< Mezmurlar 114 >
1 İsrail Mısır'dan çıktığında, Yakup'un soyu yabancı dil konuşan bir halktan ayrıldığında,
Pamene Israeli anatuluka mu Igupto, nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo,
2 Yahuda Rab'bin kutsal yeri oldu, İsrail de O'nun krallığı.
Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu, Israeli anasanduka ufumu wake.
3 Deniz olanı görüp geri çekildi, Şeria Irmağı tersine aktı.
Nyanja inaona ndi kuthawa, mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo;
4 Dağlar koç gibi, Tepeler kuzu gibi sıçradı.
mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna, timapiri ngati ana ankhosa.
5 Ey deniz, sana ne oldu da kaçtın? Ey Şeria, neden tersine aktın?
Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa? iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo?
6 Ey dağlar, niçin koç gibi, Ey tepeler, niçin kuzu gibi sıçradınız?
inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna, inu timapiri, ngati ana ankhosa?
7 Titre, ey yeryüzü, Kayayı havuza, Çakmaktaşını pınara çeviren Rab'bin önünde, Yakup'un Tanrısı'nın huzurunda.
Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi, pamaso pa Mulungu wa Yakobo,
amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime, thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.