< Süleyman'In Özdeyişleri 7 >

1 Oğlum, sözlerimi yerine getir, Aklında tut buyruklarımı.
Mwana wanga, mvera mawu anga; usunge bwino malamulo angawa.
2 Buyruklarımı yerine getir ki, yaşayasın. Öğrettiklerimi gözünün bebeği gibi koru.
Utsate malamulo anga ndipo udzakhala ndi moyo; samala malangizo angawa monga uchitira ndi maso ako.
3 Onları yüzük gibi parmaklarına geçir, Yüreğinin levhasına yaz.
Uchite ngati wawamangirira pa zala zako, ndiponso ngati kuti wawalemba pa mtima pako.
4 Bilgeliğe, “Sen kızkardeşimsin”, Akla, “Akrabamsın” de.
Nzeru uyiwuze kuti, “Iwe ndiwe mlongo wanga,” ndipo khalidwe lomvetsa bwino zinthu ulitchule kuti, “Bwenzi langa lapamtima.”
5 Zina eden kadından, Yaltaklanan ahlaksız kadından seni koruyacak olan bunlardır.
Zidzakuteteza kwa mkazi wachigololo ndiponso zidzakuthandiza kusamvera mawu oshashalika a mkazi wachilendo.
6 Evimin penceresinden, Kafesin ardından dışarıyı seyrederken,
Tsiku lina pa zenera la nyumba yanga ndinasuzumira pa zenera.
7 Bir sürü toy gencin arasında, Sağduyudan yoksun bir delikanlı çarptı gözüme.
Ndinaona pakati pa anthu opusa, pakati pa anyamata, mnyamata wina wopanda nzeru.
8 Akşamüzeri, alaca karanlıkta, Akşam karanlığı çökerken, O kadının oturduğu sokağa saptığını, Onun evine yöneldiğini gördüm.
Iye ankayenda njira yodutsa pafupi ndi nyumba ya mkaziyo, kuyenda molunjika nyumba ya mkaziyo.
9
Inali nthawi yachisisira madzulo, nthawi ya usiku, kuli mdima.
10 Derken kadın onu karşıladı, Fahişe kılığıyla sinsice.
Ndipo mkaziyo anadzakumana naye, atavala ngati munthu wachiwerewere wa mtima wonyenga.
11 Yaygaracı, dik başlı biriydi kadın. Bir an bile durmaz evde.
(Mkaziyo ndi wolongolola ndiponso nkhutukumve, iye ndi wosakhazikika pa khomo.
12 Kâh sokakta, kâh meydanlardadır. Sokak başlarında pusuya yatar.
Mwina umupeza pa msewu, mwina umupeza pa msika, ndipo amadikirira munthu pa mphambano iliyonse).
13 Delikanlıyı tutup öptü, Yüzü kızarmadan ona şöyle dedi:
Tsono amagwira mnyamatayo ndi kupsompsona ndi nkhope yake yopanda manyazi amamuwuza kuti,
14 “Esenlik kurbanlarımı kesmek zorundaydım, Adak sözümü bugün yerine getirdim.
“Ndinayenera kupereka nsembe zachiyanjano. Lero ndakwaniritsa malumbiro anga.
15 Bunun için seni karşılamaya, seni aramaya çıktım, İşte buldum seni!
Choncho ndinabwera kudzakumana nawe; ndinkakufunafuna ndipo ndakupeza!
16 Döşeğime Mısır ipliğinden dokunmuş Renkli örtüler serdim.
Pa bedi panga ndayalapo nsalu zosalala zokongola zochokera ku Igupto.
17 Yatağıma mür, öd Ve tarçın serptim.
Pa bedi panga ndawazapo zonunkhira za mure, mafuta onunkhira a aloe ndi sinamoni.
18 Haydi gel, sabaha dek doya doya sevişelim, Aşktan zevk alalım.
Bwera, tiye tikhale malo amodzi kukondwerera chikondi mpaka mmawa; tiye tisangalatsane mwachikondi!
19 Kocam evde değil, Uzun bir yolculuğa çıktı.
Mwamuna wanga kulibe ku nyumbako; wapita ulendo wautali:
20 Yanına para torbasını aldı, Dolunaydan önce eve dönmeyecek.”
Anatenga thumba la ndalama ndipo adzabwera ku nyumba mwezi ukakhwima.”
21 Onu bir sürü çekici sözlerle baştan çıkardı, Tatlı diliyle peşinden sürükledi.
Ndi mawu ake onyengerera amamukakamiza mnyamatayo; amukopa ndi mawu ake oshashalika.
22 Kesimevine götürülen öküz gibi Hemen izledi onu delikanlı; Tuzağa düşen geyik gibi,
Nthawi yomweyo chitsiru chimamutsatira mkaziyo ngati ngʼombe yopita kukaphedwa, monga momwe mbawala ikodwera mu msampha,
23 Ciğerini bir ok delene kadar; Kapana koşan bir kuş gibi, Bunun yaşamına mal olacağını bilmeden.
mpaka muvi utalasa chiwindi chake, chimakhala ngati mbalame yothamangira mʼkhwekhwe, osadziwa kuti moyo wake uwonongeka.
24 Çocuklarım, şimdi dinleyin beni, Kulak verin söylediklerime,
Tsono ana inu, ndimvereni; mvetsetsani zimene ndikunena.
25 Sakın o kadına gönül vermeyin, Onun yolundan gitmeyin.
Musatengeke mtima ndi njira za mkazi ameneyu; musasochere potsata njira zake.
26 Yere serdiği bir sürü kurbanı var, Öldürdüğü kişilerin sayısı pek çok.
Paja iye anagwetsa anthu ambiri; wapha gulu lalikulu la anthu.
27 Ölüler diyarına giden yoldur onun evi, Ölüm odalarına götürür. (Sheol h7585)
Nyumba yake ndi njira yopita ku manda, yotsikira ku malo a anthu akufa. (Sheol h7585)

< Süleyman'In Özdeyişleri 7 >