< Mezmurlar 28 >
1 Davut'un mezmuru Ya RAB, sana yakarıyorum, Kayam benim, kulak tıkama sesime; Çünkü sen sessiz kalırsan, Ölüm çukuruna inen ölülere dönerim ben.
Salimo la Davide. Kwa Inu ine ndiyitana, Yehova ndinu Thanthwe langa; musakhale osamva kwa ine. Pakuti mukapitirira kukhala chete, ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
2 Seni yardıma çağırdığımda, Ellerimi kutsal konutuna doğru açtığımda, Kulak ver yalvarışlarıma.
Imvani kupempha chifundo kwanga pomwe ndikuyitana kwa Inu kuti mundithandize, pomwe ndikukweza manja anga kuloza ku malo anu oyeretsetsa.
3 Beni kötülerle, haksızlık yapanlarla Aynı kefeye koyup cezalandırma. Onlar komşularıyla dostça konuşur, Ama yüreklerinde kötülük beslerler.
Musandikokere kutali pamodzi ndi anthu oyipa, pamodzi ndi iwo amene amachita zoyipa, amene amayankhula mwachikondi ndi anzawo koma akusunga chiwembu mʼmitima mwawo.
4 Eylemlerine, yaptıkları kötülüklere göre onları yanıtla; Yaptıklarının, hak ettiklerinin karşılığını ver.
Muwabwezere chifukwa cha zochita zawo ndi ntchito zawo zoyipa; abwezereni chifuwa cha zimene manja awo achita ndipo mubweretse pa iwo zimene zowayenera.
5 Onlar RAB'bin yaptıklarına, Ellerinin eserine önem vermezler; Bu yüzden RAB onları yıkacak, Bir daha ayağa kaldırmayacak.
Popeza iwowo sakhudzidwa ndi ntchito za Yehova, ndi zimene manja ake anazichita, Iye adzawakhadzula ndipo sadzawathandizanso.
6 RAB'be övgüler olsun! Çünkü yalvarışımı duydu.
Matamando apite kwa Yehova, popeza Iye wamva kupempha chifundo kwanga.
7 RAB benim gücüm, kalkanımdır, O'na yürekten güveniyor ve yardım görüyorum. Yüreğim coşuyor, Ezgilerimle O'na şükrediyorum.
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi chishango changa; mtima wanga umadalira Iye, ndipo Ine ndathandizidwa. Mtima wanga umalumphalumpha chifukwa cha chimwemwe ndipo ndidzayamika Iye mʼnyimbo.
8 RAB halkının gücüdür, Meshettiği kralın zafer kalesidir.
Yehova ndi mphamvu ya anthu ake, linga la chipulumutso kwa wodzozedwa wake.
9 Halkını kurtar, kendi halkını kutsa; Çobanlık et onlara, sürekli destek ol!
Pulumutsani anthu anu ndipo mudalitse cholowa chanu; mukhale mʼbusa wawo ndipo muwakweze kwamuyaya.