< Süleyman'In Özdeyişleri 14 >

1 Bilge kadın evini yapar, Ahmak kadın evini kendi eliyle yıkar.
Mkazi wanzeru amamanga banja lake, koma mkazi wopusa amalimasula ndi manja ake omwe.
2 Doğru yolda yürüyen, RAB'den korkar, Yoldan sapan, RAB'bi hor görür.
Amene amayenda molungama amaopa Yehova, koma amene njira zake ndi zoyipa amanyoza Yehova.
3 Ahmağın sözleri sırtına kötektir, Ama bilgenin dudakları kendisini korur.
Kuyankhula kwa chitsiru kumamuyitanira ndodo pa msana, koma milomo ya munthu wanzeru imamuteteza.
4 Öküz yoksa yemlik boş kalır, Çünkü bol ürünü sağlayan öküzün gücüdür.
Pakasowa ngʼombe zolima gome limakhala lopanda chakudya, koma pakakhala ngʼombe zamphamvu zakudya zimachulukanso.
5 Güvenilir tanık yalan söylemez, Yalancı tanıksa yalan solur.
Mboni yokhulupirika sinama, koma mboni yonyenga imayankhula zabodza.
6 Alaycı bilgeliği arasa da bulamaz, Akıllı içinse bilgi edinmek kolaydır.
Wonyoza anzake amafunafuna nzeru koma osayipeza, koma munthu womvetsa bwino amadziwa zinthu msanga.
7 Akılsız kişiden uzak dur, Çünkü sana öğretecek bir şeyi yok.
Khala kutali ndi munthu wopusa chifukwa sudzapeza mawu a nzeru.
8 İhtiyatlı kişinin bilgeliği, ne yapacağını bilmektir, Akılsızların ahmaklığıysa aldanmaktır.
Nzeru za munthu wochenjera zagona pakuzindikira njira zake. Koma uchitsiru wa zitsiru umapusitsidwa ndi chinyengo chawo chomwe.
9 Ahmaklar suç sunusuyla alay eder, Dürüstler ise iyi niyetlidir.
Zitsiru zimanyoza za kulapa machimo, awo, koma kufuna kwabwino kumapezeka mwa anthu olungama.
10 Yürek kendi acısını bilir, Sevinciniyse kimse paylaşmaz.
Mtima uliwonse umadziwa wokha zowawa zake, ndipo palibe wina aliyense angadziwe kukondwa kwake.
11 Kötü kişinin evi yerle bir edilecek, Doğru kişinin konutuysa bayındır olacak.
Nyumba ya munthu woyipa idzapasuka, koma tenti ya munthu wowongoka mtima idzakhazikika.
12 Öyle yol var ki, insana düz gibi görünür, Ama sonu ölümdür.
Pali njira ina yooneka ngati yabwino kwa munthu, koma kumatsiriziro kwake ndi ku imfa.
13 Gülerken bile yürek sızlayabilir, Sevinç bitince acı yine görünebilir.
Ngakhale poseka mtima utha kumva kuwawa, ndipo mathero achimwemwe akhoza kukhala chisoni.
14 Yüreği dönek olan tuttuğu yolun, İyi kişi de yaptıklarının ödülünü alacaktır.
Munthu wosakhulupirika adzalandira zogwirizana ndi ntchito yake, koma munthu wabwino adzalandira mphotho ya ntchito yake.
15 Saf kişi her söze inanır, İhtiyatlı olansa attığı her adımı hesaplar.
Munthu wopusa amakhulupirira chilichonse, koma munthu wochenjera amaganizira bwino mayendedwe ake.
16 Bilge kişi korktuğu için kötülükten uzaklaşır, Akılsızsa büyüklük taslayıp kendine güvenir.
Munthu wanzeru amaopa Mulungu ndipo amapewa zoyipa, koma munthu wopusa ndi wokula mtima amakhala wosasamala.
17 Çabuk öfkelenen ahmakça davranır, Düzenbazdan herkes nefret eder.
Munthu wopsa mtima msanga amachita zinthu za uchitsiru, ndipo anthu amadana ndi munthu wachinyengo.
18 Saf kişilerin mirası akılsızlıktır, İhtiyatlı kişilerin tacı ise bilgidir.
Anthu opusa amalandira uchitsiru, koma anthu ochenjera amavekedwa chipewa cha ulemerero wa kudziwa zinthu.
