< Mezmurlar 121 >

1 Hac ilahisi Gözlerimi dağlara kaldırıyorum, Nereden yardım gelecek?
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndikweza maso anga ku mapiri; kodi thandizo langa limachokera kuti?
2 Yeri göğü yaratan RAB'den gelecek yardım.
Thandizo langa limachokera kwa Yehova, wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
3 O ayaklarının kaymasına izin vermez, Seni koruyan uyuklamaz.
Sadzalola kuti phazi lako literereke; Iye amene amakusunga sadzawodzera.
4 İsrail'in koruyucusu ne uyur ne uyuklar.
Taonani, Iye amene amasunga Israeli sadzawodzera kapena kugona.
5 Senin koruyucun RAB'dir, O sağ yanında sana gölgedir.
Yehova ndiye amene amakusunga; Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
6 Gündüz güneş, Gece ay sana zarar vermez.
Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana, kapena mwezi nthawi ya usiku.
7 RAB her kötülükten seni korur, Esirger canını.
Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse; adzasunga moyo wako.
8 Şimdiden sonsuza dek RAB koruyacak gidişini, gelişini.
Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako; kuyambira tsopano mpaka muyaya.

< Mezmurlar 121 >