< Mezmurlar 119 >

1 Ne mutlu yolları temiz olanlara, RAB'bin yasasına göre yaşayanlara!
Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
2 Ne mutlu O'nun öğütlerine uyanlara, Bütün yüreğiyle O'na yönelenlere!
Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
3 Hiç haksızlık etmezler, O'nun yolunda yürürler.
Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
4 Koyduğun koşullara Dikkatle uyulmasını buyurdun.
Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
5 Keşke kararlı olsam Senin kurallarına uymakta!
Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
6 Hiç utanmayacağım, Bütün buyruklarını izledikçe.
Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
7 Şükredeceğim sana temiz yürekle, Adil hükümlerini öğrendikçe.
Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
8 Kurallarını yerine getireceğim, Bırakma beni hiçbir zaman!
Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
9 Genç insan yolunu nasıl temiz tutar? Senin sözünü tutmakla.
Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
10 Bütün yüreğimle sana yöneliyorum, İzin verme buyruklarından sapmama!
Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
11 Aklımdan çıkarmam sözünü, Sana karşı günah işlememek için.
Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
12 Övgüler olsun sana, ya RAB, Bana kurallarını öğret.
Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
13 Ağzından çıkan bütün hükümleri Dudaklarımla yineliyorum.
Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
14 Sevinç duyuyorum öğütlerini izlerken, Sanki benim oluyor bütün hazineler.
Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
15 Koşullarını derin derin düşünüyorum, Yollarını izlerken.
Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
16 Zevk alıyorum kurallarından, Sözünü unutmayacağım.
Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
17 Ben kuluna iyilik et ki yaşayayım, Sözüne uyayım.
Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
18 Gözlerimi aç, Yasandaki harikaları göreyim.
Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
19 Garibim bu dünyada, Buyruklarını benden gizleme!
Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
20 İçim tükeniyor, Her an hükümlerini özlemekten.
Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
21 Buyruklarından sapan Lanetli küstahları azarlarsın.
Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
22 Uzaklaştır benden küçümsemeleri, hakaretleri, Çünkü öğütlerini tutuyorum.
Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
23 Önderler toplanıp beni kötüleseler bile, Ben kulun senin kurallarını derin derin düşüneceğim.
Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
24 Öğütlerin benim zevkimdir, Bana akıl verirler.
Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
25 Toza toprağa serildim, Sözün uyarınca yaşam ver bana.
Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
26 Yaptıklarımı açıkladım, beni yanıtladın; Kurallarını öğret bana!
Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
27 Koşullarını anlamamı sağla ki, Harikalarının üzerinde düşüneyim.
Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
28 İçim eriyor kederden, Sözün uyarınca güçlendir beni!
Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
29 Yalan yoldan uzaklaştır, Yasan uyarınca lütfet bana.
Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
30 Ben sadakat yolunu seçtim, Hükümlerini uygun gördüm.
Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
31 Öğütlerine dört elle sarıldım, ya RAB, Utandırma beni!
Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
32 İçime huzur verdiğin için Buyrukların doğrultusunda koşacağım.
Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
33 Kurallarını nasıl izleyeceğimi öğret bana, ya RAB, Öyle ki, onları sonuna kadar izleyeyim.
Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
34 Anlamamı sağla, yasana uyayım, Bütün yüreğimle onu yerine getireyim.
Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
35 Buyrukların doğrultusunda yol göster bana, Çünkü yolundan zevk alırım.
Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
36 Yüreğimi haksız kazanca değil, Kendi öğütlerine yönelt.
Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
37 Gözlerimi boş şeylerden çevir, Beni kendi yolunda yaşat.
Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
38 Senden korkulması için Ben kuluna verdiğin sözü yerine getir.
Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
39 Korktuğum hakaretten uzak tut beni, Çünkü senin ilkelerin iyidir.
Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
40 Çok özlüyorum senin koşullarını! Beni doğruluğunun içinde yaşat!
Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
41 Bana sevgini göster, ya RAB, Sözün uyarınca kurtar beni!
Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
42 O zaman beni aşağılayanlara Gereken yanıtı verebilirim, Çünkü senin sözüne güvenirim.
ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
43 Gerçeğini ağzımdan düşürme, Çünkü senin hükümlerine umut bağladım.
Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
44 Yasana sürekli, Sonsuza dek uyacağım.
Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
45 Özgürce yürüyeceğim, Çünkü senin koşullarına yöneldim ben.
Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
46 Kralların önünde senin öğütlerinden söz edecek, Utanç duymayacağım.
Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
47 Senin buyruklarından zevk alıyor, Onları seviyorum.
popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
48 Saygı ve sevgi duyuyorum buyruklarına, Derin derin düşünüyorum kurallarını.
Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
49 Kuluna verdiğin sözü anımsa, Bununla umut verdin bana.
Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
50 Acı çektiğimde beni avutan budur, Sözün bana yaşam verir.
Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
51 Çok eğlendiler küstahlar benimle, Yine de yasandan şaşmadım.
Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
52 Geçmişte verdiğin hükümleri anımsayınca, Avundum, ya RAB.
Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
53 Çileden çıkıyorum, Yasanı terk eden kötüler yüzünden.
Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
54 Senin kurallarındır ezgilerimin konusu, Konuk olduğum bu dünyada.
Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
55 Gece adını anarım, ya RAB, Yasana uyarım.
Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
56 Tek yaptığım, Senin koşullarına uymak.
Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
57 Benim payıma düşen sensin, ya RAB, Sözlerini yerine getireceğim, dedim.
Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
58 Bütün yüreğimle sana yakardım. Lütfet bana, sözün uyarınca.
Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
59 Tuttuğum yolları düşündüm, Senin öğütlerine göre adım attım.
Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
60 Buyruklarına uymak için Elimi çabuk tuttum, oyalanmadım.
Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
61 Kötülerin ipleri beni sardı, Yasanı unutmadım.
Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
62 Doğru hükümlerin için Gece yarısı kalkıp sana şükrederim.
Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
63 Dostuyum bütün senden korkanların, Koşullarına uyanların.
Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
64 Yeryüzü sevginle dolu, ya RAB, Kurallarını öğret bana!
Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
65 Ya RAB, iyilik ettin kuluna, Sözünü tuttun.
Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
66 Bana sağduyu ve bilgi ver, Çünkü inanıyorum buyruklarına.
Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
67 Acı çekmeden önce yoldan sapardım, Ama şimdi sözüne uyuyorum.
Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
68 Sen iyisin, iyilik edersin; Bana kurallarını öğret.
Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
69 Küstahlar yalanlarla beni lekeledi, Ama ben bütün yüreğimle senin koşullarına uyarım.
Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
70 Onların yüreği yağ bağladı, Bense zevk alırım yasandan.
Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
71 İyi oldu acı çekmem; Çünkü kurallarını öğreniyorum.
Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
72 Ağzından çıkan yasa benim için Binlerce altın ve gümüşten daha değerlidir.
Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
73 Senin ellerin beni yarattı, biçimlendirdi. Anlamamı sağla ki buyruklarını öğreneyim.
Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
74 Senden korkanlar beni görünce sevinsin, Çünkü senin sözüne umut bağladım.
Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
75 Biliyorum, ya RAB, hükümlerin adildir; Bana acı çektirirken bile sadıksın.
Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
76 Ben kuluna verdiğin söz uyarınca, Sevgin beni avutsun.
Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
77 Sevecenlik göster bana, yaşayayım, Çünkü yasandan zevk alıyorum.
Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
78 Utansın küstahlar beni yalan yere suçladıkları için. Bense senin koşullarını düşünüyorum.
Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
79 Bana dönsün senden korkanlar, Öğütlerini bilenler.
Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
80 Yüreğim kusursuz uysun kurallarına, Öyle ki, utanç duymayayım.
Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
81 İçim tükeniyor senin kurtarışını özlerken, Senin sözüne umut bağladım ben.
Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
82 Gözümün feri sönüyor söz verdiklerini beklemekten, “Ne zaman avutacaksın beni?” diye soruyorum.
Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
83 Dumandan kararmış tuluma döndüm, Yine de unutmuyorum kurallarını.
Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
84 Daha ne kadar bekleyecek kulun? Ne zaman yargılayacaksın bana zulmedenleri?
Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
85 Çukur kazdılar benim için Yasana uymayan küstahlar.
Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
86 Bütün buyrukların güvenilirdir; Haksız yere zulmediyorlar, yardım et bana!
Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
87 Nerdeyse sileceklerdi beni yeryüzünden, Ama ben senin koşullarından ayrılmadım.
Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
88 Koru canımı sevgin uyarınca, Tutayım ağzından çıkan öğütleri.
Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
89 Ya RAB, sözün Göklerde sonsuza dek duruyor.
Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
90 Sadakatin kuşaklar boyu sürüyor, Kurduğun yeryüzü sapasağlam duruyor.
Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
91 Bugün hükümlerin uyarınca ayakta duran her şey Sana kulluk ediyor.
Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
92 Eğer yasan zevk kaynağım olmasaydı, Çektiğim acılardan yok olurdum.
Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
93 Koşullarını asla unutmayacağım, Çünkü onlarla bana yaşam verdin.
Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
94 Kurtar beni, çünkü seninim, Senin koşullarına yöneldim.
Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
95 Kötüler beni yok etmeyi beklerken, Ben senin öğütlerini inceliyorum.
Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
96 Kusursuz olan her şeyin bir sonu olduğunu gördüm, Ama senin buyruğun sınır tanımaz.
Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
97 Ne kadar severim yasanı! Bütün gün düşünürüm onun üzerinde.
Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
98 Buyrukların beni düşmanlarımdan bilge kılar, Çünkü her zaman aklımdadır onlar.
Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
99 Bütün öğretmenlerimden daha akıllıyım, Çünkü öğütlerin üzerinde düşünüyorum.
Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
100 Yaşlılardan daha bilgeyim, Çünkü senin koşullarına uyuyorum.
Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
101 Sakınırım her kötü yoldan, Senin sözünü tutmak için.
Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
102 Ayrılmam hükümlerinden, Çünkü bana sen öğrettin.
Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
103 Ne tatlı geliyor verdiğin sözler damağıma, Baldan tatlı geliyor ağzıma!
Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
104 Senin koşullarına uymakla bilgelik kazanıyorum, Bu yüzden nefret ediyorum her yanlış yoldan.
Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
105 Sözün adımlarım için çıra, Yolum için ışıktır.
Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
106 Adil hükümlerini izleyeceğime ant içtim, Andımı tutacağım.
Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
107 Çok sıkıntı çektim, ya RAB; Koru hayatımı sözün uyarınca.
Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
108 Ağzımdan çıkan içten övgüleri Kabul et, ya RAB, Bana hükümlerini öğret.
Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
109 Hayatım her an tehlikede, Yine de unutmam yasanı.
Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
110 Kötüler tuzak kurdu bana, Yine de sapmadım senin koşullarından.
Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
111 Öğütlerin sonsuza dek mirasımdır, Yüreğimin sevincidir onlar.
Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
112 Kararlıyım Sonuna kadar senin kurallarına uymaya.
Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
113 Döneklerden tiksinir, Senin yasanı severim.
Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
114 Sığınağım ve kalkanım sensin, Senin sözüne umut bağlarım.
Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
115 Ey kötüler, benden uzak durun, Tanrım'ın buyruklarını yerine getireyim.
Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
116 Sözün uyarınca destek ol bana, yaşam bulayım; Umudumu boşa çıkarma!
Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
117 Sıkı tut beni, kurtulayım, Her zaman kurallarını dikkate alayım.
Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
118 Kurallarından sapan herkesi reddedersin, Çünkü onların hileleri boştur.
Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
119 Dünyadaki kötüleri cüruf gibi atarsın, Bu yüzden severim senin öğütlerini.
Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
120 Bedenim ürperiyor dehşetinden, Korkuyorum hükümlerinden.
Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
121 Adil ve doğru olanı yaptım, Gaddarların eline bırakma beni!
Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
122 Güven altına al kulunun mutluluğunu, Baskı yapmasın bana küstahlar.
Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
123 Gözümün feri sönüyor, Beni kurtarmanı, Adil sözünü yerine getirmeni beklemekten.
Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
124 Kuluna sevgin uyarınca davran, Bana kurallarını öğret.
Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
125 Ben senin kulunum, bana akıl ver ki, Öğütlerini anlayabileyim.
Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
126 Ya RAB, harekete geçmenin zamanıdır, Yasanı çiğniyorlar.
Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
127 Bu yüzden senin buyruklarını, Altından, saf altından daha çok seviyorum;
Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
128 Koyduğun koşulların hepsini doğru buluyorum, Her yanlış yoldan tiksiniyorum.
ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
129 Harika öğütlerin var, Bu yüzden onlara candan uyuyorum.
Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
130 Sözlerinin açıklanışı aydınlık saçar, Saf insanlara akıl verir.
Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
131 Ağzım açık, soluk soluğayım, Çünkü buyruklarını özlüyorum.
Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
132 Bana lütufla bak, Adını sevenlere her zaman yaptığın gibi.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
133 Adımlarımı pekiştir verdiğin söz uyarınca, Hiçbir suç bana egemen olmasın.
Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
134 Kurtar beni insan baskısından, Koşullarına uyabileyim.
Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
135 Yüzün aydınlık saçsın kulunun üzerine, Kurallarını öğret bana.
Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
136 Oluk oluk yaş akıyor gözlerimden, Çünkü uymuyorlar yasana.
Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
137 Sen adilsin, ya RAB, Hükümlerin doğrudur.
Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
138 Buyurduğun öğütler doğru Ve tam güvenilirdir.
Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
139 Gayretim beni tüketti, Çünkü düşmanlarım unuttu senin sözlerini.
Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
140 Sözün çok güvenilirdir, Kulun onu sever.
Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
141 Önemsiz ve horlanan biriyim ben, Ama koşullarını unutmuyorum.
Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
142 Adaletin sonsuza dek doğrudur, Yasan gerçektir.
Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
143 Sıkıntıya, darlığa düştüm, Ama buyrukların benim zevkimdir.
Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
144 Öğütlerin sonsuza dek doğrudur; Bana akıl ver ki, yaşayayım.
Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
145 Bütün yüreğimle haykırıyorum, Yanıtla beni, ya RAB! Senin kurallarına uyacağım.
Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
146 Sana sesleniyorum, Kurtar beni, Öğütlerine uyayım.
Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
147 Gün doğmadan kalkıp yardım dilerim, Senin sözüne umut bağladım.
Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
148 Verdiğin söz üzerinde düşüneyim diye, Gece boyunca uyku girmiyor gözüme.
Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
149 Sevgin uyarınca sesime kulak ver, Hükümlerin uyarınca, ya RAB, yaşam ver bana!
Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
150 Yaklaşıyor kötülük ardınca koşanlar, Yasandan uzaklaşıyorlar.
Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
151 Oysa sen yakınsın, ya RAB, Bütün buyrukların gerçektir.
Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
152 Çoktan beri anladım Öğütlerini sonsuza dek verdiğini.
Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
153 Çektiğim sıkıntıyı gör, kurtar beni, Çünkü yasanı unutmadım.
Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
154 Davamı savun, özgür kıl beni, Sözün uyarınca koru canımı.
Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
155 Kurtuluş kötülerden uzaktır, Çünkü senin kurallarına yönelmiyorlar.
Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
156 Çok sevecensin, ya RAB, Hükümlerin uyarınca koru canımı.
Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
157 Bana zulmedenler, düşmanlarım çok, Yine de sapmadım senin öğütlerinden.
Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
158 Tiksinerek bakıyorum hainlere, Çünkü uymuyorlar senin sözüne.
Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
159 Bak, ne kadar seviyorum koşullarını, Sevgin uyarınca, ya RAB, koru canımı.
Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
160 Sözlerinin temeli gerçektir, Doğru hükümlerinin tümü sonsuza dek sürecektir.
Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
161 Yok yere zulmediyor bana önderler, Oysa yüreğim senin sözünle titrer.
Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
162 Ganimet bulan biri gibi Verdiğin sözlerde sevinç bulurum.
Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
163 Tiksinir, iğrenirim yalandan, Ama senin yasanı severim.
Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
164 Doğru hükümlerin için Seni günde yedi kez överim.
Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
165 Yasanı sevenler büyük esenlik bulur, Hiçbir şey sendeletmez onları.
Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
166 Ya RAB, kurtarışına umut bağlar, Buyruklarını yerine getiririm.
Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
167 Öğütlerine candan uyar, Onları çok severim.
Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
168 Öğütlerini, koşullarını uygularım, Çünkü bütün davranışlarımı görürsün sen.
Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
169 Feryadım sana erişsin, ya RAB, Sözün uyarınca akıl ver bana!
Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
170 Yalvarışım sana ulaşsın; Verdiğin söz uyarınca kurtar beni!
Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
171 Dudaklarımdan övgüler aksın, Çünkü bana kurallarını öğretiyorsun.
Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
172 Dilimde sözün ezgilere dönüşsün, Çünkü bütün buyrukların doğrudur.
Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
173 Elin bana yardıma hazır olsun, Çünkü senin koşullarını seçtim ben.
Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
174 Kurtarışını özlüyorum, ya RAB, Yasan zevk kaynağımdır.
Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
175 Beni yaşat ki, sana övgüler sunayım, Hükümlerin bana yardımcı olsun.
Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
176 Kaybolmuş koyun gibi avare dolaşıyordum; Kulunu ara, Çünkü buyruklarını unutmadım ben.
Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.

< Mezmurlar 119 >