< Süleyman'In Özdeyişleri 29 >
1 Defalarca azarlandığı halde dikbaşlılık eden, Ansızın yıkıma uğrayacak, çare yok.
Munthu amene amawumitsabe khosi lake atadzudzulidwa kwambiri, adzawonongeka mwadzidzidzi popanda chomuchiritsa.
2 Doğru kişiler çoğalınca halk sevinir, Kötü kişi hükümdar olunca halk inler.
Anthu olungama akamalamulira mʼdziko anthu amakondwa, koma ngati dziko lilamulidwa ndi anthu oyipa mtima anthu amadandaula.
3 Bilgeliği seven babasını sevindirir, Fahişelerle dostluk eden malını yitirir.
Munthu amene amakonda nzeru amasangalatsa abambo ake, koma woyenda ndi akazi achiwerewere amasakaza chuma chake.
4 Adaletle yöneten kral ülkesini ayakta tutar, Rüşvet alansa çökertir.
Mfumu imalimbitsa dziko poweruza mwachilungamo, koma mfumu imene imawumiriza anthu kuti ayipatse mphatso imawononga dziko.
5 Başkasını pohpohlayan kişi, Ona tuzak olur.
Munthu woshashalika mnzake, akudziyalira ukonde mapazi ake.
6 Kötünün başkaldırısı kendine tuzak olur, Doğru kişiyse ezgi söyler ve sevinir.
Munthu woyipa amakodwa ndi machimo ake, koma wochita chilungamo amayimba lokoma.
7 Doğru kişi yoksulların hakkını verir, Kötü kişi hak hukuk nedir bilmez.
Munthu wolungama amasamalira anthu osauka, koma woyipa salabadira zimenezi.
8 Alaycı kişiler kentleri bile karıştırır, Bilgelerse öfkeyi yatıştırır.
Anthu onyoza atha kuwutsa ziwawa mu mzinda, koma anthu anzeru amaletsa ukali.
9 Bilge kişiyle davası olan ahmak Kızar, alay eder ve rahat vermez.
Ngati munthu wanzeru atsutsana ndi chitsiru, chitsirucho chimachita phokoso ndi kumangoseka ndipo sipakhala mtendere.
10 Kana susamışlar dürüst kişiden nefret eder, Doğrularsa onun canını korur.
Anthu okhetsa magazi amadana ndi munthu wangwiro koma anthu olungama amasamalira moyo wake.
11 Akılsız hep patlamaya hazırdır, Bilgeyse öfkesini dizginler.
Munthu wopusa amaonetsa mkwiyo wake, koma munthu wanzeru amadzigwira.
12 Hükümdar yalana kulak verirse, Bütün görevlileri de kötü olur.
Ngati wolamulira amvera zabodza, akuluakulu ake onse adzakhala oyipa.
13 Zorbayla yoksulun ortak bir noktası var: İkisinin de gözünü açan RAB'dir.
Munthu wosauka ndi munthu wopondereza anzake amafanana pa kuti: Yehova ndiye anawapatsa maso onsewa.
14 Yoksulları adaletle yöneten kralın Tahtı hep güvenlikte olur.
Ngati mfumu iweruza osauka moyenera, mpando wake waufumu udzakhazikika nthawi zonse.
15 Değnekle terbiye bilgelik kazandırır, Kendi haline bırakılan çocuksa annesini utandırır.
Ndodo ndi chidzudzulo zimapatsa nzeru koma mwana womulekerera amachititsa amayi ake manyazi.
16 Kötüler çoğalınca başkaldırı da çoğalır, Ama doğrular onların düşüşünü görecektir.
Oyipa akamalamulira zoyipa zimachuluka, koma anthu olungama adzaona kugwa kwa anthu oyipawo.
17 Oğlunu terbiye et, o da sana huzur verecek Ve gönlünü hoşnut edecektir.
Umulange mwana wako ndipo adzakupatsa mtendere ndi kusangalatsa mtima wako.
18 Tanrısal esinden yoksun olan halk Sınır tanımaz olur. Ne mutlu Kutsal Yasa'yı yerine getirene!
Ngati uthenga wochokera kwa Yehova supezeka anthu amangochita zofuna zawo; koma wodala ndi amene amasunga malamulo.
19 Köle salt sözle terbiye edilemez, Çünkü anlasa da kulak asmaz.
Munthu wantchito sangalangizidwe ndi mawu okha basi; ngakhale awamvetse mawuwo sadzatha kuchitapo kanthu.
20 Sözünü tartmadan konuşan birini tanıyor musun? Akılsızın durumu bile onunkinden daha umut vericidir.
Ngakhale munthu wa uchitsiru nʼkuti ndiponi popeza chikhulupiriro chilipo kuposa munthu wodziyesa yekha kuti ndi wanzeru poyankhula.
21 Çocukluğundan beri kölesini şımartan, Sonunda cezasını çeker.
Ngati munthu asasatitsa wantchito wake kuyambira ali mwana, potsirizira adzapeza kuti wantchitoyo wasanduka mlowachuma wake.
22 Öfkeli kişi çekişme yaratır, Huysuz kişinin başkaldırısı eksik olmaz.
Munthu wamkwiyo amayambitsa mikangano, ndipo munthu waukali amachita zolakwa zambiri.
23 Kibir insanı küçük düşürür, Alçakgönüllülükse onur kazandırır.
Kunyada kwa munthu kudzamutsitsa, koma munthu wodzichepetsa amalandira ulemu.
24 Hırsızla ortak olanın düşmanı kendisidir, Mahkemede yemin etse de bildiğini söylemez.
Woyenda ndi munthu wakuba ndi mdani wa moyo wake womwe; amalumbira koma osawulula kanthu.
25 İnsandan korkmak tuzaktır, Ama RAB'be güvenen güvenlikte olur.
Kuopa munthu kudzakhala ngati msampha, koma aliyense amene amadalira Yehova adzatetezedwa.
26 Hükümdarın gözüne girmek isteyen çoktur, Ama RAB'dir insana adalet sağlayan.
Anthu ambiri amafunitsitsa kuti wolamulira awakomere mtima, koma munthu amaweruzidwa mwachilungamo ndi thandizo la Yehova basi.
27 Doğrular haksızlardan iğrenir, Kötüler de dürüst yaşayanlardan.
Anthu olungama amanyansidwa ndi anthu achinyengo; koma anthu oyipa amanyansidwa ndi anthu a mtima wowongoka.