleyenlere özenme!
Salimo la Davide. Usamavutike chifukwa cha anthu oyipa kapena kuchitira nsanje amene akuchita cholakwa;
2 Çünkü onlar ot gibi hemen solacak, Yeşil bitki gibi kuruyup gidecek.
pakuti monga udzu iwo adzafota msanga, ngati mbewu zobiriwira adzanyala msanga.
3 Sen RAB'be güven, iyilik yap, Ülkede otur, sadakatle çalış.
Khulupirira Yehova ndipo uzichita zabwino; khazikika mʼdziko ndi kutsata zokhulupirika.
4 RAB'den zevk al, O senin yüreğinin dileklerini yerine getirecektir.
Udzikondweretse wekha mwa Yehova ndipo Iye adzakupatsa zokhumba za mtima wako.
5 Her şeyi RAB'be bırak, O'na güven, O gerekeni yapar.
Pereka njira yako kwa Yehova; dalira Iye ndipo Iyeyo adzachita izi:
6 O senin doğruluğunu ışık gibi, Hakkını öğle güneşi gibi Aydınlığa çıkarır.
Iye adzachititsa chilungamo chako kuwala ngati mʼbandakucha, chiweruzo chako ngati dzuwa la masana.
7 RAB'bin önünde sakin dur, sabırla bekle; Kızıp üzülme işi yolunda olanlara, Kötü amaçlarına kavuşanlara.
Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umudikire mofatsa; usavutike pamene anthu apambana mʼnjira zawo, pamene iwo achita zinthu zawo zoyipa.
8 Kızmaktan kaçın, bırak öfkeyi, Üzülme, yalnız kötülüğe sürükler bu seni.
Pewa kupsa mtima ndipo tembenuka kuchoka ku ukali, usavutike chifukwa zimenezi zimatsogolera ku zoyipa.
9 Çünkü kötülerin kökü kazınacak, Ama RAB'be umut bağlayanlar ülkeyi miras alacak.
Pakuti anthu oyipa adzachotsedwa, koma iwo amene amayembekeza mwa Yehova adzalandira dziko.
10 Yakında kötünün sonu gelecek, Yerini arasan da bulunmayacak.
Kwa kanthawi oyipa sadzapezekanso; ngakhale muwafunefune, sadzapezekanso.
11 Ama alçakgönüllüler ülkeyi miras alacak, Derin bir huzurun zevkini tadacak.
Koma ofatsa adzalandira dziko ndipo adzasangalala ndi mtendere waukulu.
12 Kötü insan doğru insana düzen kurar, Diş gıcırdatır.
Oyipa amakonza chiwembu kutsutsana ndi olungama ndipo amawakukutira mano;
13 Ama Rab kötüye güler, Çünkü bilir onun sonunun geldiğini.
koma Ambuye amaseka oyipa pakuti Iye amadziwa kuti tsiku lawo likubwera.
14 Kılıç çekti kötüler, yaylarını gerdi, Mazlumu, yoksulu yıkmak, Doğru yolda olanları öldürmek için.
Oyipa amasolola lupanga ndi kupinda uta kugwetsa osauka ndi osowa, kupha iwo amene njira zawo ndi zolungama.
15 Ama kılıçları kendi yüreklerine saplanacak, Yayları kırılacak.
Koma malupanga awo analasa mitima yawo yomwe, ndipo mauta awo anathyoka.
16 Doğrunun azıcık varlığı, Pek çok kötünün servetinden iyidir.
Zabwino zochepa zimene olungama ali nazo ziposa chuma cha anthu oyipa ambiri;
17 Çünkü kötülerin gücü kırılacak, Ama doğrulara RAB destek olacak.
pakuti mphamvu ya oyipa idzasweka, koma Yehova amasunga olungama.
18 RAB yetkinlerin her gününü gözetir, Onların mirası sonsuza dek sürecek.
Masiku a anthu osalakwa amadziwika ndi Yehova, ndipo cholowa chawo chidzakhala mpaka muyaya.
19 Kötü günde utanmayacaklar, Kıtlıkta karınları doyacak.
Pa nthawi ya mavuto iwo sadzafota; mʼmasiku a njala adzakhala ndi zinthu zambiri.
20 Ama kötüler yıkıma uğrayacak; RAB'bin düşmanları kır çiçekleri gibi kuruyup gidecek, Duman gibi dağılıp yok olacak.
Koma oyipa adzawonongeka; adani a Yehova adzakhala ngati kukongola kwa kuthengo, iwo adzazimirira ngati utsi.
21 Kötüler ödünç alır, geri vermez; Doğrularsa cömertçe verir.
Oyipa amabwereka ndipo sabweza koma olungama amapereka mowolowamanja.
