< Çölde Sayim 5 >

1 RAB Musa'ya şöyle dedi:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 “İsrail halkına de ki, deri hastalığı veya akıntısı olan ya da ölüye dokunduğundan kirli sayılan herkesi ordugahın dışına çıkarsınlar.
“Lamula Aisraeli kuti achotse mu msasa aliyense amene ali ndi matenda opatsirana a pa khungu kapena matenda otuluka madzi mʼthupi a mtundu uliwonse, kapena aliyense wodetsedwa chifukwa cha munthu wakufa.
3 Erkeği de kadını da çıkaracaksınız. Aralarında yaşadığım ordugahlarını kirletmemeleri için onları ordugahın dışına çıkaracaksınız.”
Muchotse amuna komanso amayi ndipo muwatulutsire kunja kwa msasa kuti asadetse msasa wawo kumene Ine ndimakhala pakati pawo.”
4 İsrail halkı denileni yaparak RAB'bin Musa'ya buyurduğu gibi onları ordugahın dışına çıkardı.
Aisraeli anachitadi zimenezi. Anawatulutsira kunja kwa msasa monga momwe Yehova analamulira Mose.
5 RAB Musa'ya şöyle dedi:
Yehova anati kwa Mose,
6 “İsrail halkına de ki, ‘Bir erkek ya da kadın, insanın işleyebileceği günahlardan birini işler, RAB'be ihanet ederse o kişi suçlu sayılır.
“Uza Aisraeli kuti, ‘Pamene mwamuna kapena mayi walakwira mnzake mwa njira iliyonse, ndiye kuti ndi wosakhulupirika pamaso pa Yehova. Munthuyo ndi wochimwa ndithu ndipo
7 İşlediği günahı itiraf etmeli. Karşılığını, beşte birini üzerine ekleyerek suç işlediği kişiye ödeyecek.
ayenera kuwulula tchimo limene anachitalo. Ayenera kubweza zonse zimene anawononga, ndipo awonjezerepo chimodzi mwa magawo asanu ndi kuzipereka kwa munthu amene anamulakwirayo.
8 Eğer kişinin işlenen suçun karşılığını alacak bir yakını yoksa, suçun karşılığı RAB'be ait olacak. Günahın bağışlanması için sunulan bağışlamalık koçla birlikte suçun karşılığı da kâhine verilecek.
Ngati wolakwiridwayo alibe mʼbale komwe kungapite zinthu zobwezedwazo, zinthuzo zikhale za Yehova ndipo azipereke kwa wansembe, pamodzi ndi nkhosa yayimuna ya nsembe yopepesera tchimo lake.
9 İsrail halkının kâhine sunduğu kutsal armağanların bağış kısımları kâhinin olacak.
Zopereka zonse zopatulika zomwe Aisraeli abwera nazo kwa wansembe zikhale za wansembeyo.
10 Herkesin kendine ayırdığı sunular kendinin, ama kâhine verdikleri kâhinin olacaktır.’”
Mphatso zilizonse zopatulika ndi za munthuyo, koma zomwe wapereka kwa wansembe ndi za wansembeyo.’”
11 RAB Musa'ya şöyle dedi:
Kenaka Yehova anawuza Mose kuti,
12 “İsrail halkına de ki, ‘Eğer bir adamın karısı yoldan çıkar, ona ihanet eder,
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati mkazi wa munthu wina ayenda njira yosayenera nakhala wosakhulupirika kwa mwamuna wake,
13 başka bir adamla yatar, kirlendiği halde bu olayı kocasından gizlerse ve tanık olmadığı için kadının yaptığı ortaya çıkmazsa,
nakagonana ndi mwamuna wina koma mwamuna wake wosadziwa, ndipo palibe wina aliyense wadziwa za kudzidetsa kwake (pakuti palibe mboni yomuneneza chifukwa sanagwidwe akuchita),
14 koca karısını kıskanır, ona karşı yüreğinde kuşku uyanırsa, kadın suçluysa ya da suçlu olmadığı halde kocası onu kıskanır, ona karşı yüreğinde kuşku uyanırsa,
mwamuna wake ndi kuyamba kuchita nsanje ndi kukayikira mkazi wakeyo kuti ndi wodetsedwa, komanso ngati amuchitira nsanje ndi kumukayikira ngakhale asanadzidetse,
15 adam karısını kâhine götürecek. Karısı için sunu olarak onda bir efa arpa unu alacak. Üzerine zeytinyağı dökmeyecek, günnük koymayacak. Çünkü bu kıskançlık sunusudur. Suçu anımsatan anımsatma sunusudur.
apite naye mkaziyo kwa wansembe. Ndipo popita atengenso gawo lakhumi la chopereka chaufa wa barele wokwana kilogalamu imodzi mʼmalo mwa mkaziyo. Asathire mafuta pa nsembeyo kapena lubani, chifukwa ndi nsembe ya chopereka ya chakudya yopereka chifukwa cha nsanje, nsembe yozindikiritsa tchimo.’”
16 “‘Kâhin kadını öne çağırıp RAB'bin önünde durmasını sağlayacak.
“‘Wansembe abwere naye mkaziyo ndi kumuyimitsa pamaso pa Yehova.
17 Sonra, toprak bir kabın içine kutsal su koyacak. Konutun kurulu olduğu yerden biraz toprak alıp suya katacak.
Ndipo wansembeyo atenge madzi oyera mʼmbiya ya dothi ndi kuyika mʼmadzimo fumbi lapansi la mʼTenti ya Msonkhano.
