< Mezmurlar 110 >

1 Davut'un mezmuru RAB Efendim'e: “Ben düşmanlarını ayaklarının altına serinceye dek Sağımda otur” diyor.
Salimo la Davide. Yehova akuwuza Mbuye wanga kuti, “Khala ku dzanja langa lamanja mpaka nditasandutsa adani ako kukhala chopondapo mapazi ako.”
2 RAB Siyon'dan uzatacak kudret asanı, Düşmanlarının ortasında egemenlik sür!
Yehova adzakuza ndodo yamphamvu ya ufumu wako kuchokera mʼZiyoni; udzalamulira pakati pa adani ako.
3 Savaşacağın gün Gönüllü gidecek askerlerin. Seherin bağrından doğan çiy gibi Kutsal giysiler içinde Sana gelecek gençlerin.
Ankhondo ako adzakhala odzipereka pa tsiku lako la nkhondo. Atavala chiyero chaulemerero, kuchokera mʼmimba ya mʼbandakucha, udzalandira mame a unyamata wako.
4 RAB ant içti, kararından dönmez: “Melkisedek düzeni uyarınca Sonsuza dek kâhinsin sen!” dedi.
Yehova walumbira ndipo sadzasintha maganizo ake: “Ndiwe wansembe mpaka muyaya monga mwa unsembe wa Melikizedeki.”
5 Rab senin sağındadır, Kralları ezecek öfkelendiği gün.
Ambuye ali kudzanja lako lamanja; Iye adzaponda mafumu pa tsiku la ukali wake.
6 Ulusları yargılayacak, ortalığı cesetler dolduracak, Dünyanın dört bucağında başları ezecek.
Adzaweruza anthu a mitundu ina, adzadzaza dziko lapansi ndi mitembo ndipo adzaphwanya olamulira a pa dziko lonse lapansi.
7 Yol kenarındaki dereden su içecek; Bu yüzden başını dik tutacak.
Iye adzamwa mu mtsinje wa mʼmbali mwa njira; choncho adzaweramutsa mutu wake.

< Mezmurlar 110 >