22 RAB'bin kutsadığı insanlar ülkeyi miras alacak, Lanetlediği insanların kökü kazınacak.
Iwo amene Yehova amawadalitsa adzalandira dziko, koma amene Iye amawatemberera adzachotsedwa.
23 RAB insana sağlam adım attırır, İnsanın yolundan hoşnut olursa.
Ngati Yehova akondwera ndi njira ya munthu, amakhazikitsa mayendedwe ake;
24 Düşse bile yıkılmaz insan, Çünkü elinden tutan RAB'dir.
ngakhale atapunthwa sadzagwa, pakuti Yehova amamutchinjiriza ndi dzanja lake.
25 Gençtim, ömrüm tükendi, Ama hiç görmedim doğru insanın terk edildiğini, Soyunun ekmek dilendiğini.
Ine ndinali wamngʼono ndipo tsopano ndakalamba koma sindinaonepo olungama akusiyidwa kapena ana awo akupempha chakudya.
26 O hep cömertçe ödünç verir, Soyu kutsanır.
Iwo ndi owolowamanja nthawi zonse ndipo amabwereketsa mwaufulu; ana awo adzadalitsika.
27 Kötülükten kaç, iyilik yap; Sonsuz yaşama kavuşursun.
Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; pamenepo udzakhazikika mʼdziko kwamuyaya.
28 Çünkü RAB doğruyu sever, Sadık kullarını terk etmez. Onlar sonsuza dek korunacak, Kötülerinse kökü kazınacak.
Pakuti Yehova amakonda wolungama ndipo sadzasiya okhulupirika ake. Iwo adzatetezedwa kwamuyaya, koma zidzukulu za oyipa zidzachotsedwa;
29 Doğrular ülkeyi miras alacak, Orada sonsuza dek yaşayacak.
olungama adzalandira dziko ndipo adzakhazikikamo kwamuyaya.
30 Doğrunun ağzından bilgelik akar, Dilinden adalet damlar.
Pakamwa pa munthu wolungama pamayankhula za nzeru, ndipo lilime lake limayankhula zolungama.
31 Tanrısı'nın yasası yüreğindedir, Ayakları kaymaz.
Lamulo la Mulungu wake lili mu mtima mwake; mapazi ake saterereka.
32 Kötü, doğruya pusu kurar, Onu öldürmeye çalışır.
Oyipa amabisala kudikira olungama; kufunafuna miyoyo yawoyo;
33 Ama RAB onu kötünün eline düşürmez, Yargılanırken mahkûm etmez.
koma Yehova sadzawasiya pansi pa mphamvu yawo kapena kuti atsutsidwe pamene abweretsedwa pa milandu.
34 RAB'be umut bağla, O'nun yolunu tut, Ülkeyi miras almak üzere seni yükseltecektir. Kötülerin kökünün kazındığını göreceksin.
Khulupirira Yehova, ndipo sunga njira yake; Iye adzakukweza ndipo udzalandira dziko kuti likhale lako; udzaona anthu oyipa akuwonongeka.
35 Kötü ve acımasız adamı gördüm, İlk dikildiği toprakta yeşeren ağaç gibi Dal budak salıyordu;
Ine ndinaona munthu woyipa ndi munthu wopanda chifundo akupeza bwino ngati mtengo wobiriwira pa nthaka ya makolo ake.
36 Geçip gitti, yok oldu, Aradım, bulunmaz oldu.
Koma sanachedwe kumwalira ndipo sanaonekenso; ngakhale ndinamuyangʼanayangʼana, sanapezekenso.
37 Yetkin adamı gözle, doğru adama bak, Çünkü yarınlar barışseverindir.
Ganizira za munthu wosalakwa, yangʼanitsitsa munthu wolungama; udzaona kuti ali ndi tsogolo labwino ndipo ali ndi zidzukulu zambiri.
38 Ama başkaldıranların hepsi yok olacak, Kötülerin kökü kazınacak.
Koma anthu ochimwa adzawonongeka; iwowo pamodzi ndi zidzukulu zawo zomwe.
39 Doğruların kurtuluşu RAB'den gelir, Sıkıntılı günde onlara kale olur.
Chipulumutso cha olungama chimachokera kwa Yehova; Iye ndiye linga lawo pa nthawi ya masautso.
40 RAB onlara yardım eder, kurtarır onları, Kötülerin elinden alıp özgür kılar, Çünkü kendisine sığınırlar.
Yehova amawathandiza ndi kuwalanditsa; Iye amawalanditsa kwa oyipa ndi kuwapulumutsa, pakuti amathawira kwa Iye.

< Mezmurlar 37 >