18 Kadını RAB'bin önünde durdurduktan sonra onun saçını açacak, anımsatma sunusu, yani kıskançlık sunusunu eline verecek. Kendisi de lanet getiren acı suyu elinde tutacak.
Wansembe atayimika mkaziyo pamaso pa Yehova, amumasule tsitsi lake, ndipo ayike mʼmanja mwake nsembe yozindikiritsa tchimo, nsembe yachakudya ya nsanje, wansembeyo atanyamula madzi owawa omwe amabweretsa temberero.’
19 Sonra kadına ant içirtip şöyle diyecek: Eğer başka bir adam seninle yatmadıysa, kocanla evliyken yoldan çıkıp günah işlemediysen, lanet getiren bu acı su sana zarar vermesin.
Kenaka wansembeyo alumbiritse mkaziyo ndi kuti, ‘Ngati mwamuna wina aliyense sanagonane ndi iwe ndipo sunayende njira yoyipa ndi kukhala wodetsedwa pomwe uli pa ukwati ndi mwamuna wako, madzi owawa awa omwe amabweretsa temberero asakupweteke.
20 Ama kocanla evliyken yoldan çıkıp başka biriyle yatarak günah işlediysen
Koma ngati wayenda njira yoyipa uli pa ukwati ndi mwamuna wako ndi kudzidetsa pogonana ndi mwamuna amene si mwamuna wako,’
21 –kâhin kadına lanet andı içirtip şöyle diyecek– RAB sana eriyen kalça, şişen karın versin. RAB halkın arasında seni lanetli ve iğrenç duruma düşürsün.
pamenepo wansembe alumbiritse mkaziyo ndi mawu a matemberero ndi kumuwuza kuti, ‘Yehova achititse anthu ako kukutemberera ndi kukunyoza pamene awononga ntchafu yako ndi kutupitsa mimba yako.
22 Lanet getiren bu su karnına girince karnını şişirsin, kalçanı eritsin. “‘O zaman kadın, Amin, amin, diyecek.
Madzi awa obweretsa temberero alowe mʼthupi mwako ndi kutupitsa mimba yako ndi kuwononga ntchafu yako.’” “Pamenepo mkaziyo anene kuti, ‘Ameni, ameni.’”
23 “‘Kâhin bu lanetleri bir kitaba yazıp acı suda yıkayacak.
“‘Wansembe alembe matemberero amenewa mʼbuku ndi kuwanyika mʼmadzi owawa aja.
24 Lanet getiren acı suyu kadına içirecek. Su kadının içine girince acılık verecek.
Amwetse mkaziyo madzi owawawo omwe amabweretsa temberero, ndipo madzi amenewo adzalowa mʼmimba mwake ndi kuyambitsa ululu woopsa.
25 Kâhin kadının elinden kıskançlık sunusunu alacak, RAB'bin huzurunda salladıktan sonra sunağa getirecek.
Wansembe achotse mʼmanja mwa mkaziyo nsembe yachakudya ya nsanje ija, nayiweyula pamaso pa Yehova ndi kuyipereka pa guwa lansembe.
26 Kadının anma payı olarak sunudan bir avuç alıp sunakta yakacak. Sonra kadına suyu içirecek.
Tsono wansembeyo atapeko ufa dzanja limodzi kuti ukhale wachikumbutso ndi kuwutentha pa guwa lansembe. Atatha izi, amwetse mkaziyo madzi aja.
27 Eğer kadın kocasına ihanet etmiş, kendini kirletmişse, lanet getiren suyu içince acı duyacak; karnı şişip kalçası eriyecek. Halkı arasında lanetli olacak.
Ndipo ngati mkaziyo anadzidetsadi ndi kukhala wosakhulupirika kwa mwamuna wake, pamene amwa madzi obweretsa matemberero aja, nalowa mʼmimba mwake, adzamva ululu woopsa. Mimba yake idzatupa ndi ntchafu yake idzawonongeka ndipo adzakhala wotembereredwa pakati pa anthu ake.
28 Ama kendini kirletmemişse, temizse, zarar görmeyecek, çocuk doğurabilecek.
Koma ngati mkaziyo sanadzidetse ndi kuti alibe tchimo, adzakhala wopanda mlandu ndipo adzabereka ana.
29 “‘Kıskançlık yasası budur. Bir kadın yoldan çıkar, kocasıyla evliyken kendini kirletirse,
“‘Limeneli ndiye lamulo la nsanje pamene mkazi wayenda njira yoyipa ndi kudzidetsa ali pa ukwati ndi mwamuna wake,
30 ya da bir koca karısını kıskanır, ona karşı yüreğinde kuşku uyanırsa, kâhin kadını RAB'bin önünde durduracak, bu yasayı ona uygulayacak.
kapena pamene maganizo a nsanje abwera kwa mwamuna wake chifukwa chokayikira mkazi wakeyo. Wansembe azitenga mkazi wotere ndi kumuyimiritsa pamaso pa Yehova ndipo agwiritse ntchito lamulo lonseli kwa mkaziyo.
31 Kocası herhangi bir suçtan suçsuz sayılacak, kadınsa suçunun cezasını çekecek.’”
Mwamunayo adzakhala wopanda tchimo lililonse, koma mkaziyo adzasenza zotsatira za tchimo lake.’”

< Çölde Sayim 5 >