< Süleyman'In Özdeyişleri 24 >

1 Kötülere imrenme, Onlarla birlikte olmayı isteme.
Usachitire nsanje anthu oyipa, usalakalake kuti uzikhala nawo,
2 Çünkü yürekleri zorbalık tasarlar, Dudakları belalardan söz eder.
pakuti mitima yawo imalingalira chiwawa, ndipo pakamwa pawo pamayankhula zoyambitsa mavuto.
3 Ev bilgelikle yapılır, Akılla pekiştirilir.
Nyumba imamangidwa ndi anthu anzeru, ndipo imakhazikika ndi anthu odziwa zinthu;
4 Bilgi sayesinde odaları Her türlü değerli, güzel eşyayla dolar.
Munthu wodziwa zinthu angathe kudzaza zipinda zake ndi chuma chamtengowapatali ndiponso chabwino.
5 Bilgelik güçten, Bilgi kaba kuvvetten üstündür.
Munthu wodziwa zinthu ali ndi mphamvu yayikulu kuposa munthu wanyonga zambiri, ndipo munthu wachidziwitso amaposa munthu wamphamvu.
6 Savaşmak için yöntem, Zafer kazanmak için birçok danışman gerekli.
Pafunika malangizo kuti ukamenye nkhondo. Pakakhala aphungu ambiri kupambana kumakhalapo.
7 Ahmak için bilgelik ulaşılamayacak kadar yüksektir, Kent kurulunda ağzını açamaz.
Nzeru ndi chinthu chapatali kwambiri kwa chitsiru; chilibe choti chiyankhule pabwalo la milandu pa chipata.
8 Kötülük tasarlayan kişi Düzenbaz olarak bilinecektir.
Amene amakonzekera kuchita zoyipa adzatchedwa mvundulamadzi.
9 Ahmakça tasarılar günahtır, Alaycı kişiden herkes iğrenir.
Kukonzekera kuchita za uchitsiru ndi tchimo, ndipo munthu wonyoza amanyansa anthu.
10 Sıkıntılı günde cesaretini yitirirsen, Gücün kıt demektir.
Ngati utaya mtima nthawi ya mavuto ndiye kuti mphamvu yako ndi yochepadi!
11 Ölüm tehlikesi içinde olanları kurtar, Ölmek üzere olanları esirge.
Uwapulumutse amene akutengedwa kuti akaphedwe; uwalanditse amene akuyenda movutika kupita kokaphedwa.
12 “İşte bunu bilmiyordum” desen de, İnsanın yüreğindekini bilen sezmez mi? Senin canını koruyan anlamaz mı? Ödetmez mi herkese yaptığını?
Ukanena kuti, “Koma ife sitinadziwe kanthu za izi,” kodi Iye amene amasanthula mtima sazindikira zimenezi? Kodi Iye amene amateteza moyo wako sazidziwa zimenezi? Kodi Iye sadzalipira munthu malingana ndi ntchito zake?
13 Oğlum, bal ye, çünkü iyidir, Süzme bal damağa tatlı gelir.
Mwana wanga, uzidya uchi popeza ndi wabwino; uchi wochokera mʼchisa cha njuchi ndi wokoma ukawulawa.
14 Bilgelik de canın için öyledir, bilmiş ol. Bilgeliği bulursan bir geleceğin olur Ve umudun boşa çıkmaz.
Udziwe kuti nzeru ndi yoteronso pa moyo wako; ngati uyipeza nzeruyo, zinthu zidzakuyendera bwino mʼtsogolo, ndipo chiyembekezo chako sichidzapita pachabe.
15 Ey kötü adam, doğru kişinin evine karşı pusuya yatma, Konutunu yıkmaya kalkma.
Usachite zachifwamba nyumba ya munthu wolungama ngati munthu woyipa. Usachite nayo nkhondo nyumba yake;
16 Çünkü doğru kişi yedi kez düşse yine kalkar, Ama kötüler felakette yıkılır.
paja munthu wolungama akagwa kasanu nʼkawiri amadzukiriranso. Koma woyipa adzathedwa tsoka likadzawafikira.
17 Düşmanın düşüşüne keyiflenme, Sendelemesine sevinme.
Usamakondwera ndi kugwa kwa mdani wako. Mtima wako usamasangalale iye akapunthwa.