19 Alçaklar iyilerin önünde, Kötüler doğruların kapısında eğilirler.
Anthu oyipa adzagwada pamaso pa anthu abwino, ndipo anthu oyipa adzapempha thandizo kwa anthu olungama.
20 Komşusu bile yoksulu sevmez, Oysa zenginin dostu çoktur.
Munthu wosauka ngakhale anansi ake omwe amamuda, koma munthu wolemera ali ndi abwenzi ambiri.
21 Komşuyu hor görmek günahtır, Ne mutlu mazluma lütfedene!
Wonyoza mnansi wake ndi wochimwa koma ndi wodala amene amachitira chifundo anthu osowa.
22 Kötülük tasarlayan yolunu şaşırmaz mı? Oysa iyilik tasarlayan sevgi ve sadakat kazanır.
Kodi amene amakonzekera zoyipa sasochera? Koma amene amakonzekera zabwino anthu amawaonetsa chikondi ndi kukhulupirika.
23 Her emek kazanç getirir, Ama boş lakırdı yoksulluğa götürür.
Ntchito iliyonse imakhala ndi phindu, koma kuyankhulayankhula kumabweretsa umphawi.
24 Bilgelerin tacı servetleridir, Akılsızlarsa ahmaklıklarıyla tanınır.
Chipewa chaulemu cha anthu a nzeru ndi chuma chawo chomwe, koma malipiro a zitsiru ndi uchitsiru.
25 Dürüst tanık can kurtarır, Yalancı tanık aldatıcıdır.
Mboni yokhulupirika imapulumutsa miyoyo, koma mboni yabodza imaphetsa.
26 RAB'den korkan tam güvenliktedir, RAB onun çocuklarına da sığınak olacaktır.
Amene amaopa Yehova ali ndi chitetezo chokwanira ndipo iye adzakhala pothawira pa ana ake.
27 RAB korkusu yaşam kaynağıdır, İnsanı ölüm tuzaklarından uzaklaştırır.
Kuopa Yehova ndiye kasupe wamoyo, kumathandiza munthu kuti apewe msampha wa imfa.
28 Kralın yüceliği halkının çokluğuna bağlıdır, Halk yok olursa hükümdar da mahvolur.
Gulu lalikulu la anthu ndiye ulemerero wa mfumu, koma popanda anthu kalonga amawonongeka.
29 Geç öfkelenen akıllıdır, Çabuk sinirlenen ahmaklığını gösterir.
Munthu wosapsa mtima msanga amamvetsa zinthu kwambiri, koma munthu wopsa mtima msanga amaonetsa uchitsiru wake.
30 Huzurlu yürek bedenin yaşam kaynağıdır, Hırs ise insanı için için yer bitirir.
Mtima wodekha umapatsa thupi moyo, koma nsanje imawoletsa mafupa.
31 Muhtacı ezen, Yaradanı'nı hor görüyor demektir. Yoksula acıyansa Yaradan'ı yüceltir.
Amene amapondereza mʼmphawi amanyoza mlengi wake, koma wochitira chifundo munthu wosowa amalemekeza Mulungu.
32 Kötü kişi uğradığı felaketle yıkılır, Doğru insanın ölümde bile sığınacak yeri var.
Anthu oyipa adzakanthidwa chifukwa cha ntchito zawo zomwe, koma olungama adzatetezedwa mwa imfa yawo.
33 Bilgelik akıllı kişinin yüreğinde barınır, Akılsızlar arasında bile kendini belli eder.
Nzeru zimakhala mu mtima mwa anthu omvetsa zinthu, koma nzeru sipezeka mu mtima mwa zitsiru.
34 Doğruluk bir ulusu yüceltir, Oysa günah herhangi bir halk için utançtır.
Chilungamo chimakweza mtundu wa anthu, koma uchimo umachititsa manyazi mtundu uliwonse.
35 Kral sağduyulu kulunu beğenir, Utanç getirene öfkelenir.
Mfumu imasangalatsidwa ndi wantchito wanzeru, koma imachitira ukali wantchito wochititsa manyazi.

< Süleyman'In Özdeyişleri 14 >