18 Yoksa RAB görür ve hoşnut kalmaz Ve düşmanına duyduğu öfke yatışır.
Kuopa kuti Yehova ataziona zimenezi nayipidwa nazo, angaleke kukwiyira mdaniyo.
19 Kötülük edenlere kızıp üzülme, Onlara özenme.
Usavutike mtima chifukwa cha anthu ochita zoyipa kapena kuchitira nsanje anthu oyipa,
20 Çünkü kötülerin geleceği yok, Çırası sönecek onların.
paja munthu woyipa alibe tsogolo. Moyo wa anthu oyipa adzawuzimitsa ngati nyale.
21 Oğlum, RAB'be ve krala saygı göster, Onlara başkaldıranlarla arkadaşlık etme.
Mwana wanga, uziopa Yehova ndi mfumu, ndipo usamagwirizana ndi anthu owachitira mwano,
22 Çünkü onlar ansızın felakete uğrar, İnsanın başına ne belalar getireceklerini kim bilir?
awiri amenewa amagwetsa tsoka mwadzidzidzi. Ndani angadziwe mavuto amene angagwetse?
23 Şunlar da bilgelerin sözleridir: Yargılarken yan tutmak iyi değildir.
Malangizo enanso a anthu anzeru ndi awa: Kukondera poweruza mlandu si chinthu chabwino:
24 Kötüye, “Suçsuzsun” diyen yargıcı Halklar lanetler, uluslar kınar.
Aliyense amene amawuza munthu wolakwa kuti, “Iwe ndi munthu wosalakwa,” anthu a mitundu yonse adzamutemberera, ndi mitundu ya anthu idzayipidwa naye.
25 Ne mutlu suçluyu mahkûm edene! Herkes onu candan kutlar.
Koma olanga anthu oyipa zinthu zidzawayendera bwino ndipo madalitso ochuluka adzakhala pa iwo.
26 Dürüst yanıt Gerçek dostluğun işaretidir.
Woyankhula mawu owona ndiye amaonetsa chibwenzi chenicheni.
27 İlkin dışardaki işini bitirip tarlanı hazırla, Ondan sonra evini yap.
Ugwiriretu ntchito zako zonse, makamaka za ku munda ndipo pambuyo pake uyambe kumanga nyumba.
28 Başkalarına karşı nedensiz tanıklık etme Ve dudaklarınla aldatma.
Usakhale mboni yotsutsa mnzako popanda chifukwa, kapena kugwiritsa ntchito pakamwa pako kunena zachinyengo.
29 “Bana yaptığını ben de ona yapacağım, Ödeteceğim bana yaptığını” deme.
Usanene kuti, “Ine ndidzamuchitira iye monga momwe wandichitira ine; ndidzamubwezera munthu ameneyo zimene anandichitira.”
30 Tembelin tarlasından, Sağduyudan yoksun kişinin bağından geçtiğimde
Ndinkayenda mʼmbali mwa munda wa munthu waulesi ndinadutsa munda wamphesa wa munthu wopanda nzeru.
31 Her yanı dikenlerin, otların Kapladığını gördüm; Taş duvar da yıkılmıştı.
Ndinapeza kuti paliponse mʼmundamo munali mutamera minga, mʼnthaka imeneyo munali mutamera khwisa, ndipo mpanda wake wamiyala unali utawonongeka.
32 Gördüklerimi derin derin düşündüm, Seyrettiklerimden ibret aldım.
Tsono nditaona ndinayamba kuganizira mu mtima mwanga ndipo ndinatolapo phunziro ili:
33 “Biraz kestireyim, biraz uyuklayayım, Ellerimi kavuşturup şöyle bir uyuyayım” demeye kalmadan,
Ukati, “Bwanji ndigone pangʼono,” kapena “Ndiwodzereko pangʼono,” kapenanso “Ndipinde manja pangʼono kuti ndipumule,”
34 Yokluk bir haydut gibi, Yoksulluk bir akıncı gibi gelir üzerine.
umphawi udzafika pa iwe ngati mbala ndipo usiwa udzakupeza ngati munthu wachifwamba.

< Süleyman'In Özdeyişleri 